Danieli 2 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 2:1-49

Maloto a Nebukadinezara

1Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona. 2Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu, 3mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”

4Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”

5Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja. 6Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”

7Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”

8Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita. 9Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”

10Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi. 11Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”

12Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe. 13Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.

14Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni. 15Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli. 16Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.

17Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya. 18Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni. 19Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba, 20ndipo anati:

“Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi;

nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.

21Amasintha nthawi ndi nyengo;

amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso.

Amapatsa nzeru kwa anzeru

ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.

22Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika;

amadziwa zimene zili mu mdima,

ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.

23Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga:

mwandipatsa nzeru ndi mphamvu,

mwandiwululira zomwe tinakupemphani,

mwatiwululira maloto a mfumu.”

Danieli Atanthauzira Maloto

24Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”

25Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”

26Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”

27Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa, 28koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:

29“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika. 30Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.

31“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe. 32Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa. 33Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo. 34Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya. 35Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.

36“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu. 37Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero; 38Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.

39“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi. 40Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse. 41Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita. 42Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka. 43Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.

44“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya. 45Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa.

“Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”

46Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani. 47Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”

48Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru. 49Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.

New Serbian Translation

Књига пророка Данила 2:1-49

Навуходоносоров сан

1У другој години своје владавине, Навуходоносор2,1 603. пре Христа. је сањао снове. Он се толико узнемирио, да му сан није долазио на очи. 2Цар је наредио да се позову чаробњаци, гатари, врачари и Халдејци2,2 Халдејци су били на гласу по астролошким и магијским вештинама, па се ови окултисти у царевој служби називају именом ове етничке групе., да кажу цару шта је сањао. Кад су дошли, стали су пред цара.

3Цар им рече: „Сањао сам сан и узнемирен сам; хоћу да знам шта тај сан значи.“

4Халдејци одговорише цару на арамејском: „О, царе, да си жив довека! Испричај сан својим слугама, а ми ћемо протумачити његово значење.“

5Цар одговори Халдејцима: „Издајем проглас: ако ми не кажете какав сам сан имао и шта је његово тумачење, бићете растргнути на делове, а ваше куће лежаће у рушевинама. 6А ако ми кажете какав сам сан имао и шта је његово значење, добићете од мене дарове, награде и велику почаст. Стога ми реците шта је био мој сан и протумачите његово значење.“

7Они му опет одговорише: „Нека цар исприча сан својим слугама, а ми ћемо протумачити његово значење.“

8Али цар им одговори: „Знам ја поуздано да хоћете да добијете на времену, пошто видите да сам издао проглас, 9да ако ми не кажете какав сам сан имао, постоји само једна пресуда за вас. Ви сте се договорили да ми саопштите лажљиве и заводљиве речи, док се прилике не промене. Стога ми реците какав сам сан имао, а ја ћу знати да ли сте протумачили његово значење.“

10Халдејци одговорише цару: „Нема на земљи човека који би могао да разјасни што цар захтева. Никада један цар, било како да је велики и моћан, није тражио тако нешто од чаробњака, гатара и Халдејаца. 11Тешко је то што цар захтева; не постоји нико ко би то могао да открије цару осим богова који не бораве међу људима.“

12Због свега овога цар се толико разгневио да је наредио да се побију сви мудраци у Вавилону. 13Кад је била издана наредба да се побију сви мудраци, тражили су и Данила и његове другове да их убију.

14Тада се Данило обратио мудрим и разборитим речима Ариоху, заповеднику цареве телесне страже, који је изашао да побије вавилонске мудраце. 15Упитао је царевог заповедника Ариоха: „Зашто је царева наредба толико строга?“ Ариох обавести Данила. 16На то је Данило отишао цару и тражио од цара да му да време како би могао да протумачи значење сна.

17После тога је Данило отишао својој кући и обавестио о томе Ананију. Мисаила и Азарију, 18како би тражили милост Бога небеског у погледу ове тајне, да не би и Данило и његови другови настрадали са вавилонским мудрацима.

19Та је тајна била откривена Данилу ноћу, у виђењу. Данило је благословио Бога небеског. 20Данило рече:

„Нека је благословено име Божије од века до века;

њему припада мудрост и сила.

21Он мења времена и доба,

уклања и поставља цареве;

мудрима даје мудрост,

и разумнима знање.

22Он открива ствари дубоке и тајне,

он зна шта је у тами,

и светло с њим пребива.

23Хвалим те и славим, Боже отаца мојих,

јер ми дајеш мудрост и силу:

што сам тражио од тебе,

ти си ми открио,

обзнанио нам што је цар тражио.“

Данило тумачи сан

24Данило је отишао к Ариоху, кога је цар одредио да побије вавилонске мудраце и рекао му: „Не убијај вавилонске мудраце; одведи ме пред цара, а ја ћу цару протумачити значење сна.“

25Ариох је одмах довео Данила пред цара и рекао му: „Нашао сам међу Јудиним изгнаницима човека који може цару да објасни значење сна!“

26Цар упита Данила, коме је име било и Валтазар: „Да ли стварно можеш да ми кажеш какав сам сан имао, и протумачиш га?“

27Данило одговори цару: „Тајну, за коју цар пита, не могу расветлити мудраци, гатари, чаробњаци и звездознанци, 28али постоји Бог на небу који открива тајне. Он је обзнанио цару Навуходоносору шта ће се догодити у данима што долазе. Ово је твој сан, ово су виђења, која су ти дошла на ум на твојој постељи:

29Теби су, о, царе, дошле мисли на твојој постељи о стварима које ће се догодити касније, а онај што открива тајне објавио ти је шта ће се догодити. 30Ова тајна ми је била откривена не зато што имам више мудрости од свих живих, него да би цар сазнао њено значење, и да би дознао какве су ти мисли дошле на ум.

31Ти си, о, царе, видео велики кип. Кип је био огроман и изванредно блистав. Стајао је испред тебе, а изглед му је био застрашујући. 32Глава кипа је била од чистог злата, прса и руке од сребра, трбух и бедра од бронзе, 33ноге од гвожђа, а стопала делом од гвожђа, делом од глине. 34Док си ти гледао, одвалио се један камен, али не људским рукама, ударио кип у стопала од гвожђа и глине и разбио их. 35Истог часа су се смрвили и гвожђе и глина, бронза, сребро и злато. Постали су као плева на гумну у лето; дунуо је ветар и све их однео без трага. А камен који је ударио у кип постао је велика планина, која је испунила сву земљу.

36То је сан. Сада ћемо саопштити цару његово тумачење. 37Ти си, царе, цар над царевима, коме је Бог небески дао царство, силу, моћ и славу. 38У твоје руке је предао људе, свуда где живе, звери пољске и птице небеске, и учинио те владарем над свима њима. Ти си та глава од злата.

39После тебе ће настати друго царство, мање од твог, па треће царство, од бронзе, које ће владати над свом земљом. 40Четврто царство ће бити чврсто као гвожђе, као гвожђе које све ломи и мрви. Као што гвожђе све сатире, тако ће оно разбити и сатрти сва та царства. 41То што си видео да су стопала и прсти делом од глине, а делом од гвожђа, значи да ће се то царство поделити. Ипак, у њему ће остати нешто од чврстине гвожђа, јер си видео гвожђе помешано са глином. 42А то што су прсти на стопалима делом од гвожђа, а делом од глине, значи да ће царство бити делом јако, делом крхко. 43Видео си и да је гвожђе помешано са обичном глином. То значи да ће се мешати са семеном других народа, али да се неће одржати заједно, као што се ни гвожђе не може помешати с глином.

44У време тих царева Бог небески ће успоставити царство, које никада неће бити уништено, нити ће се то царство оставити другом народу. Оно ће разбити и окончати сва она царства, а са̂мо ће остати довека, 45баш као што си видео да се одвалио камен, али не људском руком, и смрвио гвожђе, бронзу, глину, сребро и злато.

Велики Бог је обзнанио цару шта ће се догодити касније. Сан је истинит, а тумачење му је поуздано.“

46Тада цар Навуходоносор паде ничице, поклони се Данилу и нареди да му се принесу житна жртва и кад. 47Цар рече Данилу: „Твој Бог је, заиста, Бог над боговима, господар царевима и Откриватељ тајни, кад си могао да откријеш ову тајну.“

48Цар је узвисио Данила, и дао му много великих дарова. Поставио га је за управитеља све вавилонске области и главара свих вавилонских мудраца. 49Но, Данило је замолио цара да послове вавилонске области повери Седраху, Мисаху и Авденагу. Са̂м Данило је остао на царевом двору.