Chivumbulutso 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 22:1-21

Mtsinje Wamoyo

1Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa, 2Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina. 3Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira. 4Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo. 5Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya.

6Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”

Yesu Akubweranso

7“Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”

8Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi. 9Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”

10Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira. 11Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”

Mawu Otsiriza: Kuyitanidwa ndi Chenjezo

12“Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita. 13Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.

14“Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo. 15Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.

16“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”

17Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.

18Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili. 19Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”

20Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.”

Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.

21Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.

New Russian Translation

Откровение 22:1-21

Река жизни

1Затем ангел показал мне реку воды жизни, блестящую, как кристалл, и текущую от трона Бога и Ягненка 2посредине центральной улицы города. По обе стороны реки растет дерево жизни. Оно плодоносит двенадцать раз в год, давая каждый месяц свой плод, а листья дерева предназначены для исцеления народов22:2 См. Иез. 47:12; Ср. Быт. 2:9-10.. 3И там уже больше не будет ничего проклятого22:3 См. Быт. 3:14-19; Зах. 14:11.. В городе будет находиться трон Бога и Ягненка, и Его слуги будут служить Ему. 4Они будут видеть Его лицо22:4 Ср. Исх. 33:20., и на лбу у них будет написано Его имя. 5Ночи больше не будет. Им уже не нужен будет свет ламп или свет солнца, потому что Господь Бог будет светить над ними. И они будут царствовать во веки веков22:5 См. Дан. 7:18, 27..

6Ангел сказал мне:

– Это верные и истинные слова. Господь Бог, вдохновляющий дух пророков, послал Своего ангела, чтобы показать Своим слугам то, что должно произойти вскоре.

Пришествие Иисуса

7– Вот, Я скоро приду! Блажен тот, кто соблюдает слова пророчества, записанные в этом свитке.

8Я, Иоанн, все это слышал и видел. И услышав и увидев все это, я пал к ногам ангела, показывающего мне все это, чтобы поклониться ему.

9Но он сказал мне:

– Не делай этого! Я такой же слуга, как и ты, как твои братья-пророки и как те, кто соблюдает слова, записанные в этом свитке. Поклонись Богу!

10Потом он сказал мне:

– Не запечатывай слов пророчества, записанных в этом свитке22:10 Ср. Дан. 12:4., потому что время уже близко. 11Кто поступает несправедливо, тот и будет продолжать поступать несправедливо. Кто ведет скверную жизнь, тот и будет продолжать вести скверную жизнь. Но тот, кто живет праведной жизнью, будет продолжать жить праведно, и тот, кто свят, будет продолжать жить свято22:11 См. Дан. 12:10; 2 Тим. 3:13..

12– Вот, Я скоро приду! Я несу воздаяние каждому, и каждый получит по своим делам. 13Я – Альфа и Омега, Первый и Последний22:13 См. Ис. 44:6; 48:12. Здесь мы видим, что Иисус говорит о Себе так, как говорил о Себе Сам Бог., Начало и Конец. 14Блаженны те, кто омывает свои одежды, чтобы им иметь право питаться от дерева жизни и войти в город через ворота. 15А снаружи останутся псы22:15 Псы – Писание часто называет псами тех, кто делает неугодное в глазах Бога (см. Втор. 23:17-18; Пс. 21:17; Флп. 3:2)., колдуны, развратники, убийцы, идолопоклонники и все любящие и творящие неправду.

16Я, Иисус, послал Моего ангела, чтобы передать вам это свидетельство для церквей. Я – Корень22:16 Или: «росток». и Потомок Давида, Я – яркая Утренняя Звезда22:16 См. Чис. 24:17; Ис. 11:1, 10..

17Дух и невеста говорят:

– Приди!

И каждый, кто это слышит, пусть тоже скажет:

– Приди!

Пусть приходит мучимый жаждой! Кто хочет, пусть берет воду жизни даром!22:17 См. Ис. 55:1; Ин. 7:37.

18И я предупреждаю каждого, кто слышит слова пророчества, записанные в этом свитке: кто добавит что-либо к этим словам, тому Бог добавит и бедствия, о которых написано в этом свитке. 19И если кто отнимет что-либо из слов пророчества, записанных в этом свитке, у того и Бог отнимет право питаться от дерева жизни и жить в святом городе, которые описаны в этом свитке22:18-19 См. Втор. 4:2; 12:32; Прит. 30:6..

20Свидетельствующий об этом говорит:

– Да, Я скоро приду!

Аминь! Приди, Господь Иисус!

21Пусть благодать Господа Иисуса будет со всеми22:21 В ряде древних рукописей: «со всеми святыми»..

Аминь.