Chivumbulutso 22 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 22:1-21

Mtsinje Wamoyo

1Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa, 2Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina. 3Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira. 4Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo. 5Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya.

6Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”

Yesu Akubweranso

7“Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”

8Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi. 9Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”

10Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira. 11Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”

Mawu Otsiriza: Kuyitanidwa ndi Chenjezo

12“Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita. 13Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.

14“Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo. 15Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.

16“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”

17Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.

18Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili. 19Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”

20Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.”

Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.

21Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Откровение 22:1-21

Река жизни

1Затем ангел показал мне реку воды жизни, блестящую, как кристалл, и текущую от трона Аллаха и Ягнёнка 2посредине центральной улицы города. По обе стороны реки растут деревья жизни. Они плодоносят двенадцать раз в год, давая каждый месяц свой плод, а листья деревьев предназначены для исцеления народов22:2 См. Езек. 47:12; ср. Нач. 2:9-10.. 3И там уже больше не будет ничего проклятого22:3 См. Нач. 3:14-19; ср. Зак. 14:11.. В городе будет находиться трон Аллаха и Ягнёнка, и Его рабы будут служить Ему. 4Они будут видеть Его лицо22:4 Ср. Исх. 33:20., и на лбу у них будет написано Его имя. 5Ночи больше не будет. Им уже не нужен будет свет ламп или свет солнца, потому что Вечный Бог будет светить над ними. И они будут царствовать вовеки22:5 См. Дан. 7:18, 27..

6Ангел сказал мне:

– Это верные и истинные слова. Вечный Бог, вдохновляющий дух пророков, послал Своего ангела, чтобы показать Своим рабам то, что должно произойти вскоре.

Пришествие Исы аль-Масиха

7– Вот Я скоро приду! Благословен тот, кто соблюдает слова пророчества, записанные в этом свитке.

8Я, Иохан, всё это слышал и видел. И, услышав и увидев, я пал к ногам ангела, показывающего мне всё это, чтобы поклониться ему.

9Но ангел говорит мне:

– Не делай этого! Я такой же раб, как и ты, как твои братья пророки и как те, кто соблюдает слова, записанные в этом свитке. Поклонись Аллаху!

10Потом он говорит мне:

– Не запечатывай слов пророчества, записанных в этом свитке22:10 Ср. Дан. 12:4, 9., потому что время уже близко. 11Кто поступает несправедливо, тот и будет продолжать поступать несправедливо. Кто ведёт скверную жизнь, тот и будет продолжать вести скверную жизнь. Но тот, кто живёт праведной жизнью, будет продолжать жить праведно, и тот, кто свят, будет продолжать жить свято22:11 См. Дан. 12:10; 2 Тим. 3:13..

12– Вот Я скоро приду! Я несу воздаяние каждому, и каждый получит по своим делам. 13Я – Владыка всего: от А до Я, Первый и Последний22:13 См. Ис. 44:6; 48:12. Здесь Иса говорит о Себе так, как говорил о Себе Сам Всевышний., Начало и Конец. 14Благословенны те, кто омывает свои одежды, чтобы им иметь право питаться от дерева жизни и войти в город через ворота. 15А снаружи останутся псы22:15 Священное Писание часто называет псами тех, кто делает неугодное в глазах Аллаха (см. Втор. 23:17-18; Заб. 21:17; Флп. 3:2)., колдуны, развратники, убийцы, идолопоклонники и все любящие и творящие неправду.

16Я, Иса, послал Моего ангела, чтобы передать вам это свидетельство для общин верующих. Я – Корень22:16 Или: «Росток». и Потомок Давуда, Я – яркая Утренняя Звезда22:16 См. Чис. 24:17; Ис. 11:1, 10..

17Дух Аллаха и невеста говорят Исе:

– Приди!

И каждый, кто это слышит, пусть тоже скажет:

– Приди!

Пусть приходит мучимый жаждой! Кто хочет, пусть берёт воду жизни даром!22:17 См. Ис. 55:1; Ин. 7:37.

18И я предупреждаю каждого, кто слышит слова пророчества, записанные в этом свитке: кто добавит что-либо к этим словам, тому Аллах добавит и бедствия, о которых написано в этом свитке. 19И если кто отнимет что-либо из слов пророчества, записанных в этом свитке, у того и Аллах отнимет право питаться от дерева жизни и жить в святом городе, которые описаны в этом свитке22:18-19 См. Втор. 4:2; 12:32; Мудр. 30:6..

20Свидетельствующий об этом говорит:

– Да, Я скоро приду!

Да будет так! Приди, Повелитель Иса!

21Пусть благодать Повелителя Исы будет со всеми.

Аминь.