Chivumbulutso 2 – CCL & PCB

The Word of God in Contemporary Chichewa

Chivumbulutso 2:1-29

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Efeso

1“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide. 2Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza. 3Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.

4Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba. 5Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake. 6Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.

7Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Simurna

8“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo. 9Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana. 10Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.

11Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Pergamo

12“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse. 13Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.

14Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo. 15Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai. 16Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.

17Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’ ”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Tiyatira

18“Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira. 19Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.

20Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano. 21Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna. 22Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo. 23Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.

24Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena. 25Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.

26Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu. 27Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga. 28Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija. 29Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.

Persian Contemporary Bible

مکاشفه 2:1-29

پیام مسیح به کلیسای اَفِسُس

1«این پیام را برای فرشتۀ2‏:1 یا: پیام‌آور؛ همچنین در ۲‏:۸، ۱۲، ۱۸. کلیسای اَفِسُس بنویس:

آنکه هفت ستاره را در دست راست خود دارد و در میان هفت شمعدان طلا قدم می‌زند، این پیام را برای تو دارد:

2از اعمال نیک و زحمات و صبر تو آگاهم. می‌دانم که از هیچ گناهی در میان اعضای خود چشم‌پوشی نمی‌کنی و ادعای کسانی را که می‌گویند فرستادهٔ خدایند، به دقت سنجیده‌ای و پی برده‌ای که دروغ می‌گویند. 3تو به خاطر من رنج و زحمت کشیده‌ای و مقاومت کرده‌ای.

4با این حال، ایرادی در تو می‌بینم: تو محبت نخستین خود را ترک کرده‌ای. 5پس به یاد آور از کجا سقوط کرده‌ای. برگرد پیش من و کارهایی را به جا آور که در ابتدا به جا می‌آوردی. اگر توبه نکنی، خواهم آمد و شمعدان تو را از میان کلیساها برخواهم داشت.

6اما نکتهٔ خوبی در تو هست: تو نیز مانند من از رفتار نیکولاییان متنفر هستی.

7هر که این را می‌شنود، خوب توجه کند که روح خدا به کلیساها چه می‌گوید: هر که پیروز شود، به او اجازه خواهم داد از میوهٔ درخت حیات که در باغ خداست بخورد.

پیام مسیح به کلیسای اسمیرنا

8«این پیام را برای فرشتۀ کلیسای اسمیرنا بنویس:

این پیام کسی است که اول و آخر است و مُرد ولی اکنون زنده است:

9از سختیها، زحمات و فقر تو آگاهم، ولی تو ثروتمندی! از کفرهایی که مخالفانت می‌گویند نیز باخبرم. ایشان خود را یهودی می‌خوانند، اما نیستند، زیرا از کنیسۀ شیطانند. 10از زحمات و مشکلاتی که در پیش داری، نترس! به‌زودی ابلیس بعضی از شما را به زندان خواهد افکند تا شما را بیازماید. شما به مدت ده روز آزار و زحمت خواهید دید، اما تا پای مرگ وفادار بمانید تا تاج زندگی جاوید را بر سر شما بگذارم.

11هر که این را می‌شنود، خوب توجه کند که روح خدا به کلیساها چه می‌گوید: هر که پیروز شود، از مرگ دوم آسیبی نخواهد دید.

پیام مسیح به کلیسای پرگاموم

12«این پیام را برای فرشتۀ کلیسای پِرگاموم بنویس:

این پیام کسی است که می‌داند شمشیر دو دم تیز خود را چگونه به کار برد:

13می‌دانم که در شهری به سر می‌بری که مقرّ حکومت شیطان است و مردم شیطان را می‌پرستند. با این حال، به من وفادار مانده‌ای و مرا انکار نکرده‌ای؛ حتی زمانی که آنتیپاس، شاهد وفادار من، به دست هواداران شیطان شهید شد، تو نسبت به من امین ماندی.

14با وجود این، چند ایراد در تو می‌بینم. تو زیر بار تعالیم غلط کسانی می‌روی که مانند بلعام هستند که به بالاق یاد داد چگونه قوم اسرائیل را به گناه بکشاند. طبق راهنمایی‌های بلعام، قوم اسرائیل را به بی‌عفتی و خوردن خوراکهایی که به بتها تقدیم شده بود، تشویق کردند. 15در میان شما نیز کسانی از نیکولاییان هستند که از همان تعلیم پیروی می‌کنند. 16پس از گناهت توبه کن، و گرنه ناگهان نزد تو خواهم آمد و با شمشیر دهانم با آنان خواهم جنگید.

17هر که این را می‌شنود، خوب توجه کند که روح خدا به کلیساها چه می‌گوید: هر که پیروز شود، از ”مَنّای“ مخفی در آسمان به او خواهم داد؛ و من به او سنگ سفیدی خواهم بخشید که بر آن نام جدیدی نوشته شده است، نامی که هیچ‌کس از آن باخبر نیست، غیر از کسی که آن را دریافت می‌کند.

پیام مسیح برای کلیسای تیاتیرا

18«این پیام را برای فرشتۀ کلیسای تیاتیرا بنویس:

این پیام پسر خداست که چشمانش همچون شعله‌های آتش و پاهایش مانند مس صیقلی است:

19من از اعمال تو، از محبت و ایمان و خدمت و پایداری تو آگاهم. می‌دانم که در تمام این امور بیش از پیش ترقی می‌کنی. 20با این حال، ایرادی در تو می‌بینم: تو، به آن زن، ایزابل که ادعا می‌کند نبیه است، اجازه می‌دهی تا تعالیم غلط بدهد و باعث شود که خدمتگزاران من از راه راست منحرف شوند و به بی‌عفتی کشیده شده، خوراکهایی را بخورند که برای بتها قربانی شده‌اند. 21من به او فرصت دادم تا توبه کرده، راهش را تغییر دهد؛ اما نخواست. 22پس او را با تمام مریدان فاسدش، بر بستر بیماری خواهم انداخت و به مصیبتی سخت دچار خواهم ساخت، مگر اینکه به سوی من بازگردند و از گناهانی که با او کرده‌اند، دست بکشند؛ 23فرزندانش را نیز از بین خواهم برد. آنگاه همهٔ کلیساها خواهند دانست که من اعماق قلب انسانها را جستجو می‌کنم و از افکار همه آگاهم. من به هر کس مطابق اعمالش پاداش و جزا خواهم داد.

24‏-25و اما از بقیهٔ شما که در تیاتیرا هستید و به دنبال این تعالیم غلط نرفته‌اید، انتظار و درخواست دیگری ندارم. منظورم از تعالیم غلط، همان تعالیمی است که اسمش را ”حقایق عمیق“ گذاشته‌اند، که در واقع، چیزی نیست جز عمقهای شیطان! پس من انتظار دیگری از شما ندارم؛ فقط آنچه دارید محکم نگاه دارید تا بازگردم.

26هر که بر این مشکلات پیروز شود و تا زمان بازگشت من، به خواست و ارادهٔ من عمل کند، به او قدرت خواهم بخشید تا بر تمام قومها حکمرانی کند، 27و با عصای آهنین بر آنان حکومت نماید، همان‌گونه که پدرم نیز چنین قدرتی به من داد تا بر آنان سلطنت کنم. روزی همهٔ ایشان مانند کوزهٔ گلی خُرد خواهند شد. 28همچنین من ستارهٔ صبح را به او خواهم بخشید.

29هر که این را می‌شنود، خوب توجه کند که روح خدا به کلیساها چه می‌گوید.