Chivumbulutso 18 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 18:1-24

Kugwa kwa Babuloni

1Zitatha izi ndinaona mngelo wina akutsika kuchokera kumwamba. Iye anali ndi ulamuliro waukulu, ndipo dziko lapansi linawala ndi ulemerero. 2Mngeloyo anafuwula ndi mawu amphamvu kuti:

“ ‘Wagwa! Wagwa Babuloni Wamkulu!’

Wasandulika mokhalamo ziwanda

ndi kofikako mizimu yonse yoyipa

ndi mbalame zonse zonyansa

ndi zodetsedwa.

3Pakuti mayiko onse amwa

vinyo ozunguza mutu wazigololo zake.

Mafumu a dziko lapansi achita naye chigololo,

ndipo amalonda a dziko lapansi analemera kuchokera pa zolakalaka zake zosefukira.”

Awachenjeza kuti Athawe Chiweruzo cha Babuloni

4Ndiponso ndinamva mawu ena kuchokera kumwamba akuti:

“ ‘Anthu anga tulukani, mwa iye,’

mungachimwe naye

kuti musadzalandire nawo gawo lililonse la miliri yake;

5pakuti machimo ake awunjikana mpaka kumwamba,

ndipo Mulungu wakumbukira milandu yake.

6Bwezerani Iye monga momwe iye anakuchitirani.

Mubwezereni mowirikiza pa zimene anachita.

Mumusakanizire magawo awiri kuchokera mʼchikho chake.

7Mumuzunze, kumumvetsa chisoni kwambiri

monga mwaulemerero ndi zolakalaka

zimene anadzaza mu mtima mwake. Iye anadzikuza nʼkumati,

‘Ndinakhala monga mfumu yayikazi,

ine sindine wamasiye

ndipo sindidzalira maliro.’

8Chifukwa chake miliri yake idzamugonjetsa tsiku limodzi;

imfa, kulira maliro ndi njala.

Iye adzanyeka ndi moto

pakuti wamphamvu ndi Mulungu Ambuye amene wamuweruza.

Tsoka la Babuloni

9“Mafumu a dziko lapansi, amene anachita naye chigololo nachita naye pamodzi zosangalatsa moyo uno, akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzalira nakhuza maliro ake. 10Iwo adzayima kutali nalira chifukwa choopsedwa ndi mazunzo ake.

“ ‘Tsoka! Tsoka mzinda waukulu

iwe, Babuloni mzinda wamphamvu!

Mu ora limodzi chiwonongeko chako chafika!’

11“Amalonda a dziko lapansi adzalira nakhuza maliro ake chifukwa palibenso amene akugula katundu wawo, 12katundu wagolide, siliva, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale; nsalu zoyera kwambiri zapamwamba ndi zofiira; nsalu zasilika ndi zapepo; mitengo iliyonse yonunkhira ndi zinthu zilizonse zopangidwa ndi mnyanga, kapena matabwa ogulidwa ndi ndalama zambiri kapena mkuwa kapena chitsulo ndi mwala wonyezimira; 13zokometsera zakudya, mure, lubani ndi zofukiza zina, vinyo ndi mafuta a olivi, ufa wosalala ndi tirigu; ngʼombe ndi nkhosa; akavalo ndi ngolo; ndi anthu adzagulitsidwa ukapolo.

14“Iwo adzanena kuti, ‘Chipatso chimene unachilakalaka chakuchokera. Chuma chako chonse ndi ulemerero zatha, sizidzapezekanso.’ 15Amalonda amene anagulitsa zinthu izi napeza chuma kuchokera kwa iye adzayima patali potero ataopsedwa ndi mazunzo ake. Adzalira ndi kukhuza maliro 16ndipo adzalira mokuwa kuti,

“ ‘Tsoka! Tsoka! Mzinda waukulu,

iwe wovala nsalu zoyera kwambiri, zapepo ndi zofiira,

ndi wonyezimira ndi golide, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale!

17Chuma chambiri choterechi chafika powonongeka mu ora limodzi!’

“Oyendetsa sitima ndi onse oyenda pa sitima ya pamadzi, ogwira ntchito mʼsitima ndi onse amene amadalira nyanja pamoyo wa tsiku ndi tsiku adzayima patali potero. 18Akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzakuwa kuti, ‘Kodi panalinso mzinda wina ngati mzinda waukuluwu?’ 19Adzathira fumbi pamitu pawo ndipo adzalira nakhuza maliro kuti,

“Tsoka! Tsoka mzinda waukulu iwe,

kumene onse anali ndi sitima pa nyanja

analemera kudzera mʼchuma chake!

Mu ora limodzi wawonongedwa.

20“Kondwerani chifukwa cha iye inu kumwamba!

Kondwerani oyera mtima

ndi atumwi ndi aneneri!

Mulungu wamuweruza iye

monga momwe anakuchitirani inu.”

Chiwonongeko Chotsiriza cha Babuloni

21Kenaka mngelo wamphamvu ananyamula mwala waukulu ngati mphero yayikulu nawuponya mʼnyanja nanena kuti,

“Mwa mphamvu chonchi

mzinda waukulu wa Babuloni udzaponyedwa pansi,

sudzapezekanso.

22Mwa iwe simudzamvekanso liwu la woyimba zeze, ndi akatswiri a zoyimbayimba,

oyimba zitoliro, ndi lipenga.

Mwa iwe simudzapezekanso

mʼmisiri wina aliyense.

Mwa iwe simudzapezekanso

phokoso la mphero.

23Kuwala kwa nyale

sikudzawunikanso mwa inu.

Mawu a mkwati ndi mkwatibwi

sadzamvekanso mwa iwe.

Amalonda anu anali akuluakulu a dziko lapansi.

Mitundu yonse inasokonezedwa ndi zamatsenga zako.

24Mwa iye munapezeka magazi a aneneri ndi a oyera mtima,

ndi onse amene anaphedwa pa dziko lapansi.”

Священное Писание

Откровение 18:1-24

Падение Вавилона

1После этого я увидел ещё одного ангела, сходящего с небес и обладающего великой властью; вся земля была озарена его славой. 2Он произнёс могучим голосом:

– Пала, пала великая блудница Вавилон18:2 См. Ис. 21:9.

и стала жилищем демонов,

пристанищем для всякого нечистого духа

и всякой нечистой и мерзкой птицы.

Все народы пили

доводящее до безумия вино её разврата.

3Цари земли развратничали с ней,

и купцы земли нажились на её необузданной тяге к роскоши.

4Затем я услышал с небес ещё один голос. Он сказал:

– Выйди из неё, народ мой,

чтобы тебе не участвовать в её грехах

и не подвергнуться её наказанию,

5потому что её грехи поднялись уже до небес18:5 См. Иер. 51:9.,

и Всевышний помнит её преступления.

6Сделайте ей то же, что она сделала другим,

и отплатите ей вдвойне за её дела.

В той самой чаше, в которой она замешивала своё вино,

замешайте ей напиток двойной крепости.

7Доставьте ей столько горя и страданий,

сколько она позволяла себе славы и роскоши,

потому что она хвалится в своём сердце:

«Я не какая-нибудь вдова! Я сижу как царица!

Я никогда не буду скорбеть!»

8И поэтому настанет день, когда её постигнут горести:

смерть, плачь и голод.

Она будет сожжена огнём,

потому что могуч Вечный Бог, осудивший её18:7-8 См. Ис. 47:7-9..

9Когда цари земли, которые развратничали с ней и наслаждались её роскошью, увидят дым от её пожарища, они будут рыдать по ней и бить себя в грудь18:9 Ср. Езек. 26:16-18.. 10Стоя вдали в ужасе от её мучений, они будут говорить:

– Горе! Горе! О великая столица!

О, Вавилон, могучая столица!

В один час свершился над тобой суд!

11Купцы земли плачут и скорбят по ней, потому что никто уже не покупает их товаров: 12грузов золота, серебра, драгоценных камней и жемчуга; тончайших льняных тканей, пурпура, шёлка и алых материй; ароматической древесины; изделий из слоновой кости, ценной древесины, бронзы, железа и мрамора; 13корицы, пряностей, благовоний, ароматического масла и ладана18:13 Ладан – ценная ароматическая смола растений, произрастающих в Аравии и Северной Африке. См. пояснительный словарь., вина, оливкового масла, отборной муки и пшеницы, крупного и мелкого скота, коней и колесниц, рабов и пленённых на войне18:12-13 См. Езек. 27:12-22.. 14Они будут говорить:

– Плодов, которых желала душа твоя, уже нет у тебя. Все твои богатства и слава покинули тебя и уже никогда не вернутся.

15Торговавшие этими товарами купцы, нажившиеся на ней, будут стоять в стороне, перепуганные её бедствиями. Они будут плакать и скорбеть, 16говоря:

– Горе! Горе! О великая столица,

одетая в тончайшую льняную одежду, в пурпурное и алое,

украшенная золотом, драгоценными камнями и жемчугом!

17В один час было уничтожено такое огромное богатство!

Все капитаны кораблей, все их пассажиры и моряки и все, чей промысел связан с мореплаванием, будут издали наблюдать, 18и, когда увидят дым, поднимающийся от неё, зарыдают:

– Разве был ещё когда-либо город, подобный этой великой столице?18:17-18 Ср. Езек. 27:28-29, 32.

19Они посыпали свои головы пылью18:19 Ср. Езек. 27:30. и со слезами и скорбью причитали:

– Горе! Горе! О великая столица,

обогатившая всех судовладельцев своим богатством!

В один час ты была уничтожена!

20– Радуйтесь об этом, небеса!

Радуйтесь, святой народ Всевышнего, посланники Масиха и пророки,

потому что Всевышний осудил её за то, как она поступала с вами.

21Затем могучий ангел взял большой камень размером с мельничный жёрнов и бросил его в море, говоря:

– Так будет брошен и Вавилон, великая столица,

и никто уже её не найдёт.

22Никогда уже в тебе не будет слышно

голоса певцов, музыки арфистов, свирельщиков и трубачей,

никогда уже в тебе не отыщутся

ремесленники, каким бы ремеслом они ни занимались,

никогда уже не будет слышно в тебе

шума мельничных жерновов.

23Никогда уже не будет гореть в тебе свет светильника,

не будет слышно голосов жениха и невесты.

Твои купцы были господами на земле,

и все народы были обмануты твоим колдовством.

24Но в этой столице пролилась кровь пророков, святого народа Всевышнего

и всех убитых на земле.