Chivumbulutso 16 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 16:1-21

Mbale Zisanu ndi Ziwiri za Mkwiyo wa Mulungu

1Kenaka ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Nyumba ya Mulungu ija kuwuza angelo asanu ndi awiri kuti, “Pitani, katsanulireni pa dziko lapansi ukali wa Mulungu umene uli mʼmbale zisanu ndi ziwirizi!”

2Mngelo woyamba anapita natsanula mbale yake pa dziko lapansi ndipo zilonda zoyipa ndi zowawa zinabuka pa anthu amene anali ndi chizindikiro cha chirombo chija, napembedza fano lake.

3Mngelo wachiwiri anapita natsanula mbale yake pa nyanja ndipo madzi ake anasanduka magazi, magazi ake ngati a munthu wakufa. Chamoyo chilichonse cha mʼnyanjamo chinafa.

4Mngelo wachitatu anapita natsanula mbale yake pa mitsinje ndi akasupe amadzi ndipo zinasanduka magazi. 5Kenaka ndinamva mngelo wolamulira madzi uja akuti,

“Inu mwachita chilungamo, Inu Woyerayo,

amene mulipo ndipo munalipo;

6pakuti iwo anakhetsa magazi a oyera anu ndi aneneri anu,

nʼchifukwa chake mwawapatsa magazi kuti amwe, zomwe zikuwayenera.”

7Kenaka ndinamva mawu ochokera ku guwa lansembe akuti,

“Inde, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,

chiweruzo chanu ndi choona ndi cholungama.”

8Mngelo wachinayi anapita natsanula mbale yake pa dzuwa ndipo dzuwa linapatsidwa mphamvu yopsereza anthu ndi moto. 9Anapserera nako kutentha kwakukuluko ndipo anatukwana Mulungu, amene anali ndi ulamuliro pa miliri imeneyi, koma anakana kulapa ndi kumulemekeza.

10Mngelo wachisanu anapita natsanula mbale yake pa mpando waufumu wa chirombo chija ndipo mdima unagwa ponse pamene panali ufumu wake. Anthu analuma malilime awo chifukwa cha ululu. 11Ndipo anatukwana Mulungu wakumwamba chifukwa cha maululu awo ndi zilonda zawo koma anakana kulapa pa zimene anachita.

12Mngelo wachisanu ndi chimodzi anapita natsanula mbale yake pa mtsinje waukulu wa Yufurate, ndipo madzi ake anaphwa kuti pakhale njira yodzera mafumu ochokera kummawa. 13Kenaka ndinaona mizimu yoyipa itatu imene inkaoneka ngati achule; inatuluka mʼkamwa mwa chinjoka chija, mʼkamwa mwa chirombo chija ndi mʼkamwa mwa mneneri wonyenga uja. 14Imeneyi ndiyo mizimu ya ziwanda imene imachita zizindikiro zodabwitsa ndipo imatuluka kupita kwa mafumu a dziko lonse, kukawasonkhanitsa ku nkhondo ya pa tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuzonse.

15“Taonani, ndikubwera ngati mbala! Wodala munthu amene ali maso, nasunga zovala zake, kuti asayende maliseche kuti angaonetse maliseche ake.”

16Kenaka mizimu ija inasonkhanitsa pamodzi mafumu ku malo amene mʼChihebri amatchedwa Armagedo.

17Mngelo wachisanu ndi chiwiri anatsanulira mbale yake mu mlengalenga ndipo ku Nyumba ya Mulungu kunamveka mawu ofuwula kuchokera ku mpando waufumu kuti, “Kwatha!” 18Kenaka kunachitika mphenzi, phokoso, mabingu ndi chivomerezi choopsa. Chivomerezi ngati ichi sichinachitikepo chikhalire cha munthu pa dziko lapansi. Chinali chivomerezi choopsa kwambiri. 19Mzinda waukuluwo unagawika magawo atatu ndipo mizinda ya mitundu ya anthu inagwa. Mulungu anakumbukira Babuloni Wamkulu namupatsa chikho chake chodzaza ndi vinyo wa ukali wa mkwiyo wake. 20Chilumba chilichonse chinathawa ndipo mapiri sanaonekenso. 21Matalala akuluakulu olemera pafupifupi makilogalamu makumi asanu anagwa kuchokera kumwamba kugwera pa anthu. Ndipo anthu anatukwana Mulungu chifukwa cha mliri wa matalala popeza unali mliri woopsa kwambiri.

New International Reader’s Version

Revelation 16:1-21

The Seven Bowls of God’s Great Anger

1Then I heard a loud voice from the temple speaking to the seven angels. “Go,” it said. “Pour out the seven bowls of God’s great anger on the earth.”

2The first angel went and poured out his bowl on the land. Ugly and painful sores broke out on people. Those people had the mark of the beast and worshiped its statue.

3The second angel poured out his bowl on the sea. It turned into blood like the blood of a dead person. Every living thing in the sea died.

4The third angel poured out his bowl on the rivers and springs of water. They became blood. 5Then I heard the angel who was in charge of the waters. He said,

“Holy One, the way you judge is fair.

You are the God who is and who was.

6Those who worship the beast have poured out blood.

They have poured out the life’s blood of your holy people and your prophets.

So you have given blood to drink to those who worship the beast.

That’s exactly what they should get.”

7Then I heard the altar reply. It said,

“Lord God who rules over all,

the way you judge is true and fair.”

8The fourth angel poured out his bowl on the sun. The sun was allowed to burn people with fire. 9They were burned by the blazing heat. So they spoke evil things against the name of God, who controlled these plagues. But they refused to turn away from their sins. They did not give glory to God.

10The fifth angel poured out his bowl on the throne of the beast. The kingdom of the beast became very dark. People chewed on their tongues because they were suffering so much. 11They spoke evil things against the God of heaven. They did this because of their pains and their sores. But they refused to turn away from the sins they had committed.

12The sixth angel poured out his bowl on the great river Euphrates. Its water dried up to prepare the way for the kings from the East. 13Then I saw three evil spirits that looked like frogs. They came out of the mouths of the dragon, the beast and the false prophet. 14They are spirits of demons that perform signs. They go out to gather the kings of the whole world for battle. This battle will take place on the great day of the God who rules over all.

15“Look! I am coming like a thief! Blessed is anyone who stays awake and keeps their clothes on. Then they will be ready. They will not be caught naked and so be put to shame.”

16Then the evil spirits gathered the kings together. In the Hebrew language, the place where the kings met is called Armageddon.

17The seventh angel poured out his bowl into the air. Out of the temple came a loud voice from the throne. It said, “It is done!” 18Then there came flashes of lightning, rumblings, thunder and a powerful earthquake. There has never been an earthquake as terrible as this. One like this hasn’t happened while human beings have lived on earth. 19The great city split into three parts. The cities of the nations crumbled and fell. God remembered Babylon the Great. He gave Babylon the cup filled with the wine of his terrible anger. 20Every island ran away. The mountains could not be found. 21Huge hailstones weighing about 100 pounds each fell from the sky. The hail crushed people. And they spoke evil things against God because of the plague. That’s because the plague of hail was so terrible.