Chivumbulutso 14 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 14:1-20

Mwana Wankhosa ndi Anthu 144,000

1Kenaka ndinaona patsogolo panga panali Mwana Wankhosa, atayimirira pa Phiri la Ziyoni, ndipo Iye anali pamodzi ndi anthu 144,000 amene pa mphumi pawo panalembedwa dzina la Mwana Wankhosayo ndi la Atate ake. 2Ndipo ndinamva liwu lochokera kumwamba ngati mkokomo wa madzi ambiri, ndiponso ngati kugunda kwamphamvu kwa bingu. Liwu limene ndinamvalo linali ngati a anthu akuyimba azeze awo. 3Anthuwo ankayimba nyimbo yatsopano patsogolo pa mpando waufumu ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kuphunzira nyimboyo kupatula anthu 144,000 aja amene anawomboledwa pa dziko lapansi. 4Awa ndiwo amene sanadzidetse koma anadzisunga ndipo sanadziyipitse ndi akazi. Anthu amenewa ndiwo ankatsatira Mwana Wankhosa kulikonse kumene ankapita. Ndiwo amene anagulidwa pakati pa anthu a dziko lapansi kuti akhale oyambirira kuperekedwa kwa Mulungu ndi kwa Mwana Wankhosa. 5Iwo sananenepo bodza ndipo alibe cholakwa.

Angelo Atatu

6Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. 7Mngeloyo anayankhula mokweza mawu kuti, “Wopani Mulungu ndi kumutamanda, chifukwa nthawi yoweruza anthu yafika. Mumupembedze Iye amene analenga thambo, dziko lapansi, nyanja ndi akasupe amadzi.”

8Mngelo wachiwiri anatsatana naye ndipo anati, “Wagwa! Wagwa Babuloni womveka uja, amene anachititsa anthu a mitundu yonse kumwa vinyo wa zilakolako zake zachigololo.”

9Mngelo wachitatu anatsatana nawo ndi mawu ofuwula anati, “Ngati wina apembedza chirombo chija ndi fano lake ndi kulembedwa chizindikiro pa mphumi kapena pa dzanja, 10nayenso adzamwa vinyo waukali wa Mulungu, umene wathiridwa popanda kuchepetsa mphamvu zake mʼchikho cha ukali wa Mulungu. Munthuyo adzazunzidwa ndi moto wamiyala yasulufure pamaso pa angelo oyera ndi pa Mwana Wankhosa. 11Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” 12Pamenepa ndi pofunika kupirira kwa anthu oyera mtima amene amasunga malamulo a Mulungu ndi kukhalabe okhulupirika kwa Yesu.

13Kenaka ndinamva mawu kuchokera kumwamba akuti, “Lemba kuti, Odala anthu amene akufa ali mwa Ambuye kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo.”

“Inde,” akutero Mzimu, “akapumule ntchito zawo zotopetsa pakuti ntchito zawo zidzawatsata.”

Zokolola za Dziko la Pansi

14Ndinayangʼana patsogolo panga ndinaona mtambo woyera patakhalapo wina ngati Mwana wa Munthu, kumutu atavala chipewa chaufumu chagolide ndipo mʼdzanja mwake munali chikwakwa chakunthwa. 15Tsono mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu nafuwula mwamphamvu kwa uja wokhala pa mtamboyu. Mngeloyo anati, “Tenga chikwakwa chako ndipo kolola, pakuti nthawi yokolola ya dziko la pansi yakwana” 16Choncho wokhala pa mtambo uja anayamba kukolola dzinthu pa dziko lapansi ndi chikwakwa chakecho.

17Mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu kumwamba ndipo nayenso anali ndi chikwakwa chakunthwa. 18Kenaka mngelo winanso amene amalamulira moto, anatuluka kuchokera ku guwa lansembe nayitana mwamphamvu mngelo uja amene anali ndi chikwakwa chakunthwa chija, nati, “Tenga chikwakwa chako chakunthwacho yamba kudula mphesa za mʼmunda wamphesa wa pa dziko lapansi, pakuti mphesa zapsa kale.” 19Pamenepo mngeloyo anayambadi kugwiritsa ntchito chikwakwa chake nadula mphesa za dziko lapansi, naziponya mʼchopondera mphesa chachikulu cha ukali woopsa wa Mulungu. 20Mphesazo zinapondedwa mʼchopondera mphesa kunja kwa mzinda. Mʼchopondera mphesamo munatuluka magazi amene anayenderera ngati mtsinje, kuzama kwake mita ndi theka ndipo kutalika kwake makilomita 300.

Священное Писание

Откровение 14:1-20

Новая песнь на горе Сион

1Я посмотрел и увидел Ягнёнка. Он стоял на горе Сион, и с Ним было сто сорок четыре тысячи человек, у которых на лбу было написано имя Ягнёнка и имя Его Отца. 2Я слышал шум с небес, он напоминал одновременно шум могучих вод, раскаты сильного грома и звук, который производят арфисты, играющие на своих арфах. 3Они поют новую песнь перед троном, перед четырьмя живыми существами и перед старцами. Эту песнь не мог никто выучить, кроме ста сорока четырёх тысяч искупленных с земли. 4Это были те, кто не осквернил себя с женщинами, оставшись девственниками14:4 Вероятно, это символическое описание духовной чистоты этих людей – они не осквернились развратной жизнью и поклонением зверю.. Они всюду шли за Ягнёнком, куда бы Он ни шёл. Они были искуплены из всего человечества и освящены как первые плоды14:4 Первые плоды – Всевышний через пророка Мусу повелел исраильтянам приносить Ему в жертву первые снопы (см. Лев. 23:9-14) и лепёшку, испечённую из муки от первого урожая (см. Чис. 15:17-21). Всё первое было своего рода залогом последующего, и поэтому жертва от первого урожая освящала всё остальное. Подобным образом и сто сорок четыре тысячи: 1) отделены от всего остального мира и полностью посвящены Всевышнему (см. 1 Пет. 1:15-16; 2:9); 2) будучи новым творением (см. 2 Кор. 5:17), являются залогом предстоящего обновления всего мира (ср. Рим. 8:19-21). для Всевышнего и Ягнёнка. 5В их словах не нашлось никакой лжи, они непорочны14:5 См. Соф. 3:13..

Три ангела

6Потом я увидел ещё одного ангела, летящего посреди неба. У него была Радостная Весть, которая вечна, чтобы провозгласить её живущим на земле – всем племенам, родам, языкам и народам.

7– Бойтесь Всевышнего, – громко говорил ангел, – и воздайте Ему славу, потому что наступил час суда Его. Поклонитесь Создавшему небо и землю, море и источники вод14:7 См. Исх. 20:11; Заб. 145:6..

8За ним следовал второй ангел. Он говорил:

– Пал, пал великий Вавилон!14:8 См. Ис. 21:9. Он напоил все народы доводящим до безумия вином своего разврата14:8 См. Ис. 13:19-22; Иер. 50:39; 51:6-8..

9Вслед за ними последовал третий ангел. Он громко говорил:

– Кто поклоняется зверю и его изображению и кто принимает клеймо на свой лоб или на руку, 10тот будет пить вино ярости Всевышнего, вино неразбавленное, приготовленное в чаше Его гнева, и будет мучиться в горящей сере на глазах у святых ангелов и Ягнёнка. 11Для поклоняющихся зверю и его изображению и для принявших клеймо с его именем не будет покоя ни днём ни ночью, и дым их мучений будет подниматься вечно14:11 См. Ис. 34:10.. 12Это призыв к святому народу Всевышнего, тем, кто соблюдает повеления Всевышнего и верен Исе, проявлять терпение.

13И я услышал с небес голос:

– Запиши: отныне благословенны те, кто умирает с верой в Повелителя.

– Да, – говорит Дух, – теперь они отдохнут от своих трудов, и их дела будут вознаграждены.

Жатва на земле

14Я посмотрел и увидел белое облако. На облаке сидел Некто, похожий на человека14:14 Некто, похожий на человека – букв.: «похожий на сына человека». См. сноску на 1:13.. На Его голове был золотой венец, и в руке Он держал острый серп. 15Затем из храма вышел ещё один ангел и громко сказал Сидящему на облаке:

– Пошли Свой серп и пожни, потому что время жатвы уже настало, и урожай на земле уже созрел.

16Тогда Сидящий на облаке взмахнул Своим серпом над землёй, и на земле был собран урожай.

17Потом из небесного храма вышел ещё один ангел, у него тоже в руке был острый серп. 18И ещё один ангел вышел от жертвенника, где он заведовал огнём. Он громко крикнул ангелу, у которого был острый серп:

– Пошли твой острый серп и собери грозди винограда с виноградника земли, потому что ягоды его уже созрели.

19Ангел взмахнул своим серпом над землёй, собрал виноград и кинул его в великую давильню14:19 Давильня – в те времена виноград давили в особых углублениях, высеченных в скале, откуда сок вытекал через специальное отверстие. ярости Всевышнего. 20Виноград был потоптан в давильне, которая за городом, и из неё рекой потекла кровь. Эта река крови была длиной в триста километров14:20 Букв.: «тысячу шестьсот стадий». и по глубине достигала коням до уздечек14:17-20 См. Ис. 63:1-6; Иоиль 3:13..