Aroma 6 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 6:1-23

Kufa ku Tchimo, Kukhala ndi Moyo mwa Khristu

1Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe? 2Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo? 3Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake? 4Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.

5Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake. 6Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo 7chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.

8Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye. 9Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye. 10Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.

11Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu. 12Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa. 13Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo. 14Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.

Ife Ndife Akapolo a Mulungu

15Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! 16Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake. 17Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira. 18Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.

19Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima. 20Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo. 21Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa! 22Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. 23Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

New International Reader’s Version

Romans 6:1-23

Living a New Life in Christ

1What should we say then? Should we keep on sinning so that God’s grace can increase? 2Not at all! As far as sin is concerned, we are dead. So how can we keep on sinning? 3All of us were baptized into Christ Jesus. Don’t you know that we were baptized into his death? 4By being baptized, we were buried with Christ into his death. Christ has been raised from the dead by the Father’s glory. And like Christ we also can live a new life.

5By being baptized, we have been joined with him in a death like his. So we will certainly also be joined with him in a resurrection like his. 6We know that what we used to be was nailed to the cross with him. That happened so our bodies that were ruled by sin would lose their power. So we are no longer slaves of sin. 7That’s because those who have died have been set free from sin.

8We died with Christ. So we believe that we will also live with him. 9We know that Christ was raised from the dead and will never die again. Death doesn’t control him anymore. 10When he died, he died once and for all time. He did this to break the power of sin. Now that he lives, he lives in the power of God.

11In the same way, consider yourselves to be dead as far as sin is concerned. Now you believe in Christ Jesus. So consider yourselves to be alive as far as God is concerned. 12So don’t let sin rule your body, which is going to die. Don’t obey its evil desires. 13Don’t give any part of yourself to serve sin. Don’t let any part of yourself be used to do evil. Instead, give yourselves to God. You have been brought from death to life. So give every part of yourself to God to do what is right. 14Sin will no longer control you like a master. That’s because the law does not rule you. God’s grace has set you free.

Slaves to Right Living

15What should we say then? Should we sin because we are not ruled by the law but by God’s grace? Not at all! 16Don’t you know that when you give yourselves to obey someone you become that person’s slave? If you are slaves of sin, then you will die. But if you are slaves who obey God, then you will live a godly life. 17You used to be slaves of sin. But thank God that with your whole heart you obeyed the teachings you were given! 18You have been set free from sin. You have become slaves to right living.

19Because you are human, you find this hard to understand. So I am using an everyday example to help you understand. You used to give yourselves to be slaves to unclean living. You were becoming more and more evil. Now give yourselves to be slaves to right living. Then you will become holy. 20Once you were slaves of sin. At that time right living did not control you. 21What benefit did you gain from doing the things you are now ashamed of? Those things lead to death! 22You have been set free from sin. God has made you his slaves. The benefit you gain leads to holy living. And the end result is eternal life. 23When you sin, the pay you get is death. But God gives you the gift of eternal life. That’s because of what Christ Jesus our Lord has done.