1Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu 2umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake. 3Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide. 4Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu, 5ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe. 6Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Paulo Afunitsitsa Kukacheza ku Roma
8Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu. 9Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse. 10Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni 12ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake. 13Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe. 15Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene. 17Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
Mkwiyo wa Mulungu pa Mtundu wa Anthu
18Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa. 19Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo. 20Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula.
21Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima. 22Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa. 23Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo. 25Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni.
26Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo. 27Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo. 29Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche, 30osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo, 31alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza. 32Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.
Приветствие
1От Паула, раба Исы аль-Масиха1:1 Аль-Масих (переводится как «Помазанник») – праведный Царь и Освободитель, Спаситель, обещанный Аллахом ещё в Таурате, Забуре и Книге Пророков. Аль (также передаётся в русской транскрипции как эль, الـ) — определённый артикль в арабском языке., призванного быть Его посланником и избранного для возвещения Радостной Вести Аллаха, 2которая была заранее обещана Аллахом через Его пророков в Священном Писании. 3-4Эта Весть – о Его (вечном) Сыне1:3-4 То, что Иса назван Сыном Всевышнего, не означает, что у Аллаха есть сын, который был зачат обычным путём. В древности у иудеев титул «сын Всевышнего» применялся к царям Исраила (см. 2 Цар. 7:14; Заб. 2:6-7), но также указывал на ожидаемого Масиха, Спасителя и праведного Царя от Аллаха, т. е. Ису (см. Ин. 1:49; 11:27; 20:31). В Инджиле через этот термин постепенно раскрывается идея вечных взаимоотношений Всевышнего и аль-Масиха, указывающая на сходство характеров и единство природы Этих Личностей, на понятном нам примере – близких взаимоотношениях отца и сына (см. 1 Ин. 2:23)., нашем Повелителе Исе аль-Масихе. Он по Своему человеческому происхождению был потомком царя Давуда, а Святым Духом1:3-4 Или: «…царя Давуда, а согласно Своей святой природе»., через воскресение из мёртвых, был объявлен полноправным Сыном Всевышнего (то есть Царём)1:3-4 Ср. Заб. 2:6-7; Деян. 13:32-33.. 5Через Него я1:5 Букв.: «мы». Большинство толкователей считают, что под «мы» Паул подразумевает только самого себя. Также в 3:8, 9. получил благодать и стал Его посланником, чтобы ради Его имени покорить вере людей из всех народов, 6в том числе и вас, призванных быть последователями Исы аль-Масиха.
7Я обращаюсь ко всем тем римлянам, которых Аллах полюбил и призвал быть Его святым народом.
Благодать и мир вам1:7 Мир вам – на еврейском языке это выражение звучит как «шалом алейхем» и является родственным арабскому приветствию «ассаламу алейкум». от Аллаха, нашего Небесного Отца, и от Повелителя Исы аль-Масиха!
Желание Паула посетить Рим
8Прежде всего я через Ису аль-Масиха благодарю моего Бога за всех вас, потому что о вашей вере известно всему миру. 9Пусть Аллах, Которому я от всего сердца служу, возвещая Радостную Весть о Его (вечном) Сыне, будет мне свидетелем в том, что я постоянно вспоминаю о вас 10и всегда прошу в своих молитвах, чтобы, если на то будет воля Аллаха1:10 Если на то будет воля Аллаха – это выражение широко распространено среди восточных народов, например: إن شاء الله («Иншалла», араб.), Qudai qalasa (каз.), Кудай кааласа (кырг.), Xudo xohlasa (узб.), Allah istәsә (азерб.), Hudaý halasa (турк.), Худо хоӽад (тадж.) и др., я смог бы, наконец, посетить вас. 11Я очень хочу увидеть вас и поделиться с вами духовным благословением, чтобы укрепить вас, 12то есть, чтобы мы могли взаимно ободрить друг друга своей верой, вашей и моей. 13Я хочу, чтобы вы знали, братья, что я уже много раз собирался прийти к вам, но до сих пор мне постоянно что-то препятствовало. Я хотел увидеть плод своего служения среди вас, как видел среди других народов. 14Я должник и перед цивилизованными людьми, и перед дикими, перед образованными и перед невеждами. 15Поэтому я так жажду возвещать Радостную Весть и вам, живущим в Риме.
Радостная Весть о праведности от Аллаха
16Я не стыжусь Радостной Вести, ведь она сила Аллаха для спасения1:16 Спасение – от пламени ада (см. Иуда 1:23), от гнева Аллаха и Его судов (см. 5:9), от суетной жизни (см. 1 Пет. 1:18), от греха (см. Мат. 1:21) и от Иблиса (см. 2 Тим. 2:26). каждого, кто верит, – прежде всего иудея, а потом и язычника. 17В Радостной Вести открывается, что мы можем оправдаться перед Аллахом верой, и только верой, как и написано: «Праведный верой жив будет»1:17 Авв. 2:4..
Гнев Аллаха
18Ведь с небес открывается гнев Аллаха на всякое нечестие и неправедность людей, которые истину попирают злом. 19Им известно то, что можно знать об Аллахе, потому что Аллах явил им это. 20От создания мира невидимые свойства Аллаха – Его вечная сила и Божественная природа – вполне могут быть поняты через рассматривание того, что Он сотворил. И значит, неверующим нет извинения, 21потому что хотя они и знали об Аллахе, тем не менее они не прославили Его как Бога и не были благодарны Ему, но предались пустым размышлениям, и их неразумные сердца погрузились во мрак. 22Притязая на мудрость, они стали глупыми 23и заменили славу нетленного Бога на образы, похожие на тленных людей, птиц, четвероногих животных и пресмыкающихся.
24Поэтому Аллах отдал их на произвол низменных желаний их сердец, и они сами оскверняли свои тела нечистотой. 25Эти люди заменили истину Аллаха на ложь и поклонялись и служили созданию, а не Создателю, Который достоин вечной славы, аминь.
26Итак, Аллах оставил их на произвол их постыдных страстей, и в результате их женщины заменили естественные половые сношения с мужчинами на противоестественные: друг с другом; 27так же и мужчины вместо естественных половых сношений с женщинами стали разжигаться страстью друг к другу; мужчины с мужчинами делают постыдные вещи и сами в себе получают заслуженное наказание за своё извращение.
28А поскольку они посчитали ненужным познавать Аллаха, то Аллах оставил их на произвол их испорченных умов, допустив делать то, чего делать не должно. 29Они полны всякой неправедности, зла, жадности, порочности; полны зависти, убийства, раздоров, обмана, коварства, сплетен. 30Они клеветники, они ненавидят Аллаха, они наглы, надменны, хвастливы, изобретательны на зло, непокорны родителям; 31нет в них ни рассудка, ни веры, ни любви, ни милости. 32Отношение Аллаха им известно – все, кто живёт такой жизнью, достойны смерти, но они не только сами продолжают грешить, но и одобряют других, поступающих так же.