Akolose 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 1:1-29

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.

2Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu.

Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani. 4Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse. 5Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino 6umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse. 7Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu. 8Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.

9Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa. 10Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu. 11Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe 12ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika. 13Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa. 14Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.

Kupambana Koposa kwa Khristu

15Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse. 16Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo. 17Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye. 18Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse. 19Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu. 20Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.

21Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa. 22Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho 23ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.

Utumiki wa Paulo ku Mpingo

24Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo. 25Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu, 26chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. 27Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.

28Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu. 29Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

Knijga O Kristu

Kološanima 1:1-29

1Ovo je pismo od Pavla, kojega je Bog odabrao da bude apostol Isusa Krista, i od našega brata Timoteja.

2Kološanima, svetoj i vjernoj braći i sestrama u Isusu Kristu.

Neka vam naš Bog Otac udijeli milost i mir.

Pavlova zahvala i molitva

3Uvijek se molimo za vas i zahvaljujemo za vas Bogu Ocu našega Gospodina Isusa Krista 4jer smo čuli za vašu snažnu vjeru u Isusa Krista i za vašu ljubav koju iskazujete prema svetima posvuda. 5Razlog vaše vjere je nada što vas čeka u nebesima. O toj ste nadi prvi put čuli kad ste čuli istinu Radosne vijesti. 6Ista ta Radosna vijest koja je došla k vama proširila se cijelim svijetom. Posvuda mijenja ljudske živote, baš kao što je promijenila i vas prvoga dana kad ste ju čuli i kad ste shvatili istinu o Božjoj milosti prema grešnicima.

7Vi ste za nju čuli od Epafre, našega voljenog suradnika. On nas zastupa vjerno služeći Kristu. 8On nam je i rekao za vašu ljubav prema drugima, koju vam daje Sveti Duh.

9Zato se mi od dana kad smo to čuli neprestano molimo za vas, tražeći da vas Bog ispuni mudrošću i duhovnom spoznajom kako biste mogli razabrati njegovu volju, 10živjeti dostojno Gospodina i ugoditi mu, roditi svakom vrstom dobrih djela te rasti u spoznaji Boga.

11Molimo se da vas Bog ojača svojom slavnom silom da možete biti postojani i strpljivi. Da radosno 12možete zahvaljivati Ocu koji nas je osposobio da budemo subaštinicima svetoga Božjeg naroda koji živi u svjetlu. 13Izbavio nas je od vlasti tame i prenio u Kraljevstvo svojega ljubljenog Sina. 14Njegovom krvlju Bog je otkupio našu slobodu i oprostio nam grijehe.

Kristovo prvenstvo

15Krist je vidljiva slika nevidljivoga Boga, prvorođenac iznad svih stvorenja. 16U Kristu je stvoreno sve na nebesima i na zemlji: vidljivo i nevidljivo, kraljevi i kraljevstva, vladari i vlasti. Sve je stvoreno po njemu i za njega. 17Postojao je prije svega drugoga i održava sve što postoji.

18On je glava Crkve, koja je njegovo Tijelo. On je prvi od svih ustao od mrtvih, da u svemu bude prvi. 19Jer se Bogu svidjelo u njemu prebivati svom puninom 20i kroz njega—njegovom krvlju prolivenom na križu—pomiriti sa sobom sve na zemlji i na nebesima. 21To se odnosi i na vas koji ste nekada bili daleko od njega i bili mu neprijatelji mišlju i djelima. 22Ali on vas je ponovno izmirio sa sobom kroz smrt Kristova ljudskog tijela na križu. Priveo vas je u svoju nazočnost svete, neporočne i besprijekorne. 23Ali morate čvrsto i postojano ustrajati u vjeri. Ne dajte se pokolebati u nadi Radosne vijesti koju ste čuli. Ona se propovijeda diljem svijeta, a mene, Pavla, Bog je postavio da joj služim.

Pavlovo služenje Crkvi

24Sada se radujem što dovršavam patnje za koje mi je Krist rekao da ću ih proći za dobro Crkve, njegova tijela. 25Bog mi je dao osobitu službu da vam naviještam njegovu poruku u svoj punini. 26Ta je tajna bila skrivena vjekovima i naraštajima, ali sada ju je Bog očitovao njegovim svetima. 27Jer Bogu se svidjelo da svojemu narodu objavi kako su bogatstvo i slava Kristova namijenjeni i vama poganima. Jer u ovome je tajna: Krist živi u vama i vaša je nada da ćete biti dionicima njegove slave.

28Svima naviještamo Krista. Opominjemo i poučavamo ljude, s mudrošću koju nam je Bog dao, da svakoga učinimo zrelim u Kristu. 29Da to postignem, trudim se i borim u njegovoj snazi, koja tako silno djeluje u meni.