Ahebri 8 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 8:1-13

Mkulu wa Ansembe wa Pangano Latsopano

1Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba. 2Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.

3Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka. 4Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo. 5Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.” 6Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.

7Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake. 8Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati,

“Masiku akubwera,” akutero Yehova,

“pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

9Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo,

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto

chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija

ndipo Ine sindinawasamalire,

akutero Ambuye.

10Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli:

Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye,

Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo,

ndi kulemba mʼmitima mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

11Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake,

kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye

chifukwa onse adzandidziwa,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.

12Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

13Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

Thai New Contemporary Bible

ฮีบรู 8:1-13

มหาปุโรหิตแห่งพันธสัญญาใหม่

1ประเด็นที่เรากำลังกล่าวถึงก็คือเรามีมหาปุโรหิตอย่างนี้ ผู้ซึ่งประทับเบื้องขวาพระที่นั่งขององค์ผู้ทรงบารมีในสวรรค์ 2และผู้ทรงปฏิบัติหน้าที่ในสถานนมัสการอันเป็นพลับพลาแท้ซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงตั้งขึ้น ไม่ใช่มนุษย์ตั้ง

3มหาปุโรหิตทุกคนได้รับการแต่งตั้งให้ถวายทั้งเครื่องบูชาและของถวาย ฉะนั้นมหาปุโรหิตองค์นี้ทรงจำเป็นต้องมีสิ่งที่จะถวายด้วย 4หากทรงอยู่ในโลกพระองค์จะไม่ได้เป็นปุโรหิต เพราะมีคนที่จะถวายของถวายต่างๆ ตามที่บทบัญญัติกำหนดอยู่แล้ว 5ปุโรหิตเหล่านั้นปรนนิบัติในสถานนมัสการอันเป็นแบบจำลองและเงาของสิ่งที่อยู่ในสวรรค์ ด้วยเหตุนี้เมื่อโมเสสจะสร้างพลับพลาจึงได้รับคำเตือนว่า “จงทำทุกอย่างตามแบบที่เราได้สำแดงแก่เจ้าบนภูเขานั้น”8:5 อพย.25:40 6แต่พันธกิจที่พระเยซูทรงได้รับมอบหมายนั้นยิ่งใหญ่เหนือพันธกิจของพวกเขา เช่นเดียวกับที่พันธสัญญาซึ่งพระองค์ทรงเป็นสื่อกลางก็เหนือกว่าพันธสัญญาเดิม และตั้งอยู่บนพระสัญญาต่างๆ ที่ดียิ่งกว่า

7เพราะหากพันธสัญญาแรกไม่มีข้อบกพร่องก็ไม่จำเป็นต้องเสาะหาอีกพันธสัญญาหนึ่ง 8แต่พระเจ้าทรงเห็นข้อผิดพลาดของเหล่าประชากรและตรัสว่า8:8 สำเนาต้นฉบับบางสำเนาอาจแปลได้ว่าทรงเห็นข้อผิดพลาด และตรัสกับเหล่าประชากรว่า

“องค์พระผู้เป็นเจ้าประกาศว่า เวลานั้นจะมาถึง

เมื่อเราจะทำพันธสัญญาใหม่

กับพงศ์พันธุ์อิสราเอล

และกับพงศ์พันธุ์ยูดาห์

9เป็นพันธสัญญาซึ่งไม่เหมือนพันธสัญญา

ที่เราได้ทำไว้กับบรรพบุรุษของเขา

เมื่อเราจูงมือพวกเขา

นำออกมาจากดินแดนอียิปต์

เพราะพวกเขาไม่ได้คงความสัตย์ซื่อต่อพันธสัญญาของเรา

และเราเมินหนีจากพวกเขา

องค์พระผู้เป็นเจ้าประกาศดังนั้น

10นี่คือพันธสัญญาที่เราจะทำกับพงศ์พันธุ์อิสราเอลหลังจากสมัยนั้น

องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสดังนี้

เราจะใส่บทบัญญัติของเราในจิตใจของพวกเขา

จารึกบนหัวใจของพวกเขา

เราจะเป็นพระเจ้าของพวกเขา

และพวกเขาจะเป็นประชากรของเรา

11ผู้คนจะไม่สอนเพื่อนบ้าน

หรือสอนพี่น้องของตนอีกต่อไปว่า ‘จงรู้จักองค์พระผู้เป็นเจ้า’

เพราะพวกเขาทุกคนจะรู้จักเรา

ตั้งแต่ผู้น้อยที่สุดไปจนถึงผู้ใหญ่ที่สุด

12เพราะเราจะอภัยความชั่วช้าของเขา

และจะไม่จดจำบาปทั้งหลายของเขาอีกต่อไป”8:8-12 ยรม.31:31-34

13โดยการตรัสเรียกพันธสัญญานี้ว่า “พันธสัญญาใหม่” พระองค์ทรงทำให้พันธสัญญาแรกพ้นสมัยไป สิ่งที่พ้นสมัยหรือเก่าย่อมจะสูญสิ้นไปในไม่ช้า