Afilipi 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 2:1-30

Kutsanzira Kudzichepetsa kwa Khristu

1Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, 2tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso. 3Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo. 4Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.

5Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:

6Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu,

sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.

7Koma anadzichepetsa kotheratu

nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo

ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.

8Ndipo pokhala munthu choncho

anadzichepetsa yekha

ndipo anamvera mpaka imfa yake,

imfa yake ya pamtanda!

9Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri,

ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse

10kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire,

kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,

11ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye

kuchitira ulemu Mulungu Atate.

Kuwala monga Nyenyezi

12Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera, 13pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.

14Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo, 15kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba 16powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe. 17Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse. 18Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.

Timoteyo ndi Epafrodito

19Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu. 20Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu. 21Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu. 22Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake. 23Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere. 24Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.

25Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.

New International Reader’s Version 2014

Philippians 2:1-30

Being Humble Like Christ

1So does belonging to Christ help you in any way? Does his love comfort you at all? Do you share anything in common because of the Holy Spirit? Has Christ ever been gentle and loving toward you? 2If any of these things has happened to you, then agree with one another. Have the same love. Be one in spirit and in the way you think and act. By doing this, you will make my joy complete. 3Don’t do anything only to get ahead. Don’t do it because you are proud. Instead, be humble. Value others more than yourselves. 4None of you should look out just for your own good. Each of you should also look out for the good of others.

5As you deal with one another, you should think and act as Jesus did.

6In his very nature he was God.

Jesus was equal with God. But Jesus didn’t take advantage of that fact.

7Instead, he made himself nothing.

He did this by taking on the nature of a servant.

He was made just like human beings.

8He appeared as a man.

He was humble and obeyed God completely.

He did this even though it led to his death.

Even worse, he died on a cross!

9So God lifted him up to the highest place.

God gave him the name that is above every name.

10When the name of Jesus is spoken, everyone will kneel down to worship him.

Everyone in heaven and on earth and under the earth will kneel down to worship him.

11Everyone’s mouth will say that Jesus Christ is Lord.

And God the Father will receive the glory.

Live Without Complaining

12My dear friends, you have always obeyed God. You obeyed while I was with you. And you have obeyed even more while I am not with you. So continue to work out your own salvation. Do it with fear and trembling. 13God is working in you. He wants your plans and your acts to fulfill his good purpose.

14Do everything without complaining or arguing. 15Then you will be pure and without blame. You will be children of God without fault among sinful and evil people. Then you will shine among them like stars in the sky. 16You will shine as you hold on tight to the word of life. Then I will be able to boast about you on the day Christ returns. I can be happy that I didn’t run or work for nothing. 17But my life might even be poured out like a drink offering on your sacrifices. I’m talking about the way you serve because you believe. Even so, I am glad. I am joyful with all of you. 18So you too should be glad and joyful with me.

Timothy and Epaphroditus

19I hope to send Timothy to you soon if the Lord Jesus allows it. Then I will be encouraged when I receive news about you. 20I have no one else like Timothy. He will truly care about how you are doing. 21All the others are looking out for their own interests. They are not looking out for the interests of Jesus Christ. 22But you know that Timothy has proved himself. He has served with me like a son with his father in spreading the good news. 23So I hope to send him as soon as I see how things go with me. 24And I’m sure I myself will come soon if the Lord allows it.

25But I think it’s necessary to send Epaphroditus back to you. He is my brother in the Lord. He is a worker and a soldier of Christ together with me. He is also your messenger. You sent him to take care of my needs. 26He longs for all of you. He is troubled because you heard he was sick. 27He was very sick. In fact, he almost died. But God had mercy on him. He also had mercy on me. God spared me sadness after sadness. 28So I want even more to send him to you. Then when you see him again, you will be glad. And I won’t worry so much. 29So then, welcome him as a brother in the Lord with great joy. Honor people like him. 30He almost died for the work of Christ. He put his life in danger to make up for the help you yourselves couldn’t give me.