Aefeso 3 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 3:1-21

Paulo Mlaliki wa Anthu a Mitundu Ina

1Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.

2Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu, 3ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule. 4Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu, 5chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri. 6Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.

7Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu. 8Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu. 9Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. 10Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu. 11Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 12Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima. 13Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.

Paulo Apempherera Aefeso

14Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate, 15amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo. 16Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake, 17kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi 18kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu. 19Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.

20Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife, 21Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni.

Słowo Życia

Efezjan 3:1-21

Paweł—posłany do pogan

1Ja, Paweł, stałem się więźniem Chrystusa właśnie z powodu was, pogan. 2Jak bowiem wiecie, Bóg polecił mi, abym przekazał wam dobrą nowinę o Jego łasce. 3On objawił mi również tę tajemnicę, o której przed chwilą w skrócie wam napisałem. 4Czytając moje słowa, możecie się więc dowiedzieć, jak rozumiem ten tajemniczy plan Chrystusa. 5W minionych czasach nie był on ujawniony ludziom, ale obecnie Duch objawił go świętym apostołom i prorokom. 6Sednem tej tajemnicy jest to, że dzięki dobrej nowinie o Chrystusie poganie na równi z Żydami otrzymują wspaniałe dary od Boga, należą do jednego ciała—kościoła—i razem korzystają z Bożych obietnic! 7Dzięki łasce i potężnej mocy Boga poświęciłem się głoszeniu tej właśnie dobrej nowiny. 8Mnie, najmniej znaczącemu wśród wszystkich świętych, Bóg nakazał bowiem pójść do pogan i ogłosić im, że Chrystus obdarzył ich ogromnym bogactwem. 9Polecił mi również wyjaśnić ludziom ten tajemniczy plan Boga, Stwórcy wszechświata. Wcześniej plan ten był tajemnicą, 10teraz zaś—poprzez kościół—zadziwiająca mądrość Boga została ujawniona wobec wszystkich nadziemskich władz i mocy. 11Bóg zaplanował to przed wiekami i zrealizował przez Chrystusa Jezusa, naszego Pana. 12To dzięki Niemu możemy teraz śmiało zbliżać się do Boga, bo wierzymy Mu. 13Proszę więc, nie załamujcie się, słysząc, że znoszę dla was jakieś cierpienia. Bądźcie raczej z tego dumni!

Modlitwa za Efezjan

14Padam na kolana przed naszym Ojcem, 15od którego pochodzi każda istota, zarówno w niebie, jak i na ziemi. 16On jest otoczony chwałą i wszystko do Niego należy, dlatego proszę Go, aby was wewnętrznie wzmocnił przez swojego Ducha. 17Modlę się, aby Chrystus—przez wiarę—zamieszkał w waszych sercach i abyście uchwycili się Go. 18Wtedy bowiem zrozumiecie—wraz ze wszystkimi świętymi—jak szeroka, jak długa, jak wysoka i jak głęboka jest Jego miłość. 19I poznacie ją, choć pełne zrozumienie jej przekracza ludzkie możliwości. Modlę się również o to, aby inni ludzie mogli dostrzec w waszym życiu cechy samego Boga.

20Bóg, swoją potężną mocą działającą w naszym życiu, jest w stanie uczynić o wiele więcej niż to, o co Go prosimy, a nawet więcej niż jesteśmy sobie w stanie wyobrazić. 21Jemu niech będzie wieczna chwała w kościele i w Chrystusie Jezusie—przez wszystkie pokolenia. Amen!