Aefeso 3 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 3:1-21

Paulo Mlaliki wa Anthu a Mitundu Ina

1Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.

2Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu, 3ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule. 4Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu, 5chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri. 6Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.

7Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu. 8Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu. 9Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. 10Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu. 11Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 12Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima. 13Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.

Paulo Apempherera Aefeso

14Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate, 15amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo. 16Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake, 17kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi 18kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu. 19Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.

20Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife, 21Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni.

New Serbian Translation

Ефесцима 3:1-21

1Ради тога сам ја, Павле, сужањ Исуса Христа за вас многобошце. 2Ви сте, свакако, чули за службу која ми је по Божијој милости поверена за вас. 3Наиме, Бог ми је откривењем обзнанио тајну, као што сам вам укратко написао. 4Читајући то, можете да разумете моје поимање Христове тајне, 5која није била позната ранијим нараштајима, али је сада преко Духа откривена његовим светим апостолима и пророцима. 6Тајна се састоји у томе да су многобошци постали сунаследници, припадници истог тела, те да учествују у обећању које је Бог испунио у Христу Исусу путем Радосне вести. 7Овој Радосној вести ја сам постао слуга по дару Божије милости која ми је поверена дејством његове силе.

8А мени, најмањем од свих светих, указана је ова милост да проповедам многобошцима неистраживо богатство Христово, 9и да свима расветлим остварење ове тајне, коју је Бог, створитељ свега, држао сакривеном у минулим вековима, 10да би сада, посредством Цркве, обзнанио своју многострану мудрост главарствима и властима на небесима. 11Бог је то остварио на основу свог вечног наума, посредством нашег Господа, Исуса Христа. 12У њему имамо слободу да приступимо Богу с поуздањем, вером у њега. 13Зато вас молим да се не обесхрабрите овим мојим невољама које подносим за вас; све је то ради ваше славе.

Павлова молитва

14Зато пригибам своја колена пред Оцем, 15који доводи у постојање сваки род на небу и на земљи, 16да вас он, по својој богатој слави, ојача својим Духом у вашем унутрашњем човеку; 17да се Христос вером настани у вашим срцима, те да у љубави будете укорењени и утемељени; 18да разумете са свим светима, ширину, дужину, висину, и дубину Божије љубави, 19и да упознате ту љубав Христову која надмашује свако знање, да бисте сасвим били испуњени Богом.

20А ономе, што силом којом делује у нама може да учини далеко више од свега што молимо или мислимо, 21њему нека је слава у Цркви и у Христу Исусу у свим поколењима од сад и довека! Амин.