Aefeso 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 3:1-21

Paulo Mlaliki wa Anthu a Mitundu Ina

1Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.

2Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu, 3ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule. 4Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu, 5chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri. 6Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.

7Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu. 8Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu. 9Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. 10Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu. 11Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 12Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima. 13Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.

Paulo Apempherera Aefeso

14Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate, 15amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo. 16Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake, 17kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi 18kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu. 19Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.

20Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife, 21Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni.

New International Reader’s Version 2014

Ephesians 3:1-21

God’s Wonderful Plan for the Gentiles

1I, Paul, am a prisoner because of Christ Jesus. I am in prison because of my work among you who are Gentiles.

2I am sure you have heard that God appointed me to share his grace with you. 3I’m talking about the mystery God showed me. I have already written a little about it. 4By reading about this mystery, you will be able to understand what I know. You will know about the mystery of Christ. 5The mystery was not made known to people of other times. But now the Holy Spirit has made this mystery known to God’s holy apostles and prophets. 6Here is the mystery. Because of the good news, God’s promises are for Gentiles as well as for Jews. Both groups are parts of one body. They share in the promise. It belongs to them because they belong to Christ Jesus.

7I now serve the good news because God gave me his grace. His power is at work in me. 8I am by far the least important of all the Lord’s holy people. But he gave me the grace to preach to the Gentiles about the unlimited riches that Christ gives. 9God told me to make clear to everyone how the mystery came about. In times past it was kept hidden in the mind of God, who created all things. 10He wanted the rulers and authorities in the heavenly world to come to know his great wisdom. The church would make it known to them. 11That was God’s plan from the beginning. He has fulfilled his plan through Christ Jesus our Lord. 12Through him and through faith in him we can approach God. We can come to him freely. We can come without fear. 13So here is what I’m asking you to do. Don’t lose hope because I am suffering for you. It will lead to the time when God will give you his glory.

Paul Prays for the Ephesians

14I bow in prayer to the Father because of my work among you. 15From the Father every family in heaven and on earth gets its name. 16I pray that he will use his glorious riches to make you strong. May his Holy Spirit give you his power deep down inside you. 17Then Christ will live in your hearts because you believe in him. And I pray that your love will have deep roots. I pray that it will have a strong foundation. 18May you have power together with all the Lord’s holy people to understand Christ’s love. May you know how wide and long and high and deep it is. 19And may you know his love, even though it can’t be known completely. Then you will be filled with everything God has for you.

20God is able to do far more than we could ever ask for or imagine. He does everything by his power that is working in us. 21Give him glory in the church and in Christ Jesus. Give him glory through all time and for ever and ever. Amen.