Genesis 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 1:1-31

Chiyambi cha Chilengedwe

1Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi. 2Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.

3Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi. 4Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima. 5Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.

6Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.” 7Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi. 8Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.

9Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi. 10Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

11Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi. 12Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino. 13Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.

14Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka; 15zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.” 16Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi. 17Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi, 18kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 19Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.

20Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.” 21Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 22Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.” 23Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.

24Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi. 25Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

26Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”

27Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.

Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu;

analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.

28Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”

29Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu. 30Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.

31Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

Bibelen på hverdagsdansk

1. Mosebog 1:1-31

Hvordan Gud skaber universet

1I begyndelsen skabte Gud himlen og jorden. 2Jorden var øde og tom, og urdybet lå hen i totalt mørke, men Guds Ånd svævede over de mørke vande.

3Så sagde Gud: „Der skal blive lys!” og så var der lys. 4Gud glædede sig over lyset, og han satte skel mellem lyset og mørket. 5Tiden med lys kaldte han dag, og tiden med mørke kaldte han nat. Det blev aften, og det blev morgen. Det var den første dag.

6Så sagde Gud: „Der skal være en hvælving midt i alt vandet til at dele det.” 7Og Gud dannede en hvælving, så vandet ovenfor den blev adskilt fra vandet nedenfor den. 8Hvælvingen kaldte han himmel. Det blev aften, og det blev morgen. Det var den anden dag.

9Dernæst sagde Gud: „Vandet under himmelhvælvingen skal samle sig, så det tørre land kommer til syne.” Og sådan skete det. 10Det tørre land kaldte han jord, og de steder, hvor vandet var, kaldte han hav; og Gud glædede sig over sit værk.

11Derpå sagde Gud: „Grønne planter, der bærer frø, skal spire frem af jorden, og frugttræer, som bærer frugt med kerner, skal vokse op, så de kan formere sig, hver efter sin art.” Og sådan blev det. 12Op af jorden spirede grønne planter, som bar frø, og træer, som bar frugt med kerner, hver efter sin art. Og Gud glædede sig over sit værk. 13Det blev aften, og det blev morgen. Det var den tredje dag.

14-15Så sagde Gud: „Der skal være lysgivere på himmelhvælvingen, som sætter skel mellem dag og nat, og som markerer årstidernes skiften og festdagenes begyndelse.” Og sådan blev det. 16Gud frembragte to store lys på himlen til at skinne på jorden, det største lys, solen, til at herske om dagen, og det mindre, månen, til at herske om natten sammen med stjernerne. 17Han satte dem på himmelhvælvingen til at lyse på jorden, 18til at sætte skel mellem dagen og natten. Og han glædede sig over sit værk. 19Det blev aften, og det blev morgen. Det var den fjerde dag.

20Dernæst sagde Gud: „Vandet skal vrimle med fisk og andet liv, og der skal være et mylder af fugle i luften.” Og sådan blev det. 21Gud skabte de store havdyr og en mangfoldighed af fisk og fugle; og han glædede sig over sit værk. 22Han velsignede dem og sagde: „Formér jer og bliv mange. Fiskene skal fylde havene, og fuglene skal fylde luften.” 23Det blev aften, og det blev morgen. Det var den femte dag.

24Derpå sagde Gud: „Af jorden skal der fremstå alle slags dyr—kvæg, krybdyr og alle mulige vilde dyr.” Og sådan blev det. 25Gud dannede alle slags vilde dyr, krybdyr og husdyr, alle i stand til at formere sig, hver efter sin art; og Gud glædede sig over sit værk.

26Så sagde Gud: „Lad os frembringe et levende væsen, der ligner os. Det skal herske over alt dyrelivet—fiskene i havet, fuglene i luften og de tamme og vilde dyr på jorden.” 27Da skabte Gud to mennesker, som lignede ham. De blev skabt som mand og kvinde. 28Gud velsignede dem og sagde: „Formér jer og bliv mange, bred jer over hele jorden og tag den i besiddelse! Hersk over fiskene, fuglene og alle de andre dyr på jorden.” 29Gud fortsatte: „Se! Jeg giver jer alle de frøbærende planter på jorden som føde, og I må også spise frugt fra de mange frugttræer. 30Jeg giver græsset og alt grønt til føde for dyrene og fuglene.” Og sådan blev det. 31Gud betragtede nu hele sit skaberværk, og han var ovenud tilfreds med det. Det blev aften, og det blev morgen. Det var den sjette dag.