2 Timoteyo 4 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 4:1-22

1Pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa Khristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa omwe pamene adzaonekera ndi ufumu wake, ndikukulamula kuti: 2Lalikira Mawu; khala wokonzeka pa nthawi yake, ngakhale pamene si pa nthawi yake. Konza zolakwa zawo, dzudzula ndipo limbikitsa moleza mtima kwambiri ndi malangizo osamalitsa. 3Pakuti idzafika nthawi imene anthu adzakana chiphunzitso choona. Mʼmalo mwake, chifukwa chokhumba kumva zowakomera zokha, adzasonkhanitsa aphunzitsi ambiri omawawuza zimene iwo akufuna kumva. 4Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe. 5Koma iwe, khala tcheru nthawi zonse, pirira mʼzovuta, gwira ntchito ya mlaliki, gwira ntchito zonse za utumiki wako.

6Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga. 7Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro. 8Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.

Ndemanga ya Paulo

9Uyesetse kubwera kuno msanga. 10Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. 11Ndatsala ndi Luka yekha basi. Mutenge Marko ndipo ubwere naye kuno, chifukwa amandithandiza mu utumiki wanga. 12Ndatumiza Tukiko ku Efeso. 13Pobwera, unditengere chofunda pamwamba chimene ndinachisiya kwa Kupro ku Trowa. Unditengerenso mabuku anga, makamaka aja azikopawa.

14Alekisandro, mmisiri wa zitsulo anandichitira zoyipa kwambiri. Ambuye adzamubwezera pa zimene anachita. 15Iwenso ukhale naye tcheru chifukwa anatsutsa kwambiri uthenga wathu.

16Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire. 17Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango. 18Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya.

Mawu Otsiriza

19Pereka moni kwa Prisila ndi Akura pamodzi ndi banja lonse la Onesiforo. 20Erasto anatsalira ku Korinto. Trofimo ndinamusiya akudwala ku Mileto. 21Uyesetse kubwera kuno nthawi yozizira isanafike. Eubulo akupereka moni, ndiponso Pude, Lino, Klaudiya ndi abale onse nawonso akupereka moni.

22Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס השנייה אל-טימותיוס 4:1-22

1אני מצווה עליך לפני אלוהים ולפני אדוננו ישוע המשיח, אשר ישפוט את החיים ואת המתים בבואו ובמלכותו: 2הטף את דבר האלוהים בכל עת – בכל הזדמנות שבאה לידך, בין אם זה נוח או לא. הוכח, הזהר ותקן את אנשיך כשיש צורך בכך; עודד אותם לעשות את הטוב ולמד אותם בסבלנות את דבר ה׳. 3כי יבוא הזמן שהאנשים לא יקשיבו לאמת, ויחפשו מורים שילמדו אותם מה שהם רוצים לשמוע. 4הם לא יקשיבו לדבר אלוהים, ויפנו בשמחה לאגדות ולשקרים.

5אבל אתה שמור על קור רוחך, ואל תפחד לסבול למען האדון. הדרך אנשים אחרים לאמונה במשיח, ובצע את כל המוטל עליך על הצד הטוב ביותר.

6אני אומר לך דברים אלה משום שלא נותר לי זמן רב להיות איתך. שעתי קרבה – תוך זמן קצר אעבור מן העולם הזה ואהיה בשמים. 7נלחמתי את המלחמה הטובה למען האדון, רצתי במרוץ הגדול ותמיד נשארתי נאמן לו. הגיעה העת שאנוח. 8עתה שמור לי בשמים כתר צדקה אשר האדון, שופט־הצדק, ייתן לי ביום שובו, ולא רק לי, כי אם לכל אלה שמצפים לשובו בכיליון עיניים.

9אנא, בוא אלי במהירות האפשרית, 10כי דימס עזב אותי בגלל אהבתו לדברי העולם הזה, והלך לתסלוניקי. קריסקיס הלך לגלטיא, וטיטוס הלך לדלמטיה. 11רק לוקס נמצא איתי. הבא איתך את מרקוס, כי אני זקוק לעזרתו.

12(גם טוכיקוס איננו כאן, כי שלחתיו לאפסוס). 13אנא, הבא איתך את מעילי אשר השארתי אצל אחינו קרפוס בטרואס, ואת הספרים, והחשוב ביותר – את כתבי הקלף.

14אלכסנדרוס חרש הנחושת עולל לי רעות רבות. ישלם לו אלוהים כגמולו.

15היזהר ממנו, כי הוא מתנגד בחריפות לכל מה שאנחנו מאמינים.

16כשהביאו אותי למשפט בפעם הראשונה, איש לא היה כאן כדי לעזור לי; כולם ברחו להם. (אני מקווה שאלוהים לא ישפוט אותם על כך). 17אך האדון חיזק אותי ועזר לי, כדי שאוכל להטיף את הבשורה באומץ לכל העולם, ובכך הצילני מלוע הארי. 18אכן, האדון יצילני תמיד מכל רע ויביאני אל מלכותו בשמים. לאלוהים הכבוד לעולם ועד. – אמן.

19אנא, מסור דרישת־שלום בשמי לפריסקה, לעקילס ולאלה שגרים בביתו של אוניסיפורוס. 20ארסטוס נשאר בקורינתוס, ואת טרופימוס השארתי חולה במיליטוס.

21השתדל לבוא לכאן לפני בוא החורף. אובולוס, פודיס, לינוס, קלודיה וכל האחים דורשים בשלומך.

22אדוננו ישוע המשיח יברך אותך ויהיה עם רוחך. – אמן.