2 Samueli 8 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 8:1-18

Kupambana kwa Davide pa Nkhondo

1Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.

2Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.

3Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate. 4Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.

5Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000. 6Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.

7Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu. 8Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.

9Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri, 10anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.

11Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa: 12Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.

13Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.

14Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Akuluakulu a Davide

15Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse. 16Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika. 17Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi; 18Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

O Livro

2 Samuel 8:1-18

As vitórias de David

(1 Cr 18.1-14)

1Depois disto, David venceu e submeteu os filisteus, tirando das mãos deles Metegue-Amá, a sua maior cidade.

2Também conquistou Moabe. Dividiu as suas vítimas, fazendo-as deitarem-se lado a lado, em fileiras. Depois de medir com uma fita, dois terços de cada fila eram condenados a morrer; o terço restante era poupado, para serem servos de David; pagaram-lhe um tributo anualmente, daí em diante.

3Conquistou o domínio do rei Hadadezer, filho de Reobe, rei de Zobá, numa batalha junto ao rio Eufrates, porque Hadadezer tinha tentado retomar o poder. 4David capturou 1700 cavaleiros e 20 000 soldados. Inutilizou os cavalos dos seus carros de combate, à exceção de uma centena que guardou para seu próprio uso.

5Quando os arameus vieram de Damasco para socorrer Hadadezer, David matou 22 000 deles. 6David pôs várias guarnições militares em Damasco, e os arameus tornaram-se seus súbditos, pagando-lhe um tributo anual. O Senhor concedia-lhe sempre vitórias, para onde quer que se virasse. 7Trouxe também para Jerusalém os escudos de ouro que os oficiais do rei Hadadezer usavam, 8assim como uma grande quantidade de bronze de Beta e de Berotai, cidades do rei Hadadezer.

9Quando o rei Toú de Hamate ouviu narrar todas as vitórias de David sobre o exército de Hadadezer, 10enviou o seu filho Jorão para felicitá-lo, visto que Hadadezer e Toú eram inimigos. Jorão trouxe-lhe presentes de prata, ouro e bronze. 11-12David consagrou tudo isso ao Senhor, assim como os despojos de prata e ouro que trouxera dos combates contra Aram, Moabe, Amon, os filisteus, Amaleque e o rei Hadadezer, filho de Reobe, rei de Zobá.

13David tornou-se muito famoso. Depois disso, ainda destruiu 18 000 edomitas8.13 Alguns manuscritos, além da Septuaginta, têm edomitas (cf 1 Cr 18.12); mas a maior parte dos manuscritos hebreus têm arameus. no vale do Sal. 14Colocou também guarnições militares através da terra de Edom, de forma que toda essa nação foi obrigada a pagar tributo a Israel. O Senhor tornou-o vitorioso para onde quer que se dirigisse.

Os oficiais de David

(2 Sm 20.23-26; 1 Cr 18.14-17)

15David reinou com justiça sobre Israel, dirigindo as causas do seu povo com toda a equidade. 16Joabe, filho de Zeruía, era o general do seu exército. O seu secretário para os assuntos da governação era Jeosafá, filho de Ailude. 17Zadoque, filho de Aitube, e Aimeleque, filho de Abiatar, eram os sacerdotes; Seraías era o secretário particular do rei. 18Benaia, filho de Jeoiada, era o chefe da guarda pessoal do rei, formada por cretenses e peleteus. Os filhos do rei eram seus assistentes.