2 Samueli 11 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 11:1-27

Davide ndi Batiseba

1Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.

2Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri. 3Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?” 4Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake. 5Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”

6Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide. 7Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera. 8Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya. 9Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.

10Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”

11Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”

12Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo. 13Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.

14Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya. 15Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”

16Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu. 17Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.

18Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo. 19Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi, 20mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma? 21Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’ ”

22Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene. 23Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo. 24Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”

25Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”

26Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro. 27Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.

New Russian Translation

2 Царств 11:1-27

Давид и Вирсавия

1Весной, когда цари идут на войну, Давид послал Иоава со своими приближенными и всем израильским войском, и они нанесли поражение аммонитянам и осадили их главный город Равву. Давид же оставался в Иерусалиме.

2Однажды вечером, поднявшись с постели, Давид прогуливался по крыше своего дворца. С крыши он увидел купающуюся женщину. Женщина была очень красива, 3и Давид послал разузнать о ней. Посланный сказал:

– Это Вирсавия11:3 Евр.: «Бат-Шева»., дочь Элиама и жена хетта Урии.

4Тогда Давид послал людей, чтобы привести ее. Она пришла к нему, и он лег с ней. (Она только что очистилась от своей ежемесячной нечистоты.) Затем она вернулась домой11:4 Или: «Затем она очистилась от своей нечистоты и вернулась домой». Нечистота – см. Лев. 15:18-30.. 5Эта женщина забеременела и послала сказать Давиду:

– Я беременна.

6Тогда Давид отправил Иоаву приказ:

– Пришли ко мне хетта Урию.

Иоав послал его к Давиду. 7Когда Урия пришел к нему, Давид расспросил его об Иоаве, о воинах и о ходе войны. 8Затем Давид сказал Урии:

– Ступай домой и омой ноги.

Урия вышел из царского дворца, а вслед за ним понесли царский подарок. 9Но Урия лег спать у входа во дворец со всеми слугами своего господина и не пошел к себе домой. 10Когда Давиду сказали: «Урия не пошел домой», он спросил его:

– Разве ты не после дороги? Почему ты не пошел домой?

11Урия сказал Давиду:

– Ковчег, Израиль и Иуда находятся в шатрах, и мой господин Иоав и все люди моего господина находятся в открытом поле. Как же я могу пойти домой, чтобы есть, пить и спать со своей женой? Верно, как и то, что ты жив, я не сделаю подобного!

12Тогда Давид сказал ему:

– Оставайся здесь и сегодня, а завтра я отправлю тебя обратно.

Урия остался в Иерусалиме в тот день и на следующий день. 13По приглашению Давида он ел и пил с ним, и Давид напоил его допьяна. Но вечером Урия вышел, чтобы лечь спать на своей циновке со слугами своего господина; он не пошел домой.

14Поутру Давид написал Иоаву письмо и отправил его с Урией. 15В письме было сказано: «Поставьте Урию там, где будет самое яростное сражение, и отступите от него, чтобы он погиб».

16Когда Иоав осаждал город, он поставил Урию там, где, как он знал, были самые сильные защитники. 17Когда горожане вышли из города и сразились с Иоавом, некоторые воины из войска Давида пали; хетт Урия тоже был убит. 18Иоав послал Давиду подробные известия о битве. 19Он научил вестника:

– Когда ты закончишь рассказывать царю эти известия о битве, 20царь может разгневаться и спросить тебя: «Зачем вы так близко подходили к городу сражаться? Разве вы не знали, что они станут стрелять со стены стрелами? 21Кто убил Авимелеха, сына Еруббаала?11:21 Так в некоторых древних переводах (ср. Суд. 7:1); в еврейском тексте: «Иеруб-Бешета». Разве не женщина бросила в него со стены обломок жернова, и он умер в Тевеце?11:21 См. Суд. 9:50-54. Зачем вы так близко подходили к стене?» Если спросит у тебя это, скажи ему: «А еще твой слуга хетт Урия погиб».

22Вестник пустился в путь и, когда прибыл, передал Давиду все, с чем послал его Иоав. 23Вестник сказал Давиду:

– Те люди наступали на нас и вышли против нас в открытое поле, но мы отогнали их обратно к городским воротам. 24Лучники стреляли в твоих слуг со стены, и некоторые из царских слуг погибли. Твой слуга хетт Урия тоже погиб.

25Давид сказал вестнику:

– Скажи Иоаву так: «Пусть это тебя не огорчает; меч поражает то одного, то другого. Соберись с силами против города и разрушь его». Скажи так, чтобы ободрить Иоава.

26Когда жена Урии услышала, что ее муж погиб, она оплакивала его. 27После того как время траура миновало, Давид привел ее в свой дом, она стала его женой и родила ему сына. Но то, что сделал Давид, не было угодно Господу.