2 Petro 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Petro 1:1-21

1Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu.

Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.

2Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.

Kudziwa za Mayitanidwe ndi za Kusankhidwa Kwathu

3Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake. 4Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.

5Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru. 6Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu. 7Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi. 8Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu. 9Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.

10Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse. 11Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.

Kukhala Oyera Mtima

12Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano. 13Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani, 14chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu. 15Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.

16Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake. 17Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.” 18Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.

19Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu. 20Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha. 21Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.

Persian Contemporary Bible

دوم پطرس 1:1‏-21

داستان سلام و درود از پطرس

1‏-2از طرف من، شمعون پطرس، خدمتگزار و رسول عيسی مسيح،

به همهٔ شما كه با ما ايمانی يكسان داريد.

دعا می‌كنم كه رحمت و آرامش در اثر شناخت خدا و خداوندمان عيسی، به فراوانی به شما عطا شود.

ايمانی كه به آن اشاره كردم، ايمانی است كه از جانب خدا و نجات دهندهٔ ما عيسی مسيح عطا می‌گردد و نعمتی گرانبهاست؛ و خدا به خاطر مهربانی و نيكويی مطلق خود، اين ايمان را به هر يک از ما عنايت می‌فرمايد.

زندگی برگزيدگان خدا

3او همچنين با قدرت عظيمش، هر چه كه برای يک زندگی خداپسندانه نياز داريم، عطا می‌كند و حتی ما را در جلال و نيكويی خود سهيم می‌سازد؛ اما برای اين منظور، لازم است كه او را بهتر و عمیقتر بشناسيم. 4با همين قدرت عظيم بود كه تمام بركات غنی و عالی را كه وعده داده بود، به ما بخشيد. يكی از اين وعده‌ها اين بود كه ما را از شهوت و فساد محيط اطرافمان رهايی دهد و از طبيعت و صفات الهی خود بهره‌ای به ما عطا فرمايد.

5اما برای دسترسی به اين بركات، علاوه بر ايمان، به خصلت‌های ديگری نيز نياز داريد؛ بلی، بايد سخت بكوشيد كه نيک باشيد، خدا را بهتر بشناسيد و به ارادهٔ او پی ببريد. 6همچنين بايد حاضر باشيد تا خواسته‌های خود را كنار گذاشته، با صبر و دينداری خدا را با شادی خدمت نماييد. 7به اين ترتيب، راه را برای قدم بعدی هموار می‌كنيد، يعنی آماده می‌شويد تا انسانها را دوست بداريد. اين محبت رشد كرده، تبديل به محبتی عميق نسبت به انسانها خواهد گشت. 8اگر اجازه دهيد اين خصلت‌های خوب در شما رشد كنند و فزونی يابند، از لحاظ روحانی نيرومند شده، برای خداوندمان عيسی مسيح مفيد و پرثمر خواهيد شد. 9اما كسی كه اجازه نمی‌دهد اين خصوصيات در او ريشه بدوانند، در حقيقت كور يا لااقل كوته‌بين است و فراموش كرده است كه خدا او را از زندگی گناه‌آلود سابقش نجات داده تا بتواند برای خداوند زندگی كند.

10بنابراين، ای برادران عزيز، بكوشيد تا ثابت كنيد كه حقيقتاً جزو برگزيدگان و دعوت‌شدگان خدا هستيد؛ زيرا اگر چنين كنيد، هرگز لغزش نخواهيد خورد و از خدا دور نخواهيد شد؛ 11و خدا نيز دروازه‌های آسمان را به روی شما خواهد گشود تا وارد ملكوت جاودانی خداوند و نجات‌دهندهٔ‌مان عيسی مسيح گرديد.

يادآوری حقيقت

12اما من هيچگاه از يادآوری اين مطالب به شما، كوتاهی نخواهم كرد، گرچه آنها را می‌دانيد و در حقيقتی كه يافته‌ايد، ثابت و استوار می‌باشيد. 13تا زمانی كه در اين دنيای فانی به سر می‌برم، وظيفهٔ خود می‌دانم كه اين نكات را به شما تذكر دهم تا آنها را فراموش نكنيد. 14زيرا می‌دانم كه بزودی دار فانی را وداع خواهم گفت؛ خداوندمان عيسی مسيح نيز مرا از اين موضوع آگاه ساخته است. 15بنابراين، سعی می‌كنم اين نكات را چنان در فكر و ذهن شما نقش نمايم كه حتی پس از رحلت من نيز بتوانيد آنها را به یاد آوريد.

16زمانی كه ما دربارهٔ قوت و بازگشت خداوندمان عيسی مسيح با شما سخن گفتيم، داستانهای ساختگی برايتان تعريف نكرديم، زيرا من با چشمان خود، عظمت و جلال او را ديدم. 17‏-18وقتی بر آن كوه مقدس، جلال و شكوه خدای پدر از او می‌درخشيد، من آنجا بودم. من آن صدا را شنيدم كه از آسمان طنين افكند و گفت: «اين فرزند عزيز من است؛ از او بسيار خشنودم.»

19پس ملاحظه می‌كنيد كه ما آنچه را كه انبیا گفته‌اند، به چشم ديده و ثابت كرده‌ايم كه گفتار آنان حقيقت دارد. شما نيز اگر به نوشته‌های ايشان با دقت بيشتری توجه نماييد، كار بسيار خوبی می‌كنيد. زيرا كلام ايشان همچون نور بر همهٔ زوايای تاريک می‌تابد و نكات مبهم و دشوار را برای ما روشن می‌سازد. با مطالعه و دقت در كلام ايشان، نور در وجودتان طلوع خواهد كرد و مسيح، اين «ستارهٔ صبح» در قلبتان خواهد درخشيد. 20‏-21اين را بدانيد كه هيچيک از پيشگويی‌های كتاب آسمانی، از فكر خود انبیا تراوش نكرده، بلكه روح‌القدس در وجود اين مردان خدا قرار می‌گرفت و حقيقت را به ايشان عطا می‌كرد تا بازگو نمايند.