2 Mbiri 9 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 9:1-31

Mfumu Yayikazi ya ku Seba Ichezera Solomoni

1Mfumu yayikazi ya ku Seba itamva za kutchuka kwa Solomoni, inabwera mu Yerusalemu kudzamuyesa ndi mafunso okhwima. Inafika ndi gulu lalikulu la ngamira zonyamula zokometsera zakudya, golide wambiri, ndi miyala yokongola. Inafika kwa Solomoni ndipo inayankhula naye zonse zimene zinali mu mtima mwake. 2Solomoni anayankha mafunso ake onse ndipo panalibe kanthu kalikonse kovuta kwa iye komwe sanathe kufotokozera mfumu yayikaziyo. 3Mfumu yayikazi ya ku Seba itaona nzeru za Solomoni komanso nyumba yaufumu imene anamanga, 4chakudya cha pa tebulo pake, moyo wa antchito ake ndi zovala zawo; atumiki opereka zakumwa ndi zovala zawo ndiponso nsembe zopsereza zimene ankapereka ku Nyumba ya Yehova, inathedwa nzeru.

5Iyo inati kwa mfumu, “Mbiri imene ndinamva ndili ku dziko kwathu, ya zomwe munachita komanso nzeru zanu ndi yoona. 6Koma sindinakhulupirire zimene ankanena mpaka nditafika ndi kuona ndi maso anga. Kunena zoona sanandiwuze ngakhale theka lomwe la kuchuluka kwa nzeru zanu, pakuti zaposa zimene ndinamva. 7Ngodala anthu anu! Ngodala atumiki anu amene amayimirira pamaso panu nthawi zonse ndi kumamva nzeru zanu! 8Atamandike Yehova Mulungu wanu amene wakondwera nanu nakukhazikani pa mpando wake waufumu kuti mulamulire mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu. Chifukwa cha chikondi cha Mulungu wanu pa Israeli, ndi khumbo lake kuti akusungeni mpaka muyaya, Iye wayika inu kukhala mfumu yawo kuti mulamulire moyenera ndi mwachilungamo.”

9Kenaka iyo inapereka kwa mfumu makilogalamu 4,000 a golide, zonunkhira zambirimbiri ndi miyala yokongola. Nʼkale lomwe sikunaonekenso zonunkhiritsa ngati zomwe mfumu yayikazi ya ku Seba inapereka kwa mfumu Solomoni.

10(Anthu a Hiramu ndi anthu a Solomoni anabweretsa golide kuchokera ku Ofiri ndipo anabweretsanso mitengo ya mʼbawa ndi miyala yokongola. 11Mfumu inagwiritsa ntchito mitengo ya mʼbawa pokonzera makwerero a Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndiponso kupangira anthu oyimba apangwe ndi azeze. Zinthu zonga zimenezi sizinaonekeponso mu Yuda).

12Mfumu Solomoni inapereka kwa mfumu yayikazi ya ku Seba zonse zimene inazifuna ndi kuzipempha ndipo Solomoni anayipatsa mfumuyo zoposa zimene iyo inabweretsa kwa Solomoni. Ndipo mfumuyo inabwerera ku dziko lake pamodzi ndi atumiki ake.

Ulemerero wa Mfumu Solomoni

13Kulemera kwa golide amene Solomoni amalandira pa chaka kunali makilogalamu 23,000, 14osawerengera amene ankabwera ndi anthu ochita malonda ndi osinthanitsa zinthu. Komanso mafumu onse a ku Arabiya ndi abwanamkubwa a mʼdzikomo amabweretsa golide ndi siliva kwa Solomoni.

15Mfumu Solomoni inapanga zishango zazikulu 200 zagolide wosasantha. Mʼchishango chilichonse mumalowa golide wolemera makilogalamu asanu ndi awiri. 16Iye anapanganso zishango zingʼonozingʼono 300 zagolide wosasantha ndipo chishango chilichonse chimapangidwa ndi golide wolemera makilogalamu atatu. Mfumu inayika zishangozi mʼnyumba yaufumu yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni.

17Ndipo mfumu inapanganso mpando waukulu waufumu wa nyanga za njovu ndipo unakutidwa ndi golide woyengeka bwino. 18Mpando waufumuwo unali ndi makwerero asanu ndi limodzi ndi choyikapo mapazi cholumikizidwa ku mpandowo. Mʼmbali zonse za mpandowo munali zosanjikapo manja, ndi chifanizo cha mkango chitayima posanjikapo manjapo. 19Mikango khumi ndi iwiri inayimirira pa makwerero asanu ndi imodzi aja. Umodzi mbali ina ya khwerero ndi wina mbali inayo. Palibe mpando wonga uwu umene unapangidwapo mu ufumu wina uliwonse. 20Zikho zonse za mfumu Solomoni zinali zagolide, ndiponso zipangizo zonse za ku nyumba yaufumu ya Nkhalango ya Lebanoni zinali zagolide oyengeka bwino. Panalibe chinthu chopangidwa ndi siliva, chifukwa siliva samayesedwa kanthu mʼnthawi ya Solomoni. 21Mfumu inali ndi sitima zambiri zapamadzi zimene zimayendetsedwa ndi antchito a Hiramu. Zimabwera kamodzi pa zaka zitatu zilizonse zitanyamula golide, siliva ndi nyanga za njovu, ndiponso anyani ndi apusi.

22Mfumu Solomoni anapambana mafumu ena onse a dziko lapansi pa chuma ndi nzeru. 23Mafumu onse a dziko lapansi ankafunafuna kuonana ndi Solomoni kuti adzamve nzeru zimene Mulungu anayika mu mtima mwake. 24Chaka ndi chaka, aliyense amene amabwera, amabweretsa mphatso monga zipangizo zasiliva ndi golide, mikanjo, zida zankhondo ndi zokometsera zakudya komanso akavalo ndi abulu.

25Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo ndi magaleta, ndi akavalo 12,000 amene amawasunga mʼmizinda yosungira magaleta ndiponso ena anali ndi iye ku Yerusalemu. 26Iye ankalamulira mafumu onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika ku malire a dziko la Igupto. 27Mfumu inasandutsa siliva kukhala wambiri ngati miyala wamba mu Yerusalemu ndipo mikungudza kukhala yochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa. 28Solomoni ankayitanitsa akavalo ake kuchokera ku Igupto ndi mayiko ena onse.

Kumwalira kwa Solomoni

29Tsono ntchito zina zonse za Solomoni, kuyambira pachiyambi mpaka kumaliza, kodi sizinalembedwa mʼbuku la mbiri la mneneri Natani, ndi mʼbuku la uneneri wa Ahiya wa ku Silo ndi mʼbuku la masomphenya a mlosi Ido, lokamba za Yeroboamu mwana wa Nebati? 30Solomoni analamulira Aisraeli onse ku Yerusalemu zaka makumi anayi. 31Ndipo anamwalira nagona ndi makolo ake. Anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

Persian Contemporary Bible

دوم تواريخ 9:1-31

ديدار ملكه سبا با سليمان

(اول پادشاهان 10‏:1‏-13)

1ملكهٔ سبا وقتی آوازهٔ حكمت سليمان را شنيد، خواست به ديدار او برود و با طرح مسايل دشوار او را آزمايش كند. پس به همراهی سواران بسيار و كاروانی از شتران با بار طلا، جواهرات و عطريات به شهر اورشليم آمد و مسايل خود را با سليمان در ميان گذاشت. 2سليمان به تمام سؤالات او جواب داد. پاسخ هيچ مسئله‌ای برای سليمان مشكل نبود. 3‏-4وقتی ملكهٔ سبا سخنان حكيمانهٔ سليمان را شنيد و كاخ زيبا، خوراک شاهانه، تشريفات درباريان و مقامات، خدمت منظم خدمتكاران و ساقيان، و قربانیهایی كه در خانهٔ خداوند تقديم می‌شد، همه را به چشم خود ديد مات و مبهوت ماند! 5پس به سليمان گفت: «اينک باور می‌كنم كه هر چه در مملكتم دربارهٔ حكمت تو و كارهای بزرگت شنيده‌ام، همه راست بوده است. 6باور نمی‌كردم تا اينكه آمدم و با چشمان خود ديدم. حكمت تو بيش از آنست كه فكرش را می‌كردم! 7خوشا به حال اين قوم و خوشا به حال اين درباريان كه هميشه سخنان حكيمانهٔ تو را می‌شنوند! 8خداوند، خدای تو را ستايش می‌كنم كه تو را برگزيده تا بر قوم او سلطنت كنی. خدای تو قوم اسرائيل را دوست دارد و می‌خواهد ايشان را تا به ابد حفظ نمايد، به همين سبب است كه تو را به پادشاهی ايشان گمارده، تا به عدل و انصاف بر آنان سلطنت كنی!»

9سپس ملكهٔ سبا به سليمان هدايای فراوانی داد. اين هدايا عبارت بودند از: چهار تن طلا، مقدار زيادی عطريات بی‌نظير و سنگهای گرانبها.

10(ملوانان كشتيهای حيرام پادشاه و سليمان پادشاه از اوفير، طلا، سنگهای گرانبها و چوب صندل آوردند. 11سليمان پادشاه از همين چوبهای صندل، پلكان خانهٔ خداوند و كاخ سلطنتی خود را ساخت و برای دستهٔ نوازندگان نيز از اين چوب، عود و بربط درست كرد. تا به آن روز چنين چوبهای مرغوبی در سراسر سرزمين يهودا ديده نشده بود.)

12سليمان پادشاه علاوه بر چيزهايی كه خود ملكهٔ سبا خواست، هدايايی به ارزش همان هدايايی كه برايش آورده بود، به او داد. سپس ملكهٔ سبا و همراهانش به مملكت خويش بازگشتند.

ثروت و شهرت سليمان

(اول پادشاهان 10‏:14‏-25)

13‏-14سليمان پادشاه علاوه بر دريافت ماليات و سود بازرگانی، هر سال بيست و سه تن طلا هم عايدش می‌شد. پادشاهان عرب و حاكمان سرزمين اسرائيل نيز طلا و نقره برای سليمان می‌آوردند. 15سليمان از اين طلا دويست سپر بزرگ، هر كدام به وزن سه و نيم كيلو 16و سيصد سپر كوچک، هر يک به وزن دو كيلو ساخت. پادشاه اين سپرها را در تالار بزرگ قصر خود كه «جنگل لبنان» نام داشت، گذاشت.

17او يک تخت سلطنتی بزرگ نيز از عاج با روكش طلای ناب ساخت. 18اين تخت شش پله، و يک زيرپايی متصل به تخت داشت. در دو طرف تخت دو دسته بود كه كنار هر دسته، يک مجسمهٔ شير قرار داشت. 19در دو طرف هر يک از پله‌ها نيز دو مجسمهٔ شير نصب شده بود. اين تخت در تمام دنيا بی‌نظير بود!

20همهٔ جامهای سليمان و ظروف تالار «جنگل لبنان» از طلای خالص بود. در ميان آنها حتی يک ظرف نقره هم پيدا نمی‌شد، چون طلا به حدی فراوان بود كه ديگر نقره ارزشی نداشت!

21كشتيهای تجاری سليمان پادشاه با كمک ملوانان حيرام هر سه سال يک بار با بارهای طلا، نقره، عاج، ميمون و طاووس وارد بنادر اسرائيل می‌شدند. 22سليمان از تمام پادشاهان دنيا ثروتمندتر و داناتر بود. 23پادشاهان دنيا مشتاق ديدن سليمان بودند تا شاهد حكمتی باشند كه خدا به او داده بود. 24هر سال عده‌ای به ديدن او می‌آمدند و با خود هدايايی از طلا و نقره، لباس، عطريات، اسلحه، اسب و قاطر برايش می‌آوردند.

25علاوه بر اين، سليمان در پايتخت خود اورشليم و ساير شهرها چهار هزار آخور اسب و محل نگهداری عرابه‌ها و دوازده هزار اسب داشت.

26او بر همهٔ پادشاهان و سرزمينهای آنها از رود فرات تا مملكت فلسطين و از آنجا تا مرز سرزمين مصر فرمانروايی می‌كرد. 27در روزگار سليمان در اورشليم، نقره مثل ريگ بيابان فراوان بود و الوارهای گرانبهای سرو، مانند چوب معمولی مصرف می‌شد! 28اسبهای سليمان را از مصر و كشورهای ديگر می‌آوردند.

مرگ سليمان

(اول پادشاهان 11‏:41‏-43)

29شرح بقيهٔ رويدادهای دوران سلطنت سليمان، از اول تا آخر، در كتاب «تاريخ ناتان نبی»، «نبوت اخيای شيلونی» و «روياهای يعدوی نبی» كه وقايع يربعام پسر نباط را نيز در بر دارد، نوشته شده است. 30سليمان مدت چهل سال در اورشليم بر تمام اسرائيل سلطنت كرد. 31وقتی مرد، او را در شهر پدرش داوود دفن كردند و پسرش رحبعام به جای او پادشاه شد.