2 Mbiri 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 5:1-14

1Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.

Bokosi la Chipangano Libweretsedwa mʼNyumba ya Mulungu

2Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide. 3Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.

4Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano, 5ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula, 6ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.

7Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi. 8Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira. 9Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino. 10Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.

11Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera. 12Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi. 13Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti,

“Yehova ndi wabwino;

chikondi chake chikhala mpaka muyaya.”

Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo, 14choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 5:1-14

1Solomon finished all the work for the Lord’s temple. Then he brought in the things his father David had set apart for the Lord. They included the silver and gold and all the objects for God’s temple. Solomon placed them there with the other treasures.

The Ark Is Brought to the Temple

2Then Solomon sent for the elders of Israel. He told them to come to Jerusalem. They included all the leaders of the tribes. They also included the chiefs of the families of Israel. Solomon wanted them to bring up the ark of the Lord’s covenant from Zion. Zion was the City of David. 3All the Israelites came together to where the king was. It was at the time of the Feast of Booths. The feast was held in the seventh month.

4All the elders of Israel arrived. Then the Levites picked up the ark and carried it. 5They brought up the ark. They also brought up the tent of meeting and all the sacred things in the tent. The priests, who were Levites, carried up everything. 6The entire community of Israel had gathered around King Solomon. All of them were in front of the ark. They sacrificed huge numbers of sheep and cattle. There were so many animals that they couldn’t be recorded. In fact, they couldn’t even be counted.

7The priests brought the ark of the Lord’s covenant to its place in the Most Holy Room of the temple. They put it under the wings of the cherubim. 8The cherubim’s wings were spread out over the place where the ark was. They covered the ark. They also covered the poles used to carry it. 9The poles reached out from the ark. They were so long that their ends could be seen from in front of the Most Holy Room. But they couldn’t be seen from outside the Holy Room. They are still there to this day. 10There wasn’t anything in the ark except the two tablets. Moses had placed them in it at Mount Horeb. That’s where the Lord had made a covenant with the Israelites. He made it after they came out of Egypt.

11The priests left the Holy Room. All the priests who were there had set themselves apart to the Lord. It didn’t matter what group they were in. 12All the Levites who played music stood near the east side of the altar. They included Asaph, Heman, Jeduthun and their sons and relatives. They were dressed in fine linen. They were playing cymbals, harps and lyres. They were joined by 120 priests who were blowing trumpets. 13The trumpet players and other musicians played their instruments together. They praised the Lord and gave thanks to him. The singers sang to the music of the trumpets, cymbals and other instruments. They sang in praise to the Lord,

“The Lord is good.

His faithful love continues forever.”

Then a cloud filled the temple of the Lord. 14The priests couldn’t do their work. That’s because the cloud of the Lord’s glory filled God’s temple.