2 Mbiri 35 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 35:1-27

Yosiya Achita Chikondwerero cha Paska

1Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba. 2Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova. 3Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli. 4Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.

5“Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba. 6Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”

7Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.

8Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300. 9Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.

10Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira. 11Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo. 12Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe. 13Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse. 14Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.

15Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.

16Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya. 17Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri. 18Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu. 19Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.

Imfa ya Yosiya

20Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye. 21Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”

22Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.

23Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.” 24Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.

25Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.

26Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova, 27zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 35:1-27

Josias célèbre la Pâque

1Josias célébra la Pâque à Jérusalem en l’honneur de l’Eternel, et l’on immola les agneaux pour cette fête le quatorzième jour du premier mois35.1 La fête est célébrée à la date réglementaire (Lv 23.5).. 2Il rétablit les prêtres dans leurs fonctions et il les encouragea dans leur service du temple de l’Eternel. 3Puis il s’adressa aux lévites chargés d’enseigner tout le peuple d’Israël et qui étaient consacrés à l’Eternel. Il leur dit : Déposez le coffre sacré dans le temple que Salomon, fils de David, roi d’Israël, a construit. Maintenant vous n’avez plus à le transporter sur vos épaules. Servez l’Eternel votre Dieu et son peuple Israël. 4Organisez-vous en vous répartissant par groupes familiaux et selon vos classes, d’après les instructions écrites de David, le roi d’Israël, et de son fils Salomon35.4 Voir 1 Ch 23 à 26 ; 2 Ch 8.14.. 5Occupez vos postes dans le sanctuaire de façon à faire correspondre une classe de groupe familial lévitique à chaque subdivision des groupes familiaux de vos compatriotes, les gens du peuple. 6Immolez les agneaux de la Pâque. Purifiez-vous rituellement et préparez la Pâque pour vos compatriotes35.6 Autre traduction : et aidez vos compatriotes à agir. selon la parole de l’Eternel, transmise par l’intermédiaire de Moïse.

7Josias préleva pour la Pâque trente mille agneaux et chevreaux ainsi que trois mille bœufs sur ses propres troupeaux pour tous les gens du peuple qui se trouvaient à Jérusalem. 8Ses grands firent aussi volontairement des dons au peuple, aux prêtres et aux lévites. Hilqiya, Zacharie et Yehiel, les responsables du Temple, donnèrent aux prêtres deux mille six cents agneaux et chevreaux pour la Pâque ainsi que trois cents bœufs. 9Konania et ses frères Shemaya et Netanéel, Hashabia, Yeïel et Yozabad, chefs des lévites, fournirent aux lévites cinq mille agneaux et chevreaux pour la Pâque et cinq cents bœufs.

10Voici comment la cérémonie fut organisée : les prêtres se tinrent à leur poste et les lévites étaient répartis selon leur classe conformément aux ordres du roi. 11Ils immolèrent les agneaux de la Pâque. Les lévites remettaient aux prêtres le sang des animaux pour qu’ils le répandent sur l’autel, puis ils ôtaient la peau des victimes. 12Ils mettaient de côté les parties des bêtes qui devaient être offertes en holocaustes pour les donner aux différentes subdivisions des groupes familiaux afin qu’ils les offrent à l’Eternel comme cela est prescrit dans le livre de Moïse. On fit de même pour le gros bétail. 13Ils firent rôtir les agneaux de la Pâque au feu, selon le rituel prescrit35.13 Voir Ex 12.8-9., tandis que les offrandes consacrées furent cuites dans des chaudières, des chaudrons et des poêles pour être ensuite rapidement distribuées à tous les gens du peuple. 14Enfin, les lévites préparèrent la Pâque pour eux-mêmes et pour les prêtres, car les prêtres descendants d’Aaron furent occupés jusqu’à la nuit à offrir les holocaustes et les graisses. C’est pourquoi les lévites préparèrent la Pâque pour eux-mêmes et pour les prêtres descendants d’Aaron.

15Les musiciens descendants d’Asaph étaient à leur poste selon les directives de David, d’Asaph, d’Hémân et de Yedoutoun, le prophète du roi. Les portiers aussi étaient à chaque porte ; ils n’eurent pas à interrompre leur service, car leurs collègues lévites firent les préparatifs pour eux. 16Ainsi furent organisées ce jour-là toutes les cérémonies en l’honneur de l’Eternel pour célébrer la Pâque et pour offrir les holocaustes sur l’autel de l’Eternel, conformément aux ordres du roi Josias.

17Les Israélites qui se trouvaient là célébrèrent la Pâque à ce moment-là et la fête des Pains sans levain pendant sept jours35.17 Voir Ex 12.1-20..

(2 R 23.22-23)

18Aucune Pâque semblable n’avait été célébrée en Israël depuis l’époque du prophète Samuel. Aucun des rois d’Israël n’avait organisé de célébration de la Pâque comparable à la Pâque célébrée par Josias avec l’aide des prêtres et des lévites, avec tout Juda et ceux d’Israël qui se trouvaient là, ainsi que les habitants de Jérusalem. 19Ce fut dans la dix-huitième année du règne de Josias que cette Pâque fut célébrée35.19 L’année même où le livre de la Loi fut découvert (voir v. 8)..

La fin de Josias

(2 R 23.28-30)

20Après tous ces événements, après que Josias eut remis le Temple en état, Néko35.20 En 609 av. J.-C., le pharaon Néko est parti combattre les Babyloniens pour secourir les Assyriens, ses alliés., roi d’Egypte, partit en guerre à Karkemish sur l’Euphrate35.20 Une grande ville sur la rive ouest de l’Euphrate, une capitale hittite, centre du commerce d’Asie occidentale.. Josias se mit en campagne pour lui barrer la route. 21Mais Néko lui envoya des messagers pour lui dire : Roi de Juda, qu’avons-nous à faire ensemble ? Ce n’est pas contre toi que je me suis mis en campagne aujourd’hui. C’est contre une autre dynastie que je suis en guerre. Dieu m’a ordonné de me dépêcher. Garde-toi de t’opposer à Dieu qui est avec moi, sinon il te détruira.

22Mais Josias ne voulut pas se retirer, et il se déguisa pour aller l’affronter sans tenir compte de l’avertissement de Néko, qui était pourtant inspiré par Dieu. Il vint livrer bataille dans la vallée de Meguiddo35.22 Antique et classique champ de bataille dans la plaine d’Esdrelon (voir Jg 5.19 ; 1 R 9.15-19 ; 2 R 9.27).. 23Au cours du combat, les archers l’atteignirent. Le roi dit à ses serviteurs : Emmenez-moi, car je suis grièvement blessé.

24Ses officiers le descendirent de son char de combat, le mirent sur son second char et le conduisirent à Jérusalem. Il mourut et fut enterré dans les tombeaux de ses ancêtres. Tout Juda et Jérusalem prirent le deuil pour Josias. 25Jérémie composa une complainte funèbre sur lui. Tous les chanteurs et toutes les chanteuses célèbrent Josias dans leurs complaintes jusqu’à ce jour, car c’est devenu une tradition en Israël. Ces chants sont consignés dans le recueil des complaintes.

26Les autres faits et gestes de Josias et ses actes de piété qu’il a accomplis conformément à ce qui est écrit dans la Loi de l’Eternel, 27ses actes, des premiers aux derniers, tout cela est cité dans le livre des rois d’Israël et de Juda.