2 Mbiri 31 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 31:1-21

1Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.

Zopereka ku Ntchito ya Chipembedzo

2Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova. 3Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova. 4Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova. 5Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse. 6Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu. 7Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri. 8Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.

9Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi; 10ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”

11Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika. 12Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake. 13Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.

14Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika. 15Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.

16Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo. 17Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo. 18Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.

19Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.

20Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake. 21Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 31:1-21

1The Passover Feast came to an end. The people of Israel who were in Jerusalem went out to the towns of Judah. They smashed the sacred stones. They cut down the poles used to worship the female god named Asherah. They destroyed the high places and the altars. They did those things all through Judah and Benjamin. They also did them in Ephraim and Manasseh. They destroyed all the objects used to worship other gods. Then the Israelites returned to their own towns and property.

The People Bring Gifts to the Lord

2Hezekiah put the priests and Levites in groups based on their duties. The priests sacrificed burnt offerings and friendship offerings. The Levites served the Lord by giving thanks and singing praises at the gates of his house. 3The king gave some of his own possessions to the temple. He gave them for the morning and evening burnt offerings. He gave them for the burnt offerings for every Sabbath day. He gave them for the burnt offerings for every New Moon feast. And he gave them for the burnt offerings for every yearly appointed feast. He did it in keeping with what is written in the Law of the Lord. 4Hezekiah gave an order to the people who were living in Jerusalem. He commanded them to give to the priests and Levites the share they owed them. Then the priests and Levites could give their full attention to the Law of the Lord. 5The order went out. Right away the people of Israel began to give freely. They gave the first share of the harvest of their grain, fresh wine, olive oil and honey. They also gave the first share of everything else their fields produced. They brought a large amount. It was a tenth of everything. 6Here is what the people of Israel and Judah who lived in the towns of Judah brought. They brought a tenth of their herds and flocks. They also brought a tenth of the holy things they had set apart to the Lord their God. They put them in piles. 7They began doing it in the third month. They finished in the seventh month. 8Hezekiah and his officials came and saw the piles. When they did, they praised the Lord. And they blessed his people Israel.

9Hezekiah asked the priests and Levites about the piles. 10Azariah the chief priest answered him. He said, “The people have been bringing their gifts to the Lord’s temple. Ever since they began to bring them, we’ve had enough to eat. We have even had plenty to spare. That’s because the Lord has blessed his people. So we have a large amount left over.” Azariah was from the family line of Zadok.

11Hezekiah gave orders to prepare storerooms in the Lord’s temple. And it was done. 12The people were faithful. They brought in their offerings and a tenth of everything they produced. They also brought the gifts they had set apart to the Lord. Konaniah the Levite was in charge of everything they brought. His brother Shimei was next in command after him. 13Konaniah and his brother Shimei had helpers who worked with them. Their names were Jehiel, Azaziah, Nahath, Asahel, Jerimoth, Jozabad, Eliel, Ismakiah, Mahath and Benaiah. King Hezekiah and Azariah had appointed them. Azariah was the official in charge of God’s temple.

14Kore the Levite guarded the East Gate. He was in charge of the offerings people chose to give to God. He handed out the offerings made to the Lord. He also handed out the gifts that had been set apart to the Lord. Kore was the son of Imnah. 15Eden, Miniamin, Jeshua, Shemaiah, Amariah and Shekaniah helped Kore. They were faithful in helping him in the towns of the priests. They handed out gifts to their brother priests, group by group. They gave the gifts to old men and young men alike.

16In addition to that, they handed out gifts to the males who were three years old or more. The names of those males were listed in their family history. All of them would enter the Lord’s temple. They would carry out their duties each day. Each group did all the different things it was supposed to do. 17Kore and his Levite companions also handed out gifts to the priests. The priests were listed by their families in their family history. Those Levites also handed out gifts to the Levites who were 20 years old or more. Each group did all the different things it was supposed to do. 18Those groups included all the little ones, the wives, and the sons and daughters of the whole community. All of them were listed in their family history. They were faithful in setting themselves apart to serve the Lord.

19Some of the priests lived in other towns or on farms around their towns. They were from the family line of Aaron. Men were chosen by name to hand out shares to those priests. They gave a share to every male among them. They also gave a share to everyone whose name was written down in the family history of the Levites.

20That’s what Hezekiah did all through Judah. He did what was good and right. He was faithful to the Lord his God. 21He tried to obey his God. He worked for him with all his heart. That’s the way he worked in everything he did to serve God’s temple. He obeyed the law. He followed the Lord’s commands. So he had success.