2 Mbiri 29 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 29:1-36

Mfumu Hezekiya Ayeretsa Nyumba ya Mulungu

1Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.

3Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza. 4Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa 5ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika. 6Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira. 7Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli. 8Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino. 9Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo. 10Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere. 11Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”

12Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito:

Kuchokera ku banja la Kohati,

Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya;

kuchokera ku banja la Merari,

Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli;

kuchokera ku banja la Geresoni,

Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;

13kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani,

Simiri ndi Yeiyeli;

kuchokera kwa zidzukulu za Asafu,

Zekariya ndi Mataniya;

14kuchokera kwa zidzukulu za Hemani,

Yehieli ndi Simei;

kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni,

Semaya ndi Uzieli.

15Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova. 16Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni. 17Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.

18Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse. 19Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”

20Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova. 21Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova. 22Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe. 23Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo. 24Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.

25Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri. 26Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.

27Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli. 28Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.

29Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira. 30Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.

31Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.

32Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova. 33Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000. 34Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe. 35Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza.

Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso. 36Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

New International Version – UK

2 Chronicles 29:1-36

Hezekiah purifies the temple

1Hezekiah was twenty-five years old when he became king, and he reigned in Jerusalem for twenty-nine years. His mother’s name was Abijah daughter of Zechariah. 2He did what was right in the eyes of the Lord, just as his father David had done.

3In the first month of the first year of his reign, he opened the doors of the temple of the Lord and repaired them. 4He brought in the priests and the Levites, assembled them in the square on the east side 5and said, ‘Listen to me, Levites! Consecrate yourselves now and consecrate the temple of the Lord, the God of your ancestors. Remove all defilement from the sanctuary. 6Our parents were unfaithful; they did evil in the eyes of the Lord our God and forsook him. They turned their faces away from the Lord’s dwelling-place and turned their backs on him. 7They also shut the doors of the portico and put out the lamps. They did not burn incense or present any burnt offerings at the sanctuary to the God of Israel. 8Therefore, the anger of the Lord has fallen on Judah and Jerusalem; he has made them an object of dread and horror and scorn, as you can see with your own eyes. 9This is why our fathers have fallen by the sword and why our sons and daughters and our wives are in captivity. 10Now I intend to make a covenant with the Lord, the God of Israel, so that his fierce anger will turn away from us. 11My sons, do not be negligent now, for the Lord has chosen you to stand before him and serve him, to minister before him and to burn incense.’

12Then these Levites set to work:

from the Kohathites:

Mahath son of Amasai and Joel son of Azariah;

from the Merarites:

Kish son of Abdi and Azariah son of Jehallelel;

from the Gershonites:

Joah son of Zimmah and Eden son of Joah;

13from the descendants of Elizaphan:

Shimri and Jeiel;

from the descendants of Asaph:

Zechariah and Mattaniah;

14from the descendants of Heman:

Jehiel and Shimei;

from the descendants of Jeduthun:

Shemaiah and Uzziel.

15When they had assembled their fellow Levites and consecrated themselves, they went in to purify the temple of the Lord, as the king had ordered, following the word of the Lord. 16The priests went into the sanctuary of the Lord to purify it. They brought out to the courtyard of the Lord’s temple everything unclean that they found in the temple of the Lord. The Levites took it and carried it out to the Kidron Valley. 17They began the consecration on the first day of the first month, and by the eighth day of the month they reached the portico of the Lord. For eight more days they consecrated the temple of the Lord itself, finishing on the sixteenth day of the first month.

18Then they went in to King Hezekiah and reported: ‘We have purified the entire temple of the Lord, the altar of burnt offering with all its utensils, and the table for setting out the consecrated bread, with all its articles. 19We have prepared and consecrated all the articles that King Ahaz removed in his unfaithfulness while he was king. They are now in front of the Lord’s altar.’

20Early the next morning King Hezekiah gathered the city officials together and went up to the temple of the Lord. 21They brought seven bulls, seven rams, seven male lambs and seven male goats as a sin offering29:21 Or purification offering; also in verses 23 and 24 for the kingdom, for the sanctuary and for Judah. The king commanded the priests, the descendants of Aaron, to offer these on the altar of the Lord. 22So they slaughtered the bulls, and the priests took the blood and splashed it against the altar; next they slaughtered the rams and splashed their blood against the altar; then they slaughtered the lambs and splashed their blood against the altar. 23The goats for the sin offering were brought before the king and the assembly, and they laid their hands on them. 24The priests then slaughtered the goats and presented their blood on the altar for a sin offering to atone for all Israel, because the king had ordered the burnt offering and the sin offering for all Israel.

25He stationed the Levites in the temple of the Lord with cymbals, harps and lyres in the way prescribed by David and Gad the king’s seer and Nathan the prophet; this was commanded by the Lord through his prophets. 26So the Levites stood ready with David’s instruments, and the priests with their trumpets.

27Hezekiah gave the order to sacrifice the burnt offering on the altar. As the offering began, singing to the Lord began also, accompanied by trumpets and the instruments of David king of Israel. 28The whole assembly bowed in worship, while the musicians played and the trumpets sounded. All this continued until the sacrifice of the burnt offering was completed.

29When the offerings were finished, the king and everyone present with him knelt down and worshipped. 30King Hezekiah and his officials ordered the Levites to praise the Lord with the words of David and of Asaph the seer. So they sang praises with gladness and bowed down and worshipped.

31Then Hezekiah said, ‘You have now dedicated yourselves to the Lord. Come and bring sacrifices and thank-offerings to the temple of the Lord.’ So the assembly brought sacrifices and thank-offerings, and all whose hearts were willing brought burnt offerings.

32The number of burnt offerings the assembly brought was seventy bulls, a hundred rams and two hundred male lambs – all of them for burnt offerings to the Lord. 33The animals consecrated as sacrifices amounted to six hundred bulls and three thousand sheep and goats. 34The priests, however, were too few to skin all the burnt offerings; so their relatives the Levites helped them until the task was finished and until other priests had been consecrated, for the Levites had been more conscientious in consecrating themselves than the priests had been. 35There were burnt offerings in abundance, together with the fat of the fellowship offerings and the drink offerings that accompanied the burnt offerings.

So the service of the temple of the Lord was re-established. 36Hezekiah and all the people rejoiced at what God had brought about for his people, because it was done so quickly.