2 Mbiri 23 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 23:1-21

1Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri. 2Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu, 3msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu.

Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide. 4Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo, 5ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova. 6Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula. 7Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”

8Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite. 9Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu. 10Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.

11Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”

12Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko. 13Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”

14Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,” 15choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.

16Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova. 17Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.

18Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira. 19Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.

20Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka, 21ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 23:1-21

1When Joash was seven years old, Jehoiada showed how strong he was. He made a covenant with the commanders of groups of 100 men. The commanders were Azariah son of Jeroham, Ishmael son of Jehohanan, Azariah son of Obed, Maaseiah son of Adaiah, and Elishaphat son of Zikri. 2They went all through Judah. They gathered together the Levites and the leaders of Israelite families from all the towns. They came to Jerusalem. 3The whole community made a covenant with the new king at God’s temple.

Jehoiada said to them, “Ahaziah’s son will rule over Judah. That’s what the Lord promised concerning the family line of David. 4Here’s what I want you to do. A third of you priests and Levites who are going on duty on the Sabbath day must guard the doors. 5A third of you must guard the royal palace. And a third of you must guard the Foundation Gate. All the other men must guard the courtyards of the Lord’s temple. 6Don’t let anyone enter the temple except the priests and Levites who are on duty. They can enter because they are set apart to the Lord. But all the other men must obey the Lord’s command not to enter. 7The Levites must station themselves around the new king. Each man must have his weapon in his hand. Anyone else who enters the temple must be put to death. Stay close to the king no matter where he goes.”

8The Levites did just as Jehoiada the priest ordered. So did all the men of Judah. Each commander got his men. Some of the men were going on duty on the Sabbath day. Others were going off duty. Jehoiada didn’t let any of the groups go. 9Then he gave weapons to the commanders of the groups. He gave them spears, large shields and small shields. The weapons had belonged to King David. They had been in God’s temple. 10Jehoiada stationed all the men around the new king. Each man had his weapon in his hand. They were standing near the altar and the temple. They stood from the south side of the temple to its north side.

11Jehoiada and his sons brought Ahaziah’s son out. They put the crown on him. They gave him a copy of the covenant. And they announced that he was king. They anointed him. Then they shouted, “May the king live a long time!”

12Athaliah heard the noise of the people running and cheering the new king. So she went to them at the Lord’s temple. 13She looked, and there was the king! He was standing next to his pillar at the entrance. The officers and trumpet players were standing beside the king. All the people of the land were filled with joy. They were blowing trumpets. Musicians with their musical instruments were leading the songs of praise. Then Athaliah tore her royal robes. She shouted, “Treason! It’s treason!”

14Jehoiada the priest sent out the commanders of the groups of 100 men. They were in charge of the troops. He said to them, “Bring her away from the temple between the line of guards. Use your swords to kill anyone who follows her.” The priest had said, “Don’t put her to death at the Lord’s temple.” 15So they grabbed her as she reached the entrance of the Horse Gate on the palace grounds. There they put her to death.

16Then Jehoiada made a covenant. He promised that he, the people and the king would be the Lord’s people. 17All the people went to Baal’s temple. They tore it down. They smashed the altars and the statues of gods. They killed Mattan in front of the altars. He was the priest of Baal.

18Then Jehoiada put the priests, who were Levites, in charge of the Lord’s temple. David had given them their duties in the temple. He had appointed them to sacrifice burnt offerings to the Lord. He wanted them to do it in keeping with what was written in the Law of Moses. David wanted them to sing and be full of joy. 19Jehoiada stationed guards at the gates of the Lord’s temple. No one who was “unclean” in any way could enter.

20Jehoiada took with him the commanders of hundreds, the nobles, the rulers of the people, and all the people of the land. He brought the new king down from the Lord’s temple. They went into the palace through the Upper Gate. Then they seated the king on the royal throne. 21All the people of the land were filled with joy. And the city was calm. That’s because Athaliah had been killed by a sword.