2 Mafumu 9 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 9:1-37

Yehu Adzozedwa Ufumu wa ku Israeli

1Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi. 2Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati. 3Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”

4Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi. 5Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.”

Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?”

Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”

6Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova. 7Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli. 8Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu. 9Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya. 10Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’ ” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.

11Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?”

Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”

12Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.”

Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ ”

13Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”

Yehu Apha Yoramu ndi Ahaziya

14Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu, 15koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.” 16Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.

17Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.”

Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’ ”

18Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’ ”

Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”

Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”

19Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’ ”

Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”

20Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”

21Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli. 22Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?”

Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”

23Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”

24Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo. 25Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti, 26‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”

27Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko. 28Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. 29(Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).

Kuphedwa kwa Yezebeli

30Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera. 31Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”

32Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo. 33Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.

34Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.” 35Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake. 36Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli. 37Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

列王纪下 9:1-37

耶户被立为以色列王

1以利沙先知叫来一个先知,吩咐他:“你要束上腰带,拿着这瓶膏油去基列拉末2到了以后,你去找宁示的孙子、约沙法的儿子耶户,带他离开同僚,进入密室, 3把这瓶膏油倒在他头上,告诉他,‘耶和华说,我膏立你为以色列王。’然后,你要马上开门逃走,不可迟延。”

4于是,那位年轻的先知启程前往基列拉末5到了那里,他看见众将领正坐在一起,便说:“将军,我有话对你说。”耶户说:“你想对我们哪一个说话?”他说:“将军啊,我有话对你说。” 6耶户便站起来,随他进入屋里。他将膏油倒在耶户头上,说:“以色列的上帝耶和华说,‘我膏立你做我以色列子民的王。 7你要杀你主人亚哈的全家,这样我就可以为我的仆人——众先知以及其他仆人报仇,他们被耶洗别杀害。 8亚哈全家必灭亡,我要从以色列铲除他家中所有的男子——不论奴隶还是自由人, 9使他家像尼八的儿子耶罗波安家和亚希雅的儿子巴沙家一样。 10耶洗别的尸体必在耶斯列的田间被狗吃,无人埋葬。’”说完这话,那位年轻的先知便开门逃跑了。

11耶户出来回到同僚那里,一个人问他:“没事吧?那疯子为什么来找你?”耶户答道:“你们认得他,也知道他会说什么。” 12他们说:“我们不知道,你告诉我们吧!”耶户说:“他告诉我,耶和华说膏立我做以色列王。” 13他们连忙将自己的衣服铺在耶户脚下的台阶上,吹响号角,高喊:“耶户做王了!”

以色列王约兰被杀

14宁示的孙子、约沙法的儿子耶户背叛了约兰。当时,约兰率领全体以色列人在基列拉末防御亚兰哈薛15他与哈薛交战受伤后,回到耶斯列养伤。耶户对属下说:“如果你们要我做王,就不要让任何人逃出城去耶斯列报信。” 16于是,耶户驾车去了耶斯列,因为约兰耶斯列养伤,犹大亚哈谢也在那里探望他。

17耶斯列城楼上的哨兵看见耶户的人马朝耶斯列奔来,就报信说:“我见到一队人马!”约兰下令:“派一个骑兵去看看他们是否为平安而来。” 18骑兵出去迎接耶户,对他说:“王问你是否为平安而来。”耶户说:“这与你何干?你跟在我后面。”哨兵禀告说:“骑兵到了那里,却没有回来。” 19王又派一个骑兵到耶户那里,对他说:“王问你是否为平安而来。”耶户说:“这与你何干?你跟在我后面。” 20哨兵又禀告说:“他到了那里,也没有回来。那人驾车很猛,一定是宁示的孙子耶户。”

21约兰下令备车。以色列约兰犹大亚哈谢各乘自己的战车去见耶户。他们和耶户耶斯列拿伯的田里相遇。 22约兰问他:“耶户,你为平安而来吗?”耶户答道:“国中到处都是你母亲耶洗别的偶像和邪术,怎能平安呢?” 23约兰调转车头逃跑,向亚哈谢大喊:“亚哈谢,他反了!” 24耶户张弓搭箭,射中约兰的后背,箭穿透他的心脏,他倒毙在车上。 25耶户对将领毕甲说:“你去把他丢在耶斯列拿伯的田里。还记得吗?你我一起驾车跟随他父亲亚哈的时候,耶和华曾预言亚哈的事说, 26‘我昨天看见拿伯和他儿子们被杀,我必使你在这块田里受到报应,这是耶和华说的。’现在你照耶和华的话,把他丢在这块田里吧。”

27犹大亚哈谢见状,就沿着通往伯哈干的道路逃跑。耶户在后面追,并大喊:“射死他!”他们在以伯莲附近的姑珥坡射伤了亚哈谢。他逃到米吉多后,伤重身亡。 28他的臣仆用车把他的尸体运回耶路撒冷,安葬在大卫城他的祖坟里。

29以色列亚哈的儿子约兰执政第十一年,亚哈谢登基做犹大王。

耶洗别被杀

30耶户去了耶斯列耶洗别闻讯,便梳头描眉,向窗外眺望。 31耶户进城时,耶洗别高声喊道:“谋杀主人的心利啊,平安吗?” 32耶户抬头望着窗口,喊道:“谁拥护我?谁?”有两三个太监从窗口往外看他。 33耶户说:“把她扔下来!”那几个太监便把耶洗别扔下去,血溅在墙壁上和马匹身上。耶户驾车轧过她的身体, 34进入王宫,大吃大喝,然后吩咐部下说:“把那受咒诅的妇人埋了,她毕竟是王的女儿。” 35他们出去埋葬她,却只找到她的头骨、手掌和脚, 36便回去禀告耶户耶户说:“这正应验耶和华借祂仆人提斯比以利亚说的话,‘狗必在耶斯列的田间吃耶洗别的肉, 37耶洗别的尸体必像耶斯列田间的粪便,无人能认出那是耶洗别。’”