2 Mafumu 25 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 25:1-30

1Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo. 2Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya. 3Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya. 4Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba, 5koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika. 6Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo. 7Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.

8Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu. 9Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika. 10Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu. 11Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 12Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.

13Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni. 14Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo. 15Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.

16Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka. 17Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.

18Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo. 19Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo. 20Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula. 21Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha.

Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.

22Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda. 23Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo. 24Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”

25Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa. 26Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.

Kumasulidwa kwa Yehoyakini

27Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27. 28Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni. 29Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake. 30Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

Thai New Contemporary Bible

2พงศ์กษัตริย์ 25:1-30

กรุงเยรูซาเล็มล่มสลาย

(2พศด.36:17-20; ยรม.39:1-10; 40:7-9; 41:1-3,16-18; 52:4-27)

ครั้งนั้นเศเดคียาห์ทรงกบฏต่อกษัตริย์บาบิโลน

1ฉะนั้นกษัตริย์เนบูคัดเนสซาร์แห่งบาบิโลนทรงกรีธาทัพหลวงมารบกับกรุงเยรูซาเล็มในวันที่สิบเดือนที่สิบของปีที่เก้าแห่งรัชกาลกษัตริย์เศเดคียาห์ พระองค์ทรงตั้งค่ายอยู่นอกเมืองแล้วสร้างเชิงเทินล้อมเมืองไว้ 2กรุงเยรูซาเล็มถูกล้อมอยู่จนถึงปีที่สิบเอ็ดแห่งรัชกาลเศเดคียาห์ 3เมื่อถึงวันที่เก้าของเดือนที่สี่25:3 ยรม.52:6กรุงนี้ก็กันดารอาหารอย่างหนักจนไม่มีอาหารรับประทานเลย 4แล้วกำแพงเมืองก็ถูกพังลง ทั้งกองทัพก็หนีไปในเวลากลางคืน ผ่านประตูระหว่างกำแพงสองชั้นใกล้ราชอุทยาน แม้ว่าชาวบาบิโลนล้อมเมืองอยู่ พวกเขาหนีไปยังอาราบาห์25:4 หรือหุบเขาแห่งจอร์แดน 5แต่กองทัพบาบิโลน25:5 หรือเคลเดียเช่นเดียวกับข้อ 13,25 และ 26ไล่ล่ากษัตริย์ และมาทันพระองค์ในที่ราบเยรีโค ส่วนทหารทั้งปวงของเศเดคียาห์แตกหนีกันไปคนละทิศคนละทาง 6และพระองค์ทรงถูกจับกุม พระองค์ทรงถูกคุมตัวมาเข้าเฝ้ากษัตริย์บาบิโลนที่ริบลาห์และรับการตัดสินโทษ 7พวกเขาประหารบรรดาโอรสของเศเดคียาห์ต่อหน้าต่อตาพระองค์ แล้วควักพระเนตรของพระองค์ออกทั้งสองข้าง จองจำพระองค์ด้วยโซ่ตรวนทองสัมฤทธิ์ และคุมพระองค์ไปยังบาบิโลน

8ในวันที่เจ็ดเดือนที่ห้าของปีที่สิบเก้าแห่งรัชกาลกษัตริย์เนบูคัดเนสซาร์แห่งบาบิโลน เนบูซาระดานผู้บัญชาการทหารรักษาพระองค์ ผู้เป็นข้าราชการของกษัตริย์บาบิโลนมายังกรุงเยรูซาเล็ม 9เขาจุดไฟเผาพระวิหารขององค์พระผู้เป็นเจ้า พระราชวัง และบ้านเรือนทุกหลังในเยรูซาเล็ม รวมทั้งอาคารสำคัญทุกแห่ง 10ผู้บัญชาการทหารรักษาพระองค์สั่งการให้กองทัพบาบิโลนทั้งหมดทลายกำแพงรอบกรุงเยรูซาเล็ม 11เนบูซาระดานผู้บัญชาการทหารรักษาพระองค์กวาดต้อนผู้คนที่ยังอยู่ในกรุงนั้น ประชากรอื่นๆ ที่เหลือ และชาวยิวที่ยอมสวามิภักดิ์ต่อกษัตริย์บาบิโลนไปเป็นเชลย 12แต่ผู้บัญชาการทหารรักษาพระองค์ได้ทิ้งประชากรที่ยากจนข้นแค้นที่สุดบางคนไว้ให้ทำสวนองุ่นและทำไร่ไถนา

13ชาวบาบิโลนทำลายเสาหานทองสัมฤทธิ์ทั้งสอง แท่นเคลื่อนที่ และขันสาครทองสัมฤทธิ์ที่พระวิหารขององค์พระผู้เป็นเจ้า และนำทองสัมฤทธิ์ทั้งหมดไปยังบาบิโลน 14พวกเขายังได้นำหม้อ ทัพพี กรรไกรตัดไส้ตะเกียง จานชาม และเครื่องใช้ทองสัมฤทธิ์ทั้งหมดที่ใช้ในพระวิหารไปด้วย 15ผู้บัญชาการทหารรักษาพระองค์ยังได้ริบกระถางไฟเผาเครื่องหอมและอ่างประพรมทั้งหมดที่ทำด้วยทองคำบริสุทธิ์หรือเงินไปด้วย

16ทองสัมฤทธิ์ที่ได้จากเสาหานทั้งสองต้น ขันสาคร และแท่นเคลื่อนที่ซึ่งโซโลมอนทรงสร้างขึ้น เพื่อพระวิหารขององค์พระผู้เป็นเจ้านั้นมีปริมาณมากเกินกว่าที่จะชั่งน้ำหนักได้ 17เสาแต่ละต้นสูง 18 ศอก25:17 คือ ประมาณ 8.1 เมตร และมีข่ายทองสัมฤทธิ์สลับกับผลทับทิมทองสัมฤทธิ์ประดับรอบหัวเสายาว 3 ศอก25:17 คือ ประมาณ 1.3 เมตร

18ผู้บัญชาการทหารรักษาพระองค์ได้จับตัวเสไรอาห์หัวหน้าปุโรหิต เศฟันยาห์รองหัวหน้าปุโรหิต และนายประตูสามคนไว้ 19เขาจับกุมผู้ที่ยังอยู่ในเมืองได้แก่ แม่ทัพ ราชมนตรีห้าคน ราชเลขาผู้เป็นหัวหน้ากองเกณฑ์พล และคนของเขาที่พบในเมืองอีกหกสิบคน 20ผู้บัญชาการเนบูซาระดานได้นำตัวคนทั้งหมดนี้ไปเข้าเฝ้ากษัตริย์บาบิโลนที่ริบลาห์ 21กษัตริย์ก็ให้ประหารคนเหล่านี้ที่ริบลาห์ในเขตฮามัท

ดังนั้นยูดาห์จึงตกเป็นเชลย ต้องถูกพรากจากดินแดนของตน

22กษัตริย์เนบูคัดเนสซาร์แห่งบาบิโลนทรงแต่งตั้งเกดาลิยาห์บุตรอาหิคัมและเป็นหลานชาฟานให้ปกครองประชาชนที่เหลืออยู่ในยูดาห์ 23เมื่อบรรดาเจ้าหน้าที่ของกองทัพกับพวกได้ข่าวว่ากษัตริย์บาบิโลนทรงแต่งตั้งเกดาลิยาห์เป็นผู้ว่าการ ก็พากันมาพบเกดาลิยาห์ที่มิสปาห์ได้แก่ อิชมาเอลบุตรเนธานิยาห์ โยฮานันบุตรคาเรอาห์ เสไรอาห์บุตรทันหุเมทจากเนโทฟาห์และยาอาซันยาห์บุตรคนตระกูลมาอาคาห์กับคนของเขา 24เกดาลิยาห์ยืนยันกับพวกเขาว่า “อย่ากลัวเจ้าหน้าที่ของบาบิโลน จงตั้งรกรากในดินแดนและรับใช้กษัตริย์บาบิโลน แล้วทุกอย่างจะเป็นไปด้วยดี”

25แต่อิชมาเอลบุตรเนธานิยาห์และเป็นหลานเอลีชามาซึ่งเป็นเชื้อพระวงศ์คนหนึ่งไปยังมิสปาห์พร้อมคนอีกสิบคนในเดือนที่เจ็ด และได้สังหารเกดาลิยาห์กับชาวยูดาห์และชาวบาบิโลนที่อยู่ด้วย 26แล้วประชากรทั้งหมดตั้งแต่ผู้น้อยที่สุดจนถึงผู้ใหญ่ที่สุดพร้อมทั้งบรรดาเจ้าหน้าที่กองทัพ ก็หนีไปยังอียิปต์เพราะกลัวชาวบาบิโลน

เยโฮยาคีนได้รับการปลดปล่อย

(ยรม.52:31-34)

27ในปีที่สามสิบเจ็ดของการที่กษัตริย์เยโฮยาคีนแห่งยูดาห์ตกเป็นเชลย ซึ่งเป็นปีที่เอวิลเมโรดัก25:27 มีอีกชื่อหนึ่งว่าอาเมลมาร์ดุค ขึ้นเป็นกษัตริย์บาบิโลน พระองค์ทรงปล่อยเยโฮยาคีนออกจากคุกในวันที่ยี่สิบเจ็ดเดือนที่สิบสอง 28พระองค์ตรัสกับเยโฮยาคีนอย่างอ่อนโยน และให้ประทับนั่งในตำแหน่งที่มีเกียรติกว่ากษัตริย์อื่นๆ ที่ถูกจับมาเป็นเชลยในบาบิโลน 29ฉะนั้นเยโฮยาคีนจึงได้ทรงถอดชุดนักโทษออก และได้ทรงร่วมโต๊ะเสวยกับกษัตริย์เป็นประจำตลอดพระชนม์ชีพ 30กษัตริย์ยังได้ประทานเบี้ยเลี้ยงประจำวันแก่เยโฮยาคีนตลอดพระชนม์ชีพ