2 Mafumu 10 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 10:1-36

Kuphedwa kwa Banja la Ahabu

1Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati, 2“Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo, 3sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”

4Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”

5Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”

6Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.”

Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera. 7Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu. 8Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.”

Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”

9Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani? 10Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.” 11Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.

12Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa, 13Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?”

Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”

14Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.

15Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?”

Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.”

Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake. 16Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.

17Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.

Aneneri a Baala Aphedwa

18Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri. 19Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.

20Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo. 21Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina. 22Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.

23Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.” 24Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”

25Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala. 26Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha. 27Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.

28Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli. 29Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.

30Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.” 31Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.

32Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli, 33kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.

34Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

35Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake. 36Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

4 Царств 10:1-36

Истребление дома Ахава

1В городе Самарии было семьдесят сыновей Ахава. Иеву написал письма и послал их в Самарию к начальникам города10:1 Или: «к начальникам Изрееля»., к старейшинам и воспитателям сыновей Ахава. Он сказал:

2– Как только вы получите это письмо, то раз с вами сыновья вашего господина и у вас есть колесницы и кони, укреплённый город и оружие, 3выберите лучшего и достойнейшего из сыновей вашего господина и посадите его на отцовский престол. А затем сражайтесь за дом господина своего.

4Но они очень испугались и сказали:

– Если ему не смогли противостоять два царя, то как можем мы?

5И распорядитель дворца, правитель города, старейшины и воспитатели послали сказать Иеву:

– Мы твои рабы и сделаем всё, что ты скажешь. Мы не будем никого ставить царём, делай всё, как считаешь нужным.

6Тогда Иеву написал им второе письмо, говоря:

– Если вы на моей стороне и послушны мне, возьмите головы сыновей своего господина и завтра к этому времени приходите ко мне в Изреель.

А царские сыновья, семьдесят человек, были со знатнейшими людьми города, которым было доверено их воспитание. 7Когда пришло письмо, эти люди взяли царских сыновей и закололи их всех. Они положили их головы в корзины и послали к Иеву в Изреель. 8Когда посланец прибыл, он доложил Иеву:

– Принесли головы царских сыновей.

Иеву приказал:

– Сложите их в две кучи у входа в городские ворота до утра.

9На следующее утро Иеву вышел, встал перед народом и сказал:

– Вы невиновны. Это я составил заговор против моего господина и убил его, но кто убил вот этих? 10Итак, знайте, что ни одно слово, которое Вечный изрёк против дома Ахава, не осталось неисполненным. Вечный сделал то, что обещал через Своего раба Ильяса10:10 См. 3 Цар. 21:21-24, 29..

11И перебил Иеву в Изрееле всех, кто ещё оставался от дома Ахава, вместе со всеми его приближёнными, близкими друзьями и священнослужителями, никого не оставив в живых.

12После этого Иеву тронулся в путь к Самарии. В пастушеском Бет-Екеде 13он встретил родственников Охозии, царя Иудеи, и спросил:

– Вы кто?

Они сказали:

– Мы родственники Охозии и вышли приветствовать сыновей царя и сыновей царицы-матери.

14– Взять их живыми! – приказал он.

Их взяли живыми и закололи – сорок два человека, при колодце у Бет-Екеда. Иеву не оставил никого из них в живых.

15Уйдя оттуда, он встретил Ионадава, сына Рехава10:15 См. Иер. 35, где более подробно говорится об учении и жизни рехавитов – движения, основанного Ионадавом., который шёл ему навстречу. Иеву приветствовал его и сказал:

– Так же ли верен ты мне, как я тебе?

– Да, – ответил Ионадав.

– А если да, то дай мне руку, – сказал Иеву.

Он дал ему руку, и Иеву помог ему взойти на колесницу. 16Иеву сказал:

– Едем со мной. Ты увидишь мою ревность о Вечном, – и повёз его в своей колеснице.

17Когда Иеву прибыл в Самарию, он перебил всех, кто оставался там от дома Ахава. Он истребил их по слову, которое Вечный сказал Ильясу.

Истребление служителей Баала

18После этого Иеву собрал весь народ и сказал им:

– Ахав служил Баалу мало – я буду служить ему больше. 19Итак, позовите ко мне всех пророков Баала, всех его служителей и всех его жрецов. Смотрите, чтобы пришли все до одного, потому что я хочу принести Баалу великую жертву. А кто не придёт, тому не жить.

Но Иеву действовал с хитростью, желая истребить служителей Баала. 20Он сказал:

– Объявите праздничное собрание в честь Баала.

И люди возвестили о собрании. 21Иеву послал весть по всему Исраилу, и все служители Баала явились, не осталось ни одного, кто бы не пришёл. Они собирались в храме Баала, пока он не наполнился до предела. 22Иеву сказал хранителю одежд:

– Принеси специальные одежды для всех служителей Баала, – и тот вынес для них одежды.

23Затем Иеву и Ионадав, сын Рехава, вошли в храм Баала. Иеву сказал служителям Баала:

– Поищите и посмотрите, чтобы с вами здесь не было служителей Вечного, а только служители Баала.

24И они вошли, чтобы принести жертвы и всесожжения. А Иеву расставил снаружи восемьдесят человек, предупредив их:

– Если кто из вас позволит кому-нибудь из тех людей, которых я отдаю в ваши руки, спастись, он расплатится за это своей жизнью.

25Как только закончили приносить всесожжение, Иеву сказал стражам и военачальникам:

– Войдите и перебейте их, и пусть никто не спасётся.

И они перебили их мечами. Стражи и военачальники выбросили их тела наружу, а затем прошли во внутреннее святилище храма Баала. 26Они вынесли из храма Баала священный камень и бросили его в огонь. 27Они уничтожили священный камень Баала, разрушили храм Баала и сделали из него отхожее место, как это есть и до сегодняшнего дня.

28Так Иеву искоренил в Исраиле почитание Баала. 29Но он не отвернулся от грехов Иеровоама, сына Невата, к которым тот склонил Исраил, – от поклонения золотым тельцам Вефиля и Дана.

30Вечный сказал Иеву:

– Так как ты поступил хорошо, совершив то, что правильно в Моих глазах, и сделал с домом Ахава всё, как Я хотел, твои потомки до четвёртого поколения будут сидеть на престоле Исраила.

31Но Иеву не следил за тем, чтобы исполнять Закон Вечного, Бога Исраила, от всего сердца. Он не отвернулся от грехов Иеровоама, к которым тот склонил Исраил.

Конец правления Иеву

32В те дни Вечный начал уменьшать территорию Исраила. Хазаил разбил исраильтян по всей их земле 33к востоку от Иордана, всю землю Галаад (уделы Гада, Рувима и Манассы), от города Ароера, что у реки Арнон, через Галаад до Башана.

34Прочие события царствования Иеву, всё, что он сделал, и все его свершения записаны в «Книге летописей царей Исраила».

35Иеву упокоился со своими предками и был похоронен в Самарии. И царём вместо него стал его сын Иоахаз. 36Иеву царствовал над Исраилом в Самарии двадцать восемь лет.