2 Atesalonika 3 – CCL & NCA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 3:1-18

Tipempherereni

1Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu. 2Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro. 3Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo. 4Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani. 5Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.

Awachenjeza za Kusagwira Ntchito

6Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani. 7Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu 8ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense. 9Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire. 10Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”

11Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni. 12Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha. 13Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.

14Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi. 15Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.

Malonje Otsiriza

16Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.

17Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

New Chhattisgarhi Translation (नवां नियम छत्तीसगढ़ी)

2 थिस्‍सलुनीके 3:1-18

पराथना करे खातिर बिनती

1आखिर म, हे भाईमन हो, हमर बर पराथना करव कि परभू के संदेस ह जल्दी बगर जावय अऊ आदर के संग गरहन करे जावय, जइसने कि तुम्‍हर बीच म होय हवय। 2अऊ पराथना करव कि परमेसर ह हमन ला खराप अऊ दुस्‍ट मनखेमन ले बचावय, काबरकि जम्मो झन हमर संदेस ला बिसवास नइं करंय। 3पर परभू ह बिसवास लइक अय अऊ ओह तुमन ला बिसवास म मजबूत करही अऊ दुस्‍ट जन ले बचाही। 4तुम्‍हर बारे म, परभू के ऊपर हमन ला भरोसा हवय कि जऊन बात के हमन तुमन ला हुकूम देथन, ओकर तुमन पालन करत हव अऊ हमेसा करत रहिहू। 5परमेसर के मया अऊ मसीह के धीरज म, परभू ह तुम्‍हर हिरदय ला लगाय रखय।

आलस के बिरोध म चेतउनी

6हे भाईमन हो, हमन तुमन ला परभू यीसू मसीह के नांव म हुकूम देवत हन कि हर ओ भाई ले अलग रहव, जऊन ह आलसी ए अऊ ओ बात के मुताबिक नइं चलय, जऊन ला हमन तुमन ला सिखोय हवन। 7काबरकि तुमन खुदे जानत हव कि तुमन ला कइसने हमर चाल-चलन के नकल करना चाही। जब हमन तुम्‍हर संग रहेंन, त आलसी बनके नइं रहेंन, 8अऊ मुफत म हमन काकरो इहां खाना नइं खायेन। पर हमन लगन अऊ मिहनत ले रात अऊ दिन काम करेन, ताकि तुमन के काकरो ऊपर हमन बोझा झन होवन। 9ए बात नो हय कि हमन ला ए किसम के मदद पाय के हक नइं ए, पर हमन तुम्‍हर आघू म एक नमूना पेस करे बर वइसने करेन कि तुमन ओकर नकल करव। 10जब हमन तुम्‍हर संग रहेंन, त तुमन ला हुकूम देय रहेंन कि कहूं कोनो मनखे काम नइं करय, त ओह खाय घलो झन पावय।

11हमर सुनई म आवत हवय कि तुम्‍हर बीच म कुछू झन आलसी हवंय। ओमन कुछू बुता नइं करंय, पर आने मन के काम म बाधा डारथें। 12परभू यीसू मसीह के नांव म, हमन अइसने मनखेमन ला हुकूम अऊ सलाह देवत हन कि ओमन चुपेचाप अपन काम करंय अऊ अपन कमई के रोटी खावंय। 13अऊ हे भाईमन हो, तुमन भलई के काम करे म कभू झन थकव।

14यदि कोनो, ए चिट्ठी म बताय हमर बात ला नइं मानय, त ओकर ऊपर बिसेस धियान रखव। ओकर संग संगति झन करव ताकि ओह बेजत्ती महसूस करय। 15तभो ले ओला बईरी सहीं झन समझव, पर एक भाई जानके ओला चेतउनी देवव।

आखिरी जोहार

16अब, सांति के परभू ह खुद तुमन ला हर समय अऊ हर किसम ले सांति देवय। परभू तुमन जम्मो झन के संग रहय। 17में पौलुस, अपन हांथ ले ए जोहार लिखत हवंव, जऊन ह कि मोर हर चिट्ठी के पहिचान ए। एहीच किसम ले, मेंह लिखथंव। 18हमर परभू यीसू मसीह के अनुग्रह तुमन जम्मो झन ऊपर बने रहय।