1 Yohane 2 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 2:1-29

1Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo. 2Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.

Chikondi ndi Chidani

3Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake. 4Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi. 5Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye. 6Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.

7Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale. 8Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.

9Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima. 10Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa. 11Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.

12Inu ana okondedwa, ndikukulemberani

popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.

13Inu abambo, ndikukulemberani

popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.

Inu anyamata, ndikukulemberani

popeza kuti munagonjetsa woyipayo.

14Ana okondedwa, ndikukulemberani

chifukwa mumawadziwa Atate.

Abambo, ndikukulemberani

chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.

Inu anyamata, ndikukulemberani

chifukwa ndinu amphamvu.

Mawu a Mulungu amakhala mwa inu

ndipo mumamugonjetsa woyipayo.

Musakonde Dziko Lapansi

15Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate. 16Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi. 17Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya.

Anthu Okana Khristu

18Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza. 19Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.

20Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi. 21Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi. 22Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana. 23Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.

24Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate. 25Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha.

26Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani. 27Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.

Ana a Mulungu

28Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.

29Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約翰一書 2:1-29

1我的孩子們,我寫這些話給你們是為了叫你們不要犯罪。如果有人犯了罪,在父那裡我們有一位護慰者,就是那位義者——耶穌基督。 2祂為我們的罪作了贖罪祭,不只是為我們的罪,也是為全人類的罪。

3我們若遵行上帝的命令,就知道自己認識祂。 4若有人說「我認識祂」,卻不遵行祂的命令,這人是說謊的,他心中沒有真理。 5遵行主話語的人是真正全心愛上帝的人,我們藉此知道自己是在主裡面。 6所以,自稱住在主裡面的,就該在生活中效法基督。

新命令

7親愛的弟兄姊妹,我寫給你們的並不是一條新命令,而是你們起初接受的舊命令,這舊命令就是你們已經聽過的真道。 8然而,我寫給你們的也是新命令,在基督和你們身上都顯明是真實的,因為黑暗漸漸過去,真光已經照耀出來。

9若有人說自己在光明中,卻恨他的弟兄姊妹,他就仍然活在黑暗裡。 10愛弟兄姊妹的人活在光明中,沒有什麼可以絆倒他2·10 沒有什麼可以絆倒他」或譯「他也不會絆倒別人」。11恨弟兄姊妹的人活在黑暗中,走在黑暗中,不知何去何從,因為黑暗弄瞎了他的眼睛。

12孩子們,我寫信給你們,因為靠著祂的名,你們的罪已經得到赦免。 13父老們,我寫信給你們,因為你們認識了從太初就存在的那位。年輕人,我寫信給你們,因為你們已經戰勝了那惡者。

14孩子們,我曾寫信給你們,因為你們認識了父。父老們,我曾寫信給你們,因為你們認識了從太初就存在的那位。年輕人,我曾寫信給你們,因為你們剛強,上帝的道常存在你們心裡,並且你們戰勝了那惡者。

15不要愛世界和世上的事,因為人若愛世界,就不會再有愛父的心了。 16凡屬世界的,如肉體的私慾、眼目的私慾和今生的驕傲都不是從父那裡來的,而是從世界來的。 17這世界和其中一切的私慾都要過去,但遵守上帝旨意的人永遠長存。

防備敵基督者

18孩子們,現在是末世了。你們從前聽說敵基督者要來,其實現在許多敵基督者已經出現了,由此可知,現在是末世了。 19這些人是從我們中間出去的,但他們不屬於我們。他們如果屬於我們,就會留在我們當中了。他們的離去表明他們都不屬於我們。

20你們從那位聖者領受了聖靈2·20 聖靈」希臘文指「膏抹」。,所以你們明白真理。 21我寫信給你們不是因為你們不明白真理,而是因為你們明白真理,並且知道真理裡面絕對沒有謊言。 22誰是說謊的呢?不就是那否認耶穌是基督的嗎?那不承認父和子的就是敵基督者。 23凡否認子的,也否認了父;凡承認子的,也承認了父。

24你們務要把起初所聽見的教導謹記在心,這樣,你們必住在子和父裡面。 25主應許給我們的是永生。 26以上的話是針對那些引誘你們離開正道的人寫的。

順從聖靈

27你們既然從主領受了聖靈,聖靈又住在你們心中,就不需要其他人來教導你們,因為聖靈必會在一切事上指引你們。聖靈的教導是真實的,沒有虛假,你們要按聖靈的教導住在主裡面。 28孩子們,你們要住在主裡面。這樣,當主顯現的時候,就是祂再來的時候,我們便能坦然無懼,不會在祂面前羞愧。 29既然你們知道主是公義的,也該知道所有按公義行事的人都是上帝的兒女。