Mawu a Moyo
1Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu. 2Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. 3Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu. 4Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
Kuyenda mu Kuwunika
5Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse. 6Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi. 7Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
Kuwulula Machimo ndi Kukhululukidwa
8Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi. 9Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse. 10Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.
خدا نور است
1از ابتدا، «كلمهٔ» حياتبخش خدا وجود داشته است، من او را با چشمان خود ديدهام، و سخنان او را شنيدهام؛ من با دستهای خود او را لمس كردهام. 2اين كلمهٔ حياتبخش از جانب خدا آمد و خود را بر ما آشكار فرمود؛ و ما شهادت میدهيم كه او را ديدهايم، يعنی عيسی مسيح را. بلی، او حيات جاودانی است. او نزد خدای پدر بود، اما بعد خود را بر ما آشكار ساخت. 3باز میگويم، ما با شما دربارهٔ چيزی سخن میگوييم كه خودمان ديدهايم و شنيدهايم، تا شما نيز بتوانيد مانند ما با خدای پدر و فرزندش عيسی مسيح، رابطهٔ نزديک داشته باشيد. 4اگر به آنچه در اين نامه مینويسم عمل نماييد، شما نيز همچون ما از شادی لبريز خواهيد شد.
زندگی در نور خدا
5اينست پيغامی كه خدا به ما داده است تا به شما اعلام نماييم: خدا نور است و ذرهای تاريكی در او وجود ندارد. 6پس اگر بگوييم كه با خدا رابطهای نزديک داريم، اما در تاريكی روحانی و در گناه زندگی كنيم، دروغ میگوييم. 7اما اگر ما نيز مانند مسيح در نور حضور خدا زندگی میكنيم، آنگاه با يكديگر رابطهای نزديک داريم و خون عيسی، فرزند خدا، ما را از هر گناه پاک میسازد.
8اگر بگوييم گناهی نداريم، خود را فريب میدهيم و از حقيقت گريزانيم.
9اما اگر گناهان خود را به او اعتراف نماييم، میتوانيم اطمينان داشته باشيم كه او ما را میبخشد و از هر ناراستی پاک میسازد. اين كار خدا كاملاً منصفانه و درست است، زيرا عيسی مسيح برای شستن و پاک كردن گناهان ما، جان خود را فدا كرده است. 10اگر ادعا كنيم كه گناهی از ما سر نزده است، دروغ میگوييم و خدا را نيز دروغگو میشماريم، زيرا خدا میفرمايد كه ما گناهكاريم.