1 Timoteyo 5 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 5:1-25

Malangizo kwa Amayi Amasiye, Akulu Ampingo ndi Akapolo

1Usadzudzule munthu wachikulire mokalipa, koma umuchenjeze ngati abambo ako. Achinyamata uwatenge ngati abale ako. 2Amayi achikulire uwatenge ngati amayi ako ndipo amayi achitsikana uwatenge ngati alongo ako, nʼkuyera mtima konse.

3Uziwachitira ulemu akazi amasiye amene ali okhaokha. 4Koma ngati mkazi wamasiye ali ndi ana ndi zidzukulu, anawo ayambe aphunzira kukwaniritsa udindo wawo pa banja lawo moopa Mulungu, potero akubweza zabwino kwa makolo awo ndi agogo awo. Pakuti zimenezi ndiye zimakondweretsa Mulungu. 5Mkazi wamasiye amene ali yekha ndi wopanda womuthandiza, ameneyo wayika chiyembekezo chake pa Mulungu, ndipo amapemphera kosalekeza usana ndi usiku kuti Mulungu azimuthandiza. 6Koma mkazi wamasiye amene amangokhalira kuchita zosangalatsa moyo wake, wafa kale ngakhale akanali ndi moyo. 7Pereka malangizo amenewa kwa anthu kuti akhale opanda zolakwa. 8Ngati wina sasamalira abale ake, makamaka a mʼbanja mwake mwenimweni, ameneyo wakana chikhulupiriro ndipo ndi woyipa kuposa wosakhulupirira.

9Mayi wamasiye aliyense amene sanakwanitse zaka 60 zakubadwa, asakhale mʼgulu la akazi amasiye. Akhale woti anakwatiwapo ndi mwamuna wake mmodzi yekha. 10Akhale mayi woti amadziwika bwino pa ntchito zake zabwino monga kulera ana, kusamalira alendo, kusambitsa mapazi a anthu a Mulungu, kuthandiza amene ali pa mavuto ndi kudzipereka pa ntchito zonse zabwino.

11Akazi amasiye achitsikana, usawayike mʼgulu limeneli. Pakuti zilakolako zawo zikayamba kuwavutitsa nʼkuwalekanitsa ndi Khristu, amafuna kukwatiwanso. 12Zikatero amadziweruza okha chifukwa aphwanya lonjezo lawo loyamba. 13Komanso amakhala ndi chizolowezi cha ulesi ndi kumangoyenda khomo ndi khomo. Ndipo sikungokhala aulesi kokha komanso kuchita miseche, kududukira za eni ake, kumangokamba zinthu zosayenera kukamba. 14Kotero, ndikulangiza akazi amasiye achitsikana kuti akwatiwe, akhale ndi ana, asamalire makomo awo ndipo asamupatse mdani mpata wonyoza 15Akazi amasiye ena apatuka kale nʼkumatsatira Satana.

16Ngati mayi aliyense wokhulupirira ali ndi akazi amasiye amene akuwasamalira, apitirizebe kuwasamalira ndipo asalemetse mpingo, kuti mpingo uthandize akazi amasiye amene ali okhaokha.

17Akulu ampingo amene amayangʼanira bwino zochitika za mu mpingo, ndi oyenera ulemu wowirikiza, makamaka amene ntchito yawo ndi kulalikira ndi kuphunzitsa. 18Pakuti Mawu a Mulungu amati, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu,” ndi “Wantchito ngoyenera kulandira malipiro ake.” 19Usamamvere mawu oneneza akulu ampingo pokhapokha patakhala mboni ziwiri kapena zitatu. 20Akulu ampingo amene akuchimwa, uwadzudzule poyera kuti ena aphunzirepo.

21Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.

22Usafulumire kusanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa machimo. Usunge bwino kuyera mtima kwako.

23Uleke kumangomwa madzi okha, koma uzimwako vinyo pangʼono chifukwa cha vuto lako la mʼmimba ndi kudwala kwako kwa pafupipafupi.

24Anthu ena machimo awo amaonekeratu poyera, amakafika pa mpando wachiweruzo eni akewo asanakafike. Machimo a anthu ena amabwera mʼmbuyo mwawo. 25Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera, ndipo ngakhale zipande kutero, sizingatheke kubisika.

Persian Contemporary Bible

اول تيموتائوس 5:1-25

1مرد سالخورده را هرگز با خشونت سرزنش نكن، بلكه او را همچون پدر خود با احترام نصيحت نما. با جوانان مثل برادران خود، با محبت سخن بگو. 2با زنان پير مانند مادر خود و با دختران جوان همچون خواهران خود رفتار كن و افكارت درباره ايشان هميشه پاک باشد.

رفتار با بيوه‌زنان، کشيشان و غلامان

3كليسا بايد از بيوه‌زنان مراقبت و نگهداری كند، البته اگر كسی را نداشته باشند كه از ايشان مراقبت نمايد. 4اما اگر فرزندان يا نوه‌هايی دارند، ايشان بايد از آنان نگهداری به عمل آورند، و بياموزند كه نيكوكاری را از خانه شروع كنند و اول از همه، دِين خود را به والدين و اجداد خود ادا نمايند. اين چيزی است كه خدا را خشنود و راضی می‌سازد.

5كليسا بايد از بيوه‌زنانی نگهداری كند كه فقير و بيكس هستند و چشم اميدشان به خداست و وقتشان را بيشتر در دعا صرف می‌كنند؛ 6اما بيوه‌هايی كه بيكار می‌گردند و بدگويی می‌كنند و در پی خوشگذرانی هستند، روح خود را به سوی هلاكت سوق می‌دهند. 7اين بايد جزو مقررات كليسای شما باشد، تا اعضا بدانند چه كاری درست است و آن را انجام دهند.

8اما اگر كسی به احتياجات خويشان و بخصوص اعضای خانوادهٔ خود بی‌توجه باشد، اجازه ندارد خود را مسيحی بخواند؛ چنين شخص از يک كافر هم پستتر است.

9زنان بيوه‌ای كه بيش از ۶۰ سال سن دارند و بيش از يک بار ازدواج نكرده‌اند، بايد نامشان در فهرست بيوه‌زنان كليسا ثبت گردد. 10اين گونه بيوه‌زنان بايد به نيكوكاری معروف بوده، فرزندان خود را به خوبی تربيت كرده باشند؛ بايد نسبت به غريبان مهمان‌نواز بوده، به ايمانداران نيز خدمت كرده باشند و دردمندان و محتاجان را ياری داده و همواره نيكوكار بوده باشند.

11بيوه‌های جوانتر را جزو اين گروه نپذير، چون پس از مدتی ممكن است اميال و غرايز بر ايشان چيره شود و خواهان ازدواج مجدد گردند؛ 12به اين ترتيب، به سبب شكستن پيمان اولشان با مسيح، مورد محكوميت قرار می‌گيرند. 13از اين گذشته، بيوهٔ جوان ممكن است به بيكاری و تنبلی عادت كند، و خانه به خانه بگردد و در مورد اين و آن به بدگويی بپردازد و در كار ديگران فضولی كرده، بيهوده‌گويی نمايد. 14پس به نظر من، بهتر است كه بيوه‌های جوان ازدواج كنند و بچه‌دار شوند و به خانه‌داری بپردازند، تا كسی نتواند از كليسا عيب و ايرادی بگيرد. 15زيرا اينطور كه پيداست، عده‌ای از بيوه‌ها از كليسا روگردان شده، شيطان را پيروی می‌كنند.

16بار ديگر يادآوری می‌كنم كه خويشان هر بيوه‌زن بايد خرج او را بدهند و اين بار را بر دوش كليسا ننهند، تا كليسا بتواند از بيوه‌زنانی نگهداری كند كه هيچكس را ندارند.

17كشيشانی كه امور كليسا را خوب اداره می‌كنند، بايد هم حقوق خوبی دريافت كنند و هم مورد تشويق قرار گيرند، بخصوص آنانی كه در كار موعظه و تعليم كلام خدا، زحمت می‌كشند. 18زيرا كتاب آسمانی می‌فرمايد: «دهان گاوی را كه خرمن می‌كوبد، نبند و بگذار به هنگام كار، از خرمنت بخورد.» در جای ديگر نيز می‌فرمايد: «كسی كه كار می‌كند، بايد حقش را بگيرد.»

19اگر بر يكی از كشيشان اتهامی وارد شود، نپذير مگر آنكه دو يا سه نفر شاهد، آن را تأييد كنند. 20اگر ثابت شد كه گناه كرده است، بايد او را در حضور همه توبيخ كنی تا برای ديگران درس عبرتی باشد.

21در حضور خدا و عيسی مسيح و فرشتگان مقدس، تو را مكلف می‌سازم كه اين دستورالعمل را حتی در مورد كشيشی كه بهترين دوست توست اجرا كنی. رفتارت با همه يكسان باشد و از كسی طرفداری نكن. 22در انتصاب كشيش شتاب نکن، چون ممكن است او گناهی كرده باشد، و تو با اين كارت گناه او را تأييد كنی. مواظب باش كه خود را پاک و مقدس نگاه داری.

23خوبست كه به‌جز آب، گاهی نيز برای ناراحتی معده‌ات، كمی شراب بنوشی، زيرا اغلب بيمار می‌شوی.

24برخی از مردم و حتی بعضی از كشيشان زندگی گناه‌آلودی دارند و همه از آن مطلع هستند. در اين مورد بايد اقدام شديدی به عمل آوری. اما در مورد كسانی كه گناهانشان آشكار نيست، بايد منتظر روز داوری شد تا حقايق آشكار گردد. 25به همين ترتيب، خدمات و اعمال نيک و شريف برخی از كشيشان، بر همه واضح است. اما خدمات برخی ديگر، به تدریج بر همه آشكار خواهد شد.