1 Timoteyo 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 3:1-16

Zowayenereza Oyangʼanira ndi Atumiki

1Mawu woona ndi awa: Ngati munthu akufunitsitsa atakhala woyangʼanira, ndiye kuti akufuna ntchito yabwino. 2Tsono woyangʼanira ayenera kukhala munthu wopanda chotsutsika nacho, mwamuna wa mkazi mmodzi yekha, woganiza bwino, wodziretsa, waulemu, wosamala bwino alendo, wodziwa kuphunzitsa. 3Asakhale chidakwa, asakhale wandewu, koma wofatsa, asakhale wokonda mikangano, kapena wokonda ndalama. 4Akhale wodziwa kusamala bwino banja lake ndi kulera ana ake bwino, kuti akhale omvera ndi aulemu weniweni. 5(Ngati munthu sadziwa kusamala banja lake lomwe, angathe bwanji kusamala mpingo wa Mulungu?) 6Asakhale wongotembenuka mtima kumene kuopa kuti angadzitukumule napezeka pa chilango monga Satana. 7Ayeneranso kukhala munthu wambiri yabwino ndi akunja, kuti anthu asamutonze nagwa mu msampha wa Satana.

8Momwemonso atumiki, akhale anthu oyenera ulemu, woona mtima, osakhala okonda zoledzeretsa, osakonda kupeza zinthu mwachinyengo. 9Ayenera kugwiritsa mozama choonadi cha chikhulupiriro ndi kukhala ndi chikumbumtima chabwino. 10Ayambe ayesedwa kaye, ndipo ngati palibe kanthu kowatsutsa, aloleni akhale atumiki.

11Momwemonso, akazi akhale olemekezeka, osasinjirira koma oganiza bwino ndi odalirika pa chilichonse.

12Mtumiki akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ayenera kukhala wosamalira bwino ana ake ndi onse a pa khomo pake. 13Iwo amene atumikira bwino amakhala ndi mbiri yabwino ndipo amakhala chitsimikizo chachikulu cha chikhulupiriro chawo mwa Khristu Yesu.

Cholinga cha Malangizo a Paulo

14Ngakhale ndili ndi chiyembekezo choti ndifika komweko posachedwapa, ndikukulemberani malangizo awa. 15Ine zina zikandichedwetsa kubwera, mudziwe za mmene anthu ayenera kukhalira mʼNyumba ya Mulungu, imene ndi mpingo wa Mulungu wamoyo, mzati ndi maziko achoonadi. 16Mosakayikira, chinsinsi cha chikhulupiriro chathu chachikulu:

Khristu anaonekera ali ndi thupi la munthu,

Mzimu anamuchitira umboni,

angelo anamuona,

analalikidwa pakati pa mitundu yonse,

dziko lapansi linamukhulupirira,

anatengedwa kupita kumwamba mwa ulemerero.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提摩太前書 3:1-16

監督與執事的資格

1「人若渴望做教會的監督,他是在愛慕尊貴的工作。」這句話千真萬確。 2作監督的人必須無可指責,只有一位妻子,為人節制自律、通情達理、受人尊敬、樂於接待客旅、善於教導, 3不酗酒、不好鬥、要溫和、不爭吵、不貪財, 4善於管理自己的家,受兒女的敬重和孝順。 5一個人要是不懂得管理自己的家,又怎能照顧上帝的教會呢? 6初信主的人不可作監督,免得他自高自大,遭受魔鬼所受的懲罰。 7作監督的在教會以外也必須有好名聲,以免被人指責,陷入魔鬼的圈套。

8同樣,做執事的也要品行端正,說話誠實,不好酒,不貪財, 9要存著清潔的良心持守奧妙的真道。 10他們要先接受考驗,倘若無可指責,就可以立他們為執事。 11執事的妻子3·11 執事的妻子」或譯「女執事」。也要品行端正,不搬弄是非,為人節制,做事忠心。 12執事只能有一位妻子,他要管好自己的兒女和自己的家。 13盡忠職守的執事能得到好聲譽,也會對基督耶穌有堅定的信心。

奧妙無比的信仰

14我希望能儘快去你那裡,但還是寫信告訴你這些事。 15這樣,如果我行期延誤,你也可以知道在上帝的家中該怎麼做。這家是永活上帝的教會,是真理的柱石和根基。 16毫無疑問,我們偉大的信仰奧妙無比:

祂以肉身顯現,

被聖靈證明為義,

被天使看見,

被傳揚到列邦,

被世人信奉,

被接到天上的榮耀中。