1 Timoteyo 1 CCL – اول تيموتائوس 1 PCB
1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.
2Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro.
Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.
Kutsutsa Aphunzitsi Onyenga
3Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga, 4kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro. 5Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona. 6Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo. 7Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.
8Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino. 9Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena. 10Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona. 11Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.
Chisomo cha Ambuye kwa Paulo
12Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake. 13Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro. 14Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.
15Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa. 16Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. 17Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni.
Ntchito ya Timoteyo
18Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo 19utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka. 20Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.
سلام و درود از پولس
1از طرف من، پولس، رسول و فرستادهٔ عيسی مسيح كه طبق حكم نجات دهندهٔ ما خدا و خداوند و اميدمان عيسی مسيح، برای اين خدمت تعيين شدهام،
2به فرزند حقيقیام در ايمان، تيموتائوس.
از درگاه پدرمان خدا و خداوندمان عيسی مسيح، طالب فيض و رحمت و آرامش برای تو هستم.
مبارزه با تعاليم غلط
3-4همانطور كه هنگام عزيمت به «مقدونيه» خواهش كردم، همچنان از تو میخواهم كه در «اَفَسُس» بمانی و از تعاليم غلطی كه بعضیها میدهند، جلوگيری كنی، و اجازه ندهی كه مردم به داستانها و افسانهها روی آورند و يا خود را با شجرهنامههای طولانی و بیپايان مشغول سازند. اين گونه مسايل، جز ايجاد بحثهای بیثمر، نتيجهٔ ديگری ندارند. اين عقايد و بحثهای پوچ مانع نقشهٔ الهی كه بوسيلهٔ ايمان آشكار میشود، میگردد. 5اما منظور من از اين حكم اينست كه مسيحيان آنجا، از محبتی لبريز شوند كه از دلی پاک و انگيزهای درست و ايمانی اصيل سرچشمه میگيرد.
6اما اين قبيل افراد، اصلاً توجهی به اين امور روحانی ندارند و فقط در پی ايجاد بحث و جدل هستند؛ 7دلشان میخواهد معلم احكام و شريعت شوند، در حالی که كوچكترين دركی از مفهوم واقعی آن ندارند. 8البته شريعت و احكام مذهبی خوب است، به شرطی كه به طرز صحيح و آن گونه كه خدا در نظر دارد، به کار رود. 9اما به هر حال اين احكام به ما كه بوسيلهٔ خدا نجات يافتهايم مربوط نمیشود، بلكه برای قانونشكنان، جنايتكاران، خدانشناسان، گناهكاران و بیدينان است؛ برای آنانی است كه پدر و مادر خود را مورد ضرب و شتم قرار میدهند و يا آدم میكشند. 10بلی، اين احكام داده شد تا نشان دهد كه مرتكبين اين اعمال، جزو گناهكارانند، يعنی زناكاران، همجنسبازان، آدم دزدان، دروغگويان و تمام كسانی كه مرتكب اعمالی برخلاف تعليم صحيح میگردند، 11تعليمی كه مطابق انجيل پرجلال خدای متبارک است، و من نيز برای اعلام آن تعيين شدهام.
لطف خدا نسبت به پولس
12بنابراين، خداوندمان عيسی مسيح را شكر میگويم كه قدرت انجام اين خدمت را به من داد، و مرا لايق شمرد و به اين خدمت گمارد. 13گرچه قبلاً به مسيح كفر میگفتم و مسيحيان را تعقيب میكردم و آزار و شكنجه میدادم، اما خدا بر من رحم فرمود، زيرا نمیدانستم چه میكنم و هنوز مسيح را نشناخته بودم. 14وه كه خداوند ما چه مهربان و پر محبت است! او نشان داد كه چگونه به او ايمان بياورم و از محبت مسيح عيسی لبريز شوم.
15اين حقيقت چقدر عالی است و چقدر آرزو دارم همه آن را بپذيرند كه عيسی مسيح به جهان آمد تا گناهكاران را نجات بخشد. من خود، بزرگترين گناهكاران هستم، 16اما خدا بر من رحم كرد، تا به اين ترتيب عيسی مسيح بتواند مرا به عنوان نمونهای برای ديگران به کار ببرد و نشان دهد كه حتی نسبت به بدترين گناهكاران صبور است، تا ديگران نيز دريابند كه میتوانند زندگی جاويد داشته باشند. 17پس تا زندهام میگويم جلال و حرمت شايستهٔ خدايی است كه پادشاه تمام دورانهاست. او ناديدنی و غيرفانی است. تنها او خداست، و اوست دانای كل. آمين!
وظایف تيموتائوس
18و حال، پسرم، «تيموتائوس»، حكمی كه به تو میدهم اينست: برای خداوند خوب بجنگ، همانگونه كه خداوند قبلاً توسط نبوتها و پيغامها اين را در مورد تو فرموده بود. 19به ايمانی كه به مسيح داری محكم بچسب و وجدان خود را پاک نگاه دار و مطابق ندای آن عمل كن. زيرا بعضی از ندای وجدان خود سرپيچی كرده، به انجام كارهايی دست زدند كه میدانستند درست نيست. به همين علت، بعد از مدتی مخالفت با خدا، ايمان خود را به مسيح از دست دادند. 20«هيمينائوس» و «اسكندر»، دو نمونه از اين قبيل افراد میباشند. ايشان را در چنگ شيطان رها كردم تا تنبيه شوند و درس عبرت گيرند و ديگر باعث رسوايی نام مسيح نگردند.