1 Mbiri 17 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 17:1-27

Lonjezo la Mulungu kwa Davide

1Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”

2Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”

3Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,

4“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’ 5Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena. 6Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’ ”

7Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. 8Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi. 9Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja; 10monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse.

“ ‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako. 11Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake. 12Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya. 13Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo. 14Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’ ”

15Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.

Pemphero la Davide

16Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati,

“Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa? 17Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”

18“Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu. 19Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.

20“Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu. 21Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto? 22Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.

23“Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera, 24kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.

25“Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere. 26Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu. 27Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

New International Reader’s Version

1 Chronicles 17:1-27

God Makes a Promise to David

1David moved into his palace. Then he spoke to Nathan the prophet. He said, “Here I am, living in a house that has beautiful cedar walls. But the ark of the covenant of the Lord is under a tent.”

2Nathan replied to David, “Do what you want to. God is with you.”

3But that night a message came to Nathan from God. He said,

4“Go and speak to my servant David. Tell him, ‘The Lord says, “You are not the one who will build me a house to live in. 5I have not lived in a house from the day I brought Israel up out of Egypt until now. I have moved my tent from one place to another. I have moved my home from one place to another. 6I have moved from place to place with all the Israelites. I commanded their leaders to be shepherds over my people. I never asked any of those leaders, ‘Why haven’t you built me a house that has beautiful cedar walls?’ ” ’

7“So tell my servant David, ‘The Lord who rules over all says, “I took you away from the grasslands. That is where you were taking care of your father’s sheep and goats. I appointed you ruler over my people Israel. 8I have been with you everywhere you have gone. I destroyed all your enemies when you were attacking them. Now I will make you famous. Your name will be just as respected as the names of the most important people on earth. 9I will provide a place where my people Israel can live. I will plant them in the land. Then they will have a home of their own. They will not be bothered anymore. Sinful people will no longer crush them, as they did at first. 10That is what your enemies have done ever since I appointed leaders over my people Israel. But I will bring all your enemies under your control.

“ ‘ “I tell you that I, the Lord, will build a royal house for your family. 11Some day your life will come to an end. You will join the members of your family who have already died. Then I will give you one of your own sons to become the next king after you. I will make his kingdom secure. 12He is the one who will build me a house. I will set up his throne. It will last forever. 13I will be his father. And he will be my son. I took my love away from the man who ruled before you. But I will never take my love away from your son. 14I will place him over my house and my kingdom forever. His throne will last forever.” ’ ”

15Nathan reported to David all the words that the Lord had spoken to him.

David’s Prayer

16Then King David went into the holy tent. He sat down in front of the Lord. He said,

Lord God, who am I? My family isn’t important. So why have you brought me this far? 17I would have thought that you had already done more than enough for me. But now, my God, you have spoken about my royal house. You have said what will happen to it in days to come. Lord God, you have treated me as if I were the most honored man of all.

18“What more can I say to you for honoring me? You know all about me. 19Lord, you have done a wonderful thing. You have given me many great promises. All of them are for my good. They are exactly what you wanted to give me.

20Lord, there isn’t anyone like you. There isn’t any God but you. We have heard about it with our own ears. 21Who is like your people Israel? God, we are the one nation on earth you have saved. You have set us free for yourself. Your name has become famous. You have done great and wonderful things. You have driven out nations to make room for your people. You saved us when you set us free from Egypt. 22You made Israel your very own people forever. Lord, you have become our God.

23“And now, Lord, let the promise you have made to me and my royal house stand forever. Do exactly as you promised. 24When your promise comes true, your name will be honored forever. People will say, ‘The Lord rules over all. He is the God over Israel. He is Israel’s God!’ My royal house will be made secure in your sight.

25“My God, you have shown me that you will build me a royal house. So I can pray to you boldly. 26You, Lord, are God! You have promised many good things to me. 27You have been pleased to bless my royal house. Now it will continue forever in your sight. Lord, you have blessed it. And it will be blessed forever.”