1 Mbiri 14 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 14:1-17

Nyumba ya Davide ndi Banja Lake

1Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu. 2Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.

3Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri. 4Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni, 5Ibihari, Elisua, Elipeleti, 6Noga, Nefegi, Yafiya, 7Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.

Davide Agonjetsa Afilisti

8Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo. 9Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu. 10Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?”

Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”

11Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu. 12Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.

13Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo. 14Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku. 15Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.” 16Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.

17Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.

Thai New Contemporary Bible

1พงศาวดาร 14:1-17

ครอบครัวของดาวิด

(2ซมอ.5:11-16; 1พศด.3:5-8)

1กษัตริย์ฮีรามแห่งเมืองไทระส่งทูตมาเข้าเฝ้าดาวิด พร้อมกับช่างสกัดหินและช่างไม้ และส่งซุงไม้สนซีดาร์มาเพื่อช่วยสร้างพระราชวังของดาวิด 2ดาวิดทรงตระหนักว่าที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงสถาปนาดาวิดเป็นกษัตริย์เหนืออิสราเอล และทรงเชิดชูอาณาจักรของดาวิดอย่างมาก ก็เพื่อเห็นแก่อิสราเอลประชากรของพระองค์

3ที่กรุงเยรูซาเล็มดาวิดทรงมีมเหสีอื่นๆ อีกและมีโอรสธิดามากมาย 4โอรสซึ่งประสูติที่นั่นได้แก่ ชัมมุวา โชบับ นาธัน โซโลมอน 5อิบฮาร์ เอลีชูอา เอลเปเลท 6โนกาห์ เนเฟก ยาเฟีย 7เอลีชามา เบเอลยาดา14:7 เป็นอีกรูปหนึ่งของเอลียาดา และเอลีเฟเลท

ดาวิดพิชิตชาวฟีลิสเตีย

(2ซมอ.5:17-25)

8เมื่อชาวฟีลิสเตียได้ข่าวว่าดาวิดได้รับการเจิมตั้งเป็นกษัตริย์ปกครองอิสราเอล ก็ระดมพลทั้งหมดมาตามหาดาวิด ดาวิดทรงทราบเรื่องจึงออกไปรับมือ 9เมื่อชาวฟีลิสเตียมาถึงและได้บุกเข้าปล้นหุบเขาเรฟาอิม 10ดาวิดจึงทูลถามพระเจ้าว่า “ข้าพระองค์ควรออกไปโจมตีพวกฟีลิสเตียหรือไม่? พระองค์จะทรงมอบพวกเขาไว้ในมือของข้าพระองค์หรือไม่?”

องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสตอบว่า “ไปเถิด เราจะมอบพวกเขาไว้ในมือของเจ้า”

11ดาวิดกับพวกจึงบุกเข้าโจมตีทัพฟีลิสเตียที่บาอัลเปราซิมและมีชัยชนะ ดาวิดตรัสว่า “พระเจ้าทรงถาโถมเข้าใส่ศัตรูของข้าพเจ้าดั่งสายน้ำเชี่ยวด้วยมือของข้าพเจ้า” ที่แห่งนั้นจึงได้ชื่อว่า บาอัลเปราซิม14:11 แปลว่า องค์พระผู้เป็นเจ้าผู้ทรงถาโถมเข้าใส่ 12ชาวฟีลิสเตียทิ้งรูปเคารพของตนไว้ และดาวิดสั่งให้เผาทิ้ง

13ต่อมาชาวฟีลิสเตียมาปล้นหุบเขาแห่งนั้นอีก 14ดาวิดจึงทูลถามพระเจ้าอีกและพระเจ้าตรัสตอบว่า “อย่าบุกโจมตีทางด้านหน้า แต่จงโอบล้อมแล้วรุกเข้าโจมตีทางด้านหน้าของหมู่ต้นยางสน 15เมื่อเจ้าได้ยินเสียงคล้ายเสียงย่ำเท้าบนยอดต้นยางสน จงบุกเข้าโจมตี เพราะเป็นสัญญาณว่าพระเจ้าได้เสด็จไปล่วงหน้าเพื่อเล่นงานกองทัพฟีลิสเตียแล้ว” 16ดังนั้นดาวิดก็ทำตามที่พระเจ้าตรัสสั่ง และทำลายล้างทัพฟีลิสเตียตลอดทางตั้งแต่เมืองกิเบโอนจนถึงเมืองเกเซอร์

17ชื่อเสียงของดาวิดจึงเลื่องลือไปทั่วทุกแดน และองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงทำให้ชนชาติทั้งปวงยำเกรงดาวิด