1 Mafumu 21 – CCL & APSD-CEB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 21:1-29

Munda Wamphesa wa Naboti

1Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya. 2Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”

3Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”

4Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.

5Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”

6Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’ ”

7Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”

8Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake. 9Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti:

“Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu. 10Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”

11Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera. 12Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu. 13Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha. 14Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”

15Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.” 16Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.

17Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti, 18“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake. 19Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’ ”

20Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!”

Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova. 21Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu. 22Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’

23“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’

24“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”

25(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli. 26Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).

27Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.

28Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti, 29“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

Ang Pulong Sa Dios

1 Mga Hari 21:1-29

Ang Ubasan ni Nabot

1Karon, may usa ka tawo nga taga-Jezreel nga ginganlag Nabot. May ubasan siya sa Jezreel tapad sa palasyo ni Ahab nga hari sa Samaria. 2Usa niana ka higayon, miingon si Ahab kang Nabot, “Tungod kay duol sa akong palasyo ang imong ubasan, ihatag na lang kana kanako aron akong himuon nga tamnanan ug mga utan. Bayloan ko kini ug mas maayong ubasan, o kon gusto ka, bayran ko ikaw sa ensakto nga presyo.” 3-4Apan mitubag si Nabot, “Hinaut nga dili gayod itugot sa Ginoo nga ihatag ko kanimo ang gipanunod ko sa akong mga katigulangan.”

Mipauli si Ahab nga naguol ug naglagot tungod sa gitubag ni Nabot kaniya. Mihigda siya nga nagaatubang sa dingding, ug wala mokaon. 5Giadtoan siya ni Jezebel nga iyang asawa ug gipangutana, “Nganong naguol ka? Nganong dili ka mokaon?” 6Mitubag siya sa iyang asawa, “Giingnan ko si Nabot nga paliton ko ang iyang ubasan o kaha bayloan ko kini ug mas maayong ubasan kon gusto siya, apan wala siya mosugot.” 7Miingon si Jezebel, “Dili ba hari ka man sa Israel? Bangon ug kaon! Paglipay kay ihatag ko kanimo ang ubasan ni Nabot nga taga-Jezreel.”

8Busa nagsulat si Jezebel sa ngalan ni Ahab. Giselyohan niya kini sa selyo sa hari, ug gipadala sa mga tigdumala ug sa uban pang mga opisyal sa lungsod diin nagpuyo si Nabot. 9Mao kini ang mensahe sa iyang sulat: “Tigoma ninyo ang mga katawhan aron magpuasa, ug palingkora ninyo si Nabot atubangan sa mga tawo. 10Unya palingkora ninyo atbang kaniya ang duha ka daotang tawo aron sa pag-akusar kaniya nga gitunglo niya ang Dios ug ang hari. Dad-a dayon ninyo si Nabot sa gawas sa lungsod ug batoha hangtod mamatay.”

11Gihimo sa mga tigdumala ug sa uban pang mga opisyal ang giingon kanila ni Jezebel sa sulat. 12Gitigom nila ang mga tawo aron magpuasa ug gipalingkod nila si Nabot atubangan sa mga tawo. 13Unya may miabot nga duha ka daotang tawo ug milingkod atubangan ni Nabot, ug giakusar nila siya atubangan sa mga tawo. Miingon sila, “Gitunglo ni Nabot ang Dios ug ang hari.” Busa gidala nila si Nabot sa gawas sa lungsod ug gibato hangtod namatay. 14Unya nagsulat sila kang Jezebel nga gibato nila si Nabot ug patay na.

15Pagkahibalo ni Jezebel nga patay na si Nabot, miingon siya kang Ahab, “Patay na si Nabot. Busa lakaw ug panag-iyaha ang ubasan ni Nabot nga dili niya ibaligya kanimo.” 16Pagkadungog ni Ahab nga patay na si Nabot, milakaw siya dayon sa pagpanag-iya sa ubasan niini.

17Miingon ang Ginoo kang Elias nga taga-Tishbe, 18“Lakaw ug adtoa si Ahab nga hari sa Israel, nga atua magpuyo sa Samaria. Atua siya sa ubasan ni Nabot aron sa pagpanag-iya niini. 19Ingna siya nga mao kini ang akong giingon: ‘Human mo patya ang tawo, kuhaon mo pa apil ang iyang yuta? Tungod sa imong gihimo, tilapan usab sa mga iro ang imong dugo sa dapit diin gitilapan nila ang dugo ni Nabot.’ ”

20Pagkakita ni Ahab kang Elias miingon siya, “Nakit-an ra gayod ako sa akong kaaway!” Mitubag si Elias, “Oo, mianhi ako kanimo tungod kay gitugyan mo ang imong kaugalingon sa paghimo ug daotan atubangan sa Ginoo! 21Mao kini ang giingon sa Ginoo kanimo: ‘Padad-an ko ikaw ug katalagman. Pamatyon ko ang tanan mong kaliwat nga lalaki, ulipon man o dili. 22Laglagon ko ang imong panimalay sama sa gihimo ko sa panimalay ni Jeroboam nga anak ni Nebat, ug sa panimalay ni Baasha nga anak ni Ahia, tungod kay gipalagot mo ako ug ikaw ang nahimong hinungdan sa pagpakasala sa mga taga-Israel.’

23“Ug mahitungod kang Jezebel, miingon ang Ginoo nga kan-on siya sa mga iro didto sa paril sa Jezreel. 24Ang mga miyembro sa imong panimalay nga mangamatay sa lungsod kan-on sa mga iro, ug ang mangamatay sa uma kan-on sa mga langgam.”

25(Wala gayoy tawo nga sama kang Ahab nga nagtuygan sa iyang kaugalingon sa paghimo ug daotan atubangan sa Ginoo, nga sinulsolan sa iyang asawa nga si Jezebel. 26Gihimo niya ang labing ngil-ad nga butang pinaagi sa pagsimba ug mga dios-dios, sama sa gihimo sa mga Amorihanon nga giabog sa Ginoo gikan niini nga yuta sa pag-abot sa mga Israelinhon.)

27Pagkadungog ni Ahab sa gisulti ni Elias, gigisi niya ang iyang bisti ug nagbistig sako, ug nagpuasa. Natulog siya nga nagbistig sako ug naglakaw-lakaw nga masulob-on.

28Miingon ang Ginoo kang Elias nga taga-Tishbe, 29“Nakita mo ba kon giunsa pagpaubos ni Ahab sa iyang kaugalingon sa akong atubangan? Tungod kay nagpaubos siya, dili ko ipadala ang kalaglagan sa iyang panahon, ipadala ko kini sa iyang panimalay kon ang iya nang anak ang maghari.”