1 Mafumu 1 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 1:1-53

Adoniya Adziyika Kukhala Mfumu

1Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti. 2Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”

3Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu. 4Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.

5Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake. 6(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).

7Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza. 8Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.

9Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda, 10koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.

11Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa? 12Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni. 13Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’ 14Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”

15Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira. 16Batiseba anagwada nalambira mfumu.

Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”

17Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’ 18Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi. 19Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni. 20Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu. 21Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”

22Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa. 23Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.

24Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu? 25Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’ 26Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane. 27Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”

Davide Alonga Ufumu Solomoni

28Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.

29Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse, 30ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”

31Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”

32Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu, 33mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’ 34Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’ 35Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”

36Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero. 37Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”

38Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni. 39Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!” 40Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.

41Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”

42Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”

43Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu. 44Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu, 45ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo. 46Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu. 47Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake, 48inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’ ”

49Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana. 50Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe. 51Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’ ”

52Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.” 53Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

Swedish Contemporary Bible

1 Kungaboken 1:1-53

Salomos regeringstid

(1:1—11:43)

Salomo blir kung

Adonia försöker ta makten

1När kung David blev mycket gammal, var han frusen av sig och kunde inte bli varm hur många filtar man än bredde på honom. 2Hans tjänare sade då till honom: ”Herre, låt oss leta reda på en ung jungfru åt kungen, en som ska ta hand om dig, kung, och sköta om dig! Hon kan ligga i din famn så att du, min herre och kung, blir varm!”

3Man sökte över hela landet för att få tag på en ung, vacker flicka och slutligen fann man Avishag från Shunem som fördes till kungen. 4Hon var mycket vacker och hon tog hand om kungen och passade upp honom, men kungen hade inget intimt umgänge med henne.

5Adonia, vars mor var Haggit, upphöjde sig själv och talade om att han skulle bli kung. Han skaffade sig vagnar och ryttare och femtio män att springa före vagnen. 6Hans far hade aldrig velat gå till rätta med honom och fråga varför han uppförde sig så. Adonia såg mycket bra ut och han var född efter Absalom. 7Han förhandlade med Joav, Serujas son, och prästen Evjatar och de gav honom sitt stöd. 8Men prästen Sadok och Benaja, Jojadas son, profeten Natan, Shimi, Rei och Davids livgarde höll inte med Adonia.

9Adonia offrade får, tjurar och gödkalvar vid Ormstenen nära Rogelkällan. Han bjöd alla sina bröder, kungens söner och alla de män i Juda som var i kungens tjänst. 10Men han bjöd inte in profeten Natan, Benaja, livgardet och sin bror Salomo.

11Då frågade profeten Natan Salomos mor Batseba: ”Känner du till att Haggits son Adonia nu är kung och att vår herre David inte ens vet om det? 12Om du vill rädda ditt eget och din son Salomos liv, så ska du göra som jag råder dig. 13Du ska genast gå till kung David och fråga honom: ’Min herre och kung, har du inte med en ed lovat mig, din tjänarinna, att min son Salomo ska bli kung efter dig och sitta på din tron? Hur kan det då komma sig att Adonia nu blivit kung?’ 14Medan du talar med honom ska jag komma in och bekräfta allt du säger.”

15Batseba gick till den gamle kungen i hans rum där Avishag skötte om honom. 16Batseba bugade sig djupt för honom och böjde knä. David frågade henne: ”Vad önskar du?”

17”Min herre och kung”, svarade hon. ”Du svor inför Herren, din Gud, och lovade mig, din tjänarinna, att min son Salomo skulle efterträda dig på tronen, 18men nu har Adonia blivit kung i stället utan att du ens vet om det! 19Han har offrat oxar, gödkalvar och en mängd får och han har bjudit alla dina söner och prästen Evjatar och Joav, överbefälhavaren för hären, men inte din tjänare Salomo. 20Nu är hela Israels ögon riktade mot dig, min herre och kung, för att du ska kungöra vem som ska efterträda dig på tronen. 21Annars kommer min son Salomo och jag att betraktas som brottslingar så snart du, min herre och kung, är borta och vilar hos dina fäder.”

22Medan hon fortfarande talade med kungen, kom profeten Natan. 23Man meddelade kungen att profeten Natan var där och Natan kom in till kungen. Han bugade sig djupt för kungen med ansiktet mot marken 24och frågade: ”Min herre och kung, har du utsett Adonia att bli kung efter dig? 25I dag har han gått ner och offrat mängder av tjurar, gödkalvar och får och han har inbjudit kungasönerna, befälhavarna för hären och prästen Evjatar. De äter och dricker tillsammans med honom och ropar: ’Länge leve kung Adonia!’ 26Men mig, din tjänare, prästen Sadok och Benaja, Jojadas son, och din tjänare Salomo har han inte bjudit. 27Har detta skett med din vetskap, kung, utan att du sagt ett ord till dina tjänare om vem som ska efterträda dig på tronen?”

David gör Salomo till tronföljare

28”Kalla tillbaka Batseba!” sa David. Batseba kom omedelbart och gick fram till kungen igen.

29Kung David gav då ett löfte under ed: ”Så sant Herren lever, han som har räddat mig från alla faror, 30idag ska jag fullfölja vad jag med ed lovat inför Herren, Israels Gud: din son Salomo ska bli kung efter mig och sitta på min tron.”

31Då bugade sig Batseba djupt inför honom med ansiktet mot marken och sa: ”Må min herre och kung David leva i evighet!”

32”Kalla hit prästen Sadok, profeten Natan och Benaja, Jojadas son”, befallde kungen.

När de kom inför kungen, 33sa han till dem: ”Ta med er mina män och för Salomo till Gichon! Han ska rida på min egen mulåsna. 34Där ska prästen Sadok och profeten Natan smörja honom till kung över Israel. Sedan ska ni blåsa i horn och ropa: ’Länge leve kung Salomo!’ 35För honom sedan tillbaka hit och han ska sätta sig på min tron som den nye kungen i mitt ställe, för jag har utsett honom till furste över Israel och Juda.”

36”Amen! Må Herren min herre kungens Gud bekräfta detta”, svarade Benaja, Jojadas son. 37”Må Herren vara med Salomo på samma sätt som han har varit med dig, min herre och kung David, och må hans rike bli ännu mäktigare än ditt!”

38Prästen Sadok, profeten Natan och Benaja, Jojadas son, gick därifrån med keretéerna och peletéerna och tog med sig Salomo till Gichon och han red på kung Davids egen mulåsna. 39Sadok tog hornet med olja från tältet och smorde Salomo. Man blåste i horn och allt folket ropade: ”Länge leve kung Salomo!”

40Sedan återvände de alla efter honom under flöjtspel och jubelrop så att marken skakade. 41Adonia och hans gäster hörde också all uppståndelsen just som de skulle avsluta sin fest. ”Vad är det för larm som hörs från staden?” frågade Joav när han hörde hornsignalerna.

42Innan han hunnit säga mer, kom prästen Evjatars son Jonatan. ”Kom hit”, sa Adonia. ”En man som du kommer säkert med goda nyheter!” 43”Nej”, ropade Jonatan. ”Vår herre kung David har gjort Salomo till kung! 44Han har skickat med honom prästen Sadok och profeten Natan och Benaja, Jojadas son, keretéerna och peletéerna och de har satt Salomo på kungens mulåsna. 45Sadok och Natan har smort honom till kung i Gichon. Nu har de just kommit tillbaka jublande och hela staden firar det. Det är därför det är ett sådant oväsen. 46Salomo sitter redan på tronen 47och de styrande har kommit för att gratulera vår kung David och säger: ’Må din Gud göra Salomos namn ännu större än ditt och hans välde ännu större än ditt!’ Kung David tillbad Herren på sin bädd 48och sa: ’Välsignad vare Herren, Israels Gud, som har utsett en efterträdare på min tron och låtit mig få se det med egna ögon!’ ”

49Då flydde Adonia och hans gäster i panik åt olika håll. 50I sin fruktan för Salomo rusade Adonia fram till altaret och grep tag i dess horn.

51Man berättade för Salomo: ”Adonia är rädd för kung Salomo och har gripit tag i altarets horn. Han säger: ’Kung Salomo måste svära att han inte dödar mig, sin tjänare, med svärd!’ ” 52Salomo svarade: ”Om han är en uppriktig man kommer inte ett hår på hans huvud att falla till marken, men om han gör något ont måste han dö.”

53Kung Salomo lät hämta Adonia från altaret. När han kom, bugade han sig djupt för kungen, men Salomo sa till honom: ”Ge dig iväg hem!”