1 Akorinto 2 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 2:1-16

1Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. 2Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. 3Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. 4Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, 5kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Nzeru Yochokera kwa Mzimu

6Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. 7Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. 8Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. 9Komabe monga zalembedwa kuti,

“Palibe diso linaona,

palibe khutu linamva,

palibe amene anaganizira,

zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”

10koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake.

Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe. 11Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo. 12Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere. 13Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu. 14Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu. 15Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense. 16Pakuti

“Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye,

kuti akhoza kumulangiza Iye.”

Koma tili nawo mtima wa Khristu.

Knijga O Kristu

1 Korinćanima 2:1-16

1Draga braćo i sestre, kad sam prvi put došao k vama, nisam se služio uzvišenim ni dubokoumnim riječima da vam navijestim Božju poruku. 2Jer odlučio sam među vama ne znati ništa drugo osim Isusa Krista, i to raspetoga. 3Došao sam k vama slab—bojažljivo i drhteći. 4Moj govor i propovijedanje nisu se zasnivali na mudrim i uvjerljivim riječima, nego na djelovanju Svetoga Duha među vama, 5zato da svoju vjeru ne temeljite na ljudskoj mudrosti, nego na Božjoj sili.

6Doduše, kad smo sa zrelim kršćanima, navješćujemo mudrost—ali ne mudrost ovoga svijeta ni takvu mudrost koja bi se svidjela vladarima ovoga svijeta koji su ionako osuđeni na propast. 7Navješćujemo tajnu, skrivenu Božju mudrost koju je Bog namijenio našoj dobrobiti još prije postanka svijeta. 8Vladari ovoga svijeta nisu ju razumjeli—jer da jesu, ne bi raspeli našega Gospodina slave. 9Upravo je to značenje ulomka iz Svetoga pisma:

“Ono što oko još nije vidjelo,

što uho još nije čulo

niti um može zamisliti,

to je Bog pripravio

onima koji ga ljube.”2:9 Izaija 64:3.

10Ali mi to znamo jer nam je Bog otkrio svojim Duhom koji proniče sve, pa tako i Božje dubine. 11Tko može znati misli nekog čovjeka osim njegova vlastitoga čovječjeg duha u njemu? Tako ni Božje misli ne može znati nitko osim Božjega Duha. 12I tog nam je Božjeg Duha (a ne duha svijeta) Bog dao da bismo mogli znati čime nas je obdario. 13Govoreći vam o tomu, ne služimo se riječima ljudske mudrosti, nego riječima koje nam daje Sveti Duh—služeći se riječima Duha da bismo objasnili duhovne istine. 14Ali čovjek tjelesne naravi ne može razumjeti spoznaje koje daje Božji Duh. Njemu se one čine ludošću jer ih valja prosuđivati Duhom. 15Čovjek koji ima Duha može sve prosuđivati, ali drugi nisu kadri prosuđivati njega.

16“Jer tko poznaje Gospodnje misli?

Tko će njemu dati savjet?”2:16 Izaija 40:13.

Ali mi imamo Kristov um.