1 Akorinto 16 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 16:1-24

Ndalama Zothandizira Akhristu a ku Yerusalemu

1Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite. 2Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha. 3Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu. 4Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.

Paulo Afotokoza za Maulendo ake ndi Zina

5Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako. 6Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite. 7Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola. 8Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite, 9pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.

10Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine. 11Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.

12Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.

13Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu. 14Chitani zonse mwachikondi.

15Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale, 16kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka. 17Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane. 18Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.

Mawu Otsiriza

19Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni. 20Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.

21Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.

22Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!

23Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.

24Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.

New International Reader’s Version

1 Corinthians 16:1-24

The Offering for the Lord’s People

1Now I want to deal with the offering of money for the Lord’s people. Do what I told the churches in Galatia to do. 2On the first day of every week, each of you should put some money away. The amount should be in keeping with how much money you make. Save the money so that you won’t have to take up an offering when I come. 3When I arrive, I will send some people with your gift to Jerusalem. They will be people you consider to be good. And I will give them letters that explain who they are. 4If it seems good for me to go also, they will go with me.

What Paul Asks for Himself

5After I go through Macedonia, I will come to you. I will only be passing through Macedonia. 6But I might stay with you for a while. I might even spend the winter. Then you can help me on my journey everywhere I go. 7I don’t want to see you now while I am just passing through. Instead, I hope to spend some time with you, if the Lord allows it. 8But I will stay at Ephesus until the day of Pentecost. 9A door has opened wide for me to do some good work here. There are many people who oppose me.

10Timothy will visit you. Make sure he has nothing to worry about while he is with you. He is doing the work of the Lord, just as I am. 11No one should treat him badly. Send him safely on his way so he can return to me. I’m expecting him to come back along with the others.

12I want to say something about our brother Apollos. I tried my best to get him to go to you with the others. But he didn’t want to go right now. He will go when he can.

13Be on your guard. Remain strong in the faith. Be brave. 14Be loving in everything you do.

15You know that the first believers in Achaia were from the family of Stephanas. They have spent all their time serving the Lord’s people. Brothers and sisters, I am asking you 16to follow the lead of people like them. Follow everyone who joins in the task and works hard at it. 17I was glad when Stephanas, Fortunatus and Achaicus arrived. They have supplied me with what you couldn’t give me. 18They renewed my spirit, and yours also. People like them are worthy of honor.

Final Greetings

19The churches in Asia Minor send you greetings.

Aquila and Priscilla greet you warmly because of the Lord’s love. So does the church that meets in their house.

20All the brothers and sisters here send you greetings.

Greet one another with a holy kiss.

21I, Paul, am writing this greeting with my own hand.

22If anyone does not love the Lord, let a curse be on that person! Come, Lord!

23May the grace of the Lord Jesus be with you.

24I give my love to all of you who belong to Christ Jesus. Amen.