1 Akorinto 14 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 14:1-40

Mphatso ya Uneneri ndi ya Malilime

1Funafunani chikondi, ndikufunitsitsa mphatso zauzimu, makamaka mphatso ya uneneri. 2Pakuti aliyense amene amayankhula malilime sayankhula kwa anthu, koma kwa Mulungu. Zoonadi, palibe amene amamva zimene akunena chifukwa Mzimu ndiye amamuyankhulitsa zachinsinsi. 3Koma amene amanenera amayankhula kwa anthu kuti awapatse mphamvu, awalimbikitse ndi kuwakhazikitsa mtima pansi. 4Iye amene amayankhula malilime amadzilimbikitsa yekha, koma amene amanenera amalimbikitsa mpingo. 5Nʼkanakonda kuti aliyense mwa inu atamayankhula malilime, koma ndi bwino kuti muzinenera. Amene amanenera amaposa amene amayankhula malilime, pokhapokha atatanthauzira kuti mpingo upindule.

6Tsono, abale, mudzapindula chiyani nditabwera kwa inu ndi kukuyankhulani mʼmalilime? Koma mudzapindula ngati nditakubweretserani vumbulutso lina lake, kapena chidziwitso, kapena chiphunzitso. 7Ngakhale mu zinthu zopanda moyo monga chitoliro kapena gitala, zimene zimatulutsa liwu; kodi munthu akhoza kudziwa bwanji nyimbo imene ikuyimbidwa ngati mawu sakumveka mogwirizana bwino? 8Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo? 9Chimodzimodzinso inu. Ngati simungayankhule mawu omveka bwino mʼchiyankhulo chanu, wina angadziwe bwanji chimene mukunena? Muzingodziyankhulira nokha. 10Mosakayika, pali ziyankhulo zosiyanasiyana pa dziko lapansi, koma palibe nʼchimodzi chomwe chimene chilibe tanthauzo. 11Tsono ngati sindingatolepo tanthauzo la zimene wina akuyankhula, ndiye kuti ndine mlendo kwa oyankhulayo ndipo iyeyo ndi mlendo kwa ine. 12Chimodzimodzinso inu. Popeza mumafunitsitsa mphatso za Mzimu, yesetseni kuchita bwino pa mphatso zimene zimamanga mpingo.

13Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena. 14Popeza ngati ndipemphera mʼmalilime, ndi mzimu wanga umene ukupemphera, koma nzeru zanga sizikupindula kanthu. 15Tsono pamenepa nʼkutani? Ndidzapemphera ndi mzimu wanga, komanso ndidzapemphera ndi nzeru zanga. Ndidzayimba ndi mzimu wanga, komanso ndidzayimba ndi nzeru zanga. 16Ngati mutamanda Mulungu mu mzimu, kodi munthu amene wapezeka pakati pa amene akuyankhula zomwe sakumva, adzavomereza bwanji kuti “Ameni” pa pemphero lanu loyamikalo popeza sakumva chimene mukunena? 17Mukhoza kumathokoza mokwanira, koma munthu winayo sanathandizikepo.

18Ndikuyamika Mulungu chifukwa ndimayankhula malilime kuposa nonsenu. 19Koma mu mpingo ndi kwabwino kuti ndiyankhule mawu asanu okha omveka bwino kuti ndilangize bwino ena kusiyana ndikuyankhula mawu ambirimbiri mʼmalilime.

20Abale, lekani kuganiza ngati ana. Mukhale ana pa nkhani ya zoyipa koma mʼmaganizo anu mukhale okhwima. 21Zinalembedwa mʼMalamulo kuti,

“Ndidzayankhula kwa anthu awa,

kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo

ndiponso ndi milomo yachilendo.

Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine,

akutero Ambuye.”

22Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira. 23Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala? 24Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse 25ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”

Kupembedza Mwadongosolo

26Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo. 27Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo. 28Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.

29Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo. 30Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete. 31Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa. 32Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri. 33Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.

Amayi Akhale Chete mu Mpingo

34Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera. 35Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.

36Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha? 37Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye. 38Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.

39Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime. 40Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.

Knijga O Kristu

1 Korinćanima 14:1-40

Darovi govora u jezicima i prorokovanja

1Težite za ljubavlju! Žarko čeznite za duhovnim darovima, posebice za prorokovanjem! 2Jer tko govori u jezicima, Bogu govori; nitko ga, naime, ne razumije jer Duhom govori tajanstvene stvari. 3Tko prorokuje, međutim, govori ljudima: pomaže im da se izgrađuju u Gospodinu, hrabri ih i tješi. 4Tko govori u jezicima, izgrađuje sebe u Gospodinu, ali tko prorokuje, izgrađuje Crkvu.

5Želio bih da svi govorite u jezicima, ali još više da prorokujete. Jer tko prorokuje, veći je od onoga tko govori u drugim jezicima, osim ako to protumači za izgradnju Crkve.

6Draga braćo, kad bih došao i govorio vam drugim jezicima, od kakve bi vam to bilo koristi ako vam ne bih priopćio ni kakvo otkrivenje, ni znanje, ni proroštvo, ni pouku? 7Čak i ako beživotna glazbala—flauta ili lira—ne daju od sebe razgovijetna glasa, kako ćete razabrati što izvode? 8Ili ako trublja ne dade jasna glasa, kako će vojnici znati da se treba spremiti za boj? 9Također, govorite li tuđim jezikom, nerazumljivo, tko će razabrati što govorite? Bit će kao da govorite u vjetar.

10Na svijetu ima toliko različitih jezika i oni koji ih razumiju odlično se na njima sporazumijevaju. 11Ali meni ne znače ništa. Neću razumjeti ljude koji mi tim jezicima govore niti će oni razumjeti mene. 12Kad već tako silno čeznete za duhovnim darovima, molite Boga da vam dade one koji će biti na izgradnju cijeloj Crkvi.

13Zato onaj koji govori jezike, neka moli i za dar tumačenja kako bi ljudima mogao reći i značenje poruke koju je u jezicima dobio. 14Jer ako se molim na jeziku koji ne razumijem, moj se duh moli, ali moj um u tome ne sudjeluje.

15Što mi je dakle činiti? Molit ću se duhom, ali također i umom, riječima koje razumijem. Pjevat ću hvalospjeve duhom, ali i umom. 16Jer ako se moliš Bogu samo duhom, kako će oni koji ne razumiju što govoriš s tobom slaviti Boga te reći “Amen” na tvoju molitvu? 17Izricat ćeš divne hvalospjeve, ali oni drugima neće biti na izgradnju.

18Ja, hvala Bogu, govorim u drugim jezicima više od svih vas. 19Ali na crkvenome sastanku draže mi je izgovoriti pet razumljivih riječi, da i druge poučim, nego izreći bezbroj riječi na drugim jezicima.

20Ne budite, draga braćo i sestre, poput djece u razboritosti glede toga, nego budite djeca po zloći, a zreli pameću. 21U Svetome pismu piše da je Gospodin rekao:

“Govorit ću svom narodu

nepoznatim jezicima

i kroz usne tuđinaca.

Ali čak me ni tada

neće poslušati.”14:21 Izaija 28:11-12.

22Drugi jezici dakle nisu znak zbog kojega će nevjerni povjerovati nego ih ostavlja u nezanju.

Ali proroštvo navodi nevjernike da vjeruju. 23Govore li, primjerice, na crkvenome sastanku svi u drugim jezicima, a uđu nevjernici ili tko neupućen u te stvari, pomislit će da ste poludjeli. 24Ali ako svi prorokujete, a uđe koji nevjernik ili neupućen čovjek, shvatit će da je grešnik i vaše će ga riječi osuditi. 25Dok bude slušao, tajne njegova srca bit će razotkrivene te će pasti na koljena i pokloniti se Bogu i priznati: “Bog je zaista među vama!”

Poziv na red tijekom bogoslužja

26Braćo i sestre, kad se dakle sastanete, netko će imati hvalospjev, netko pouku, netko otkrivenje koje mu je Bog dao, netko će govoriti nepoznatim jezikom, a netko će to tumačiti. Ali sve što činite mora svima biti na izgradnju u Gospodinu. 27Neka nepoznatim jezikom govore samo dvoje ili troje, i to jedan po jedan, a netko neka tumači što govore. 28Ako pak nema nikoga tko bi to znao protumačiti, neka taj šuti u Crkvi i govori samo sebi i Bogu.

29Neka prorokuje samo dvoje ili troje, a zatim neka drugi prosuđuju njihovu poruku. 30Ali ako za čijeg prorokovanja tko drugi dobije objavu od Boga, prvi neka ušuti. 31Tako ćete, jedan po jedan, svi moći prorokovati, da svi budu poučeni i ohrabreni. 32Upamtite da oni koji prorokuju vladaju svojim proročkim duhovima te mogu čekati svoj red. 33Jer Bog nije Bog nereda, nego Bog mira.

Kao i u svim ostalim crkvama, 34žene neka šute na sastancima. Nije im dopušteno govoriti. Neka se u svezi s tim pokore odredbama Zakona. 35Imaju li pitanja, neka doma pitaju svoje muževe jer nije primjereno da žene govore na crkvenim sastancima.

36Mislite li da spoznaja Božje riječi počinje i završava s vama Korinćanima? Jako se varate. 37Tvrdi li tko od vas da je prorok ili da je obdaren duhom, treba znati da je ovo što vam pišem zapovijed samoga Gospodina. 38Tko to ne priznaje, ni Gospodin njega neće priznati.14:38 U nekim rukopisima: Ne znate li to, ostanite u neznanju.

39Zato, braćo i sestre, čeznite za darom prorokovanja i ne branite govoriti drugim jezicima. 40Ali neka sve bude primjereno i uredno.