1 Akorinto 13 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 13:1-13

Kupambana kwa Chikondi

1Ngakhale nditamayankhula mʼmalilime a anthu ndi a angelo, koma ngati ndilibe chikondi, ndili ngati chinganga chaphokoso kapena ngati chitsulo chosokosera. 2Ngati ndili ndi mphatso ya uneneri, nʼkumazindikira zinsinsi ndi kudziwa zonse, ndipo ngati ndili ndi chikhulupiriro chosuntha mapiri, koma wopanda chikondi, ine sindili kanthu. 3Ngati ndipereka zanga zonse kwa osauka ndi kupereka thupi langa kuti alitenthe, koma ngati ndilibe chikondi, ine sindipindula kanthu.

4Chikondi nʼcholeza mtima, chikondi nʼchokoma mtima, chilibe nsanje, sichidzikuza, sichidzitamandira. 5Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga, sichisunga mangawa. 6Chikondi sichikondwera ndi zoyipa koma chimakondwera ndi choonadi. 7Chimatchinjiriza nthawi zonse, chimakhulupirika nthawi zonse, chimakhala ndi chiyembekezo nthawi zonse, chimapirira nthawi zonse.

8Chikondi ndi chosatha. Koma mphatso ya uneneri idzatha, pamene pali kuyankhula malilime adzatha, pamene pali chidziwitso chidzatha. 9Pakuti timadziwa zinthu pangʼono chabe ndipo timanenera pangʼono chabe. 10Koma changwiro chikadzaoneka ndipo chopereweracho chidzatha. 11Pamene ndinali mwana ndinkayankhula ngati mwana, ndinkaganiza ngati mwana, ndinkalingalira ngati mwana. Koma nditakula, zonse zachibwana ndinazisiya. 12Pakuti tsopano tiona zinthu mosaoneka bwino ngati mʼgalasi loonera; kenaka tidzaziona maso ndi maso. Tsopano ndidziwa mosakwanira koma kenaka ndidzadziwa mokwanira, monga mmene Mulungu akundidziwira ine.

13Ndipo tsopano zatsala zinthu zitatu: chikhulupiriro, chiyembekezo ndi chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.

Slovo na cestu

1 Korintským 13:1-13

1Bych jazyky lidskými mluvil i andělskými, a lásky kdybych neměl, učiněn jsem jako měď zvučící anebo zvonec znějící. 2A bychť měl proroctví, a znal všecka tajemství, i všelikého umění došel, a kdybych měl tak velikou víru, že bych hory přenášel, lásky pak kdybych neměl, nic nejsem. 3A kdybych vynaložil na pokrmy chudých všecken statek svůj, a bych vydal tělo své k spálení, a lásky bych jen neměl, nic mi to neprospívá. 4Láska trpělivá jest, dobrotivá jest, láska nezávidí, láska není všetečná, nenadýmá se. 5V nic neslušného se nevydává, nehledá svých věcí, nezpouzí se, neobmýšlí zlého. 6Neraduje se z nepravosti, ale spolu raduje se pravdě. 7Všecko snáší, všemu věří, všeho se naděje, všeho trpělivě čeká. 8Láska nikdy nevypadá, ačkoli proroctví přestanou, i jazykové utichnou, i učení v nic přijde. 9Z částky zajisté poznáváme a z částky prorokujeme. 10Ale jakžť by přišlo dokonalé, tehdyť to, což jest z částky, vyhlazeno bude. 11Dokudž jsem byl dítě, mluvil jsem jako dítě, myslil jsem jako dítě, smýšlel jsem jako dítě, ale když jsem učiněn muž, opustil jsem dětinské věci. 12Nyní zajisté vidíme v zrcadle a skrze podobenství, ale tehdáž tváří v tvář. Nyní poznávám z částky, ale tehdy poznám, tak jakž i známostí obdařen budu. 13Nyní pak zůstává víra, naděje, láska, to tré, ale největší z nich jestiť láska.