以斯拉記 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以斯拉記 1:1-11

塞魯士下令猶太人回國

1波斯塞魯士元年,耶和華為要應驗祂藉耶利米所說的話,就感動波斯塞魯士,使他下詔通告全國:

2波斯塞魯士如此說,『天上的上帝耶和華已把天下萬國都賜給我,祂吩咐我在猶大耶路撒冷為祂建造殿宇。 3你們當中凡是耶和華的子民,都可以去猶大耶路撒冷,為住在耶路撒冷以色列的上帝耶和華建殿,願上帝與他們同在! 4凡留下不回國的人,無論住在哪裡,都要用金銀、財物和牲畜幫助同區那些將要回國的人,此外還要為耶路撒冷的上帝的殿獻上自願獻的禮物。』」

5於是,猶大便雅憫的族長、祭司和利未人——所有被上帝感動的人都準備上耶路撒冷重建耶和華的殿。 6他們周圍的人除了獻上自願獻的禮物外,還拿出銀器、金子、財物、牲畜和珍寶來支持他們。 7巴比倫尼布甲尼撒曾從耶路撒冷耶和華的殿裡帶回珍貴的器皿,放在自己神明的廟裡。波斯塞魯士將這些器皿取出來, 8派財政大臣米提利達如數交給猶大的首領設巴薩9三十個金盤、一千個銀盤、二十九把刀、 10三十個金碗、四百一十個次等銀碗及一千件其他器皿, 11共有五千四百件金銀器皿。被擄者從巴比倫耶路撒冷時,設巴薩把這些器皿一併帶去。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 1:1-11

Koresi Athandiza Ayuda Kubwerera Kwawo

1Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.

2Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti,

“ ‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda. 3Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu. 4Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’ ”

5Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu. 6Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija. 7Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake. 8Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.

9Chiwerengerochi chinali motere:

Mabeseni agolide 30mabeseni asiliva1,000a zopereka2910timiphika tagolide 230timiphika tasiliva 410ziwiya zina 1,000.

11Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.