诗篇 77 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 77:1-20

第 77 篇

患难中的安慰

亚萨的诗,照耶杜顿的做法,交给乐长。

1我呼求上帝,我高声呼求,

上帝垂听我的祷告。

2我在困境中寻求主。

我整夜举手祷告,

我的心无法得到安慰。

3我思想上帝,发出哀叹;

我默想,心灵疲惫不堪。(细拉)

4你使我无法合眼,

我心乱如麻,默然无语。

5我回想从前的日子,

那久远的岁月,

6想起自己夜间所唱的歌。

我沉思默想,扪心自问:

7“难道主要永远丢弃我,

不再恩待我了吗?

8难道祂的慈爱永远消逝了吗?

祂的应许永远落空了吗?

9难道上帝已忘记施恩,

在愤怒中收回了祂的慈爱吗?”(细拉)

10于是我说:“我感到悲伤的是,

至高者已不再彰显大能。”

11耶和华啊,我要回想你的作为,

回想你从前所行的奇事。

12我要默想你所行的一切事,

思想你一切大能的作为。

13上帝啊,你的作为全然圣洁,

有哪个神明像你一样伟大?

14你是行奇事的上帝,

你在列邦中彰显你的大能。

15你以大能救赎了你的子民,

就是雅各约瑟的后代。(细拉)

16上帝啊,海水看见你就战栗,

深渊看见你就颤抖。

17云层倒出雨水,

天上雷霆霹雳,电光四射。

18旋风中传来你的雷声,

你的闪电照亮世界,

大地颤抖震动。

19你的道路穿越海洋,经过洪涛,

但你的足迹无人看见。

20你借着摩西亚伦的手引领你的子民,

如同牧人引领羊群。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 77:1-20

Salimo 77

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

1Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;

ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.

2Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;

usiku ndinatambasula manja mosalekeza

ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

3Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;

ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.

Sela

4Munagwira zikope zanga kuti ndisagone

ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.

5Ndinaganizira za masiku akale,

zaka zamakedzana;

6Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.

Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

7“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?

Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?

8Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?

Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?

9Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?

Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:

zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.

11Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;

Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.

12Ndidzakumbukira ntchito zanu

ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13Njira zanu Mulungu ndi zoyera.

Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?

14Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;

Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.

15Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,

zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.

Sela

16Madzi anakuonani Mulungu,

madzi anakuonani ndipo anachita mantha;

nyanja yozama inakomoka.

17Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,

mu mlengalenga munamveka mabingu;

mivi yanu inawuluka uku ndi uku.

18Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,

mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;

dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19Njira yanu inadutsa pa nyanja,

njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,

ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa

mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.