诗篇 62 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 62:1-12

第 62 篇

唯上帝是拯救

大卫作的训诲诗,交给乐长,照耶杜顿的做法。

1我的心默默等候上帝,

祂是我的拯救者。

2唯有祂才是我的磐石,

我的拯救,我的堡垒,

我必不致动摇。

3我就像一面摇摇欲坠的墙壁、行将倒塌的篱笆,

你们要攻击我、置我于死地到何时呢?

4你们千方百计把我从高位拉下。

你们善于说谎,嘴上祝福,

心却咒诅。(细拉)

5我的心啊!要默默等候上帝,

因为我的盼望从祂而来。

6唯有祂才是我的磐石,

我的拯救,我的堡垒,

我必不致动摇。

7上帝是我的拯救者,

是我的荣耀,

祂是我的坚固磐石,

是我的避难所。

8众百姓啊,

要时刻信靠上帝,

向祂倾心吐意,

因为祂是我们的避难所。(细拉)

9卑贱人不过是一丝气息,

尊贵人不过是一场幻影,

把他们放在天平上一秤,

比空气还轻,毫无分量。

10不要敲诈勒索,

不要妄想靠偷盗发财,

即使财富增多,也不要倚靠它。

11上帝再三告诉我:

祂拥有权能,

12充满慈爱。

主啊,你必照各人的行为来施行赏罚。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.