诗篇 31 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 31:1-24

第 31 篇

信靠上帝的祷告

大卫的诗,交给乐长。

1耶和华啊,我寻求你的庇护,

求你让我永不蒙羞;

你是公义的,求你拯救我。

2求你侧耳听我的呼求,

快来救我,作我坚固的避难所,

作拯救我的堡垒。

3你是我的磐石,我的堡垒,

求你为了自己的名而引导我,带领我。

4你是我的避难所,

求你救我脱离人们为我设下的陷阱。

5我将灵魂交托给你。

信实的上帝耶和华啊,

你必救赎我。

6我憎恨拜假神的人,

我信靠耶和华。

7你已经看见我的困苦,

知道我心中的愁烦,

你的恩慈使我欢喜快乐。

8你没有将我交给仇敌,

而是领我到宽阔之地。

9耶和华啊,我落在苦难之中,

求你怜悯我,

我双眼哭肿,身心疲惫。

10我的生命被愁苦吞噬,

岁月被哀伤耗尽,

力量因罪恶而消逝,

我成了枯骨一堆。

11仇敌羞辱我,

邻居厌弃我,

朋友害怕我,

路人纷纷躲避我。

12我就像已死之人,被人遗忘;

又像破碎的陶器,被人丢弃。

13我听见许多人毁谤我,

惊恐笼罩着我。

他们图谋不轨,

谋害我的性命。

14然而,耶和华啊,

我依然信靠你;

我说:“你是我的上帝。”

15我的时日都掌握在你手中,

求你救我脱离仇敌和追逼我的人。

16求你笑颜垂顾仆人,

施慈爱拯救我。

17耶和华啊,我曾向你呼求,

求你不要叫我蒙羞。

求你使恶人蒙羞,

寂然无声地躺在阴间。

18愿你堵住撒谎之人的口,

他们骄傲自大,

狂妄地攻击义人。

19你的恩惠何其大——为敬畏你的人而预备,

在世人面前赐给投靠你的人。

20你把他们藏在你那里,

使他们得到庇护,

免遭世人暗算。

你使他们在你的居所安然无恙,

免受恶言恶语的攻击。

21耶和华当受称颂!

因为我被困城中时,

祂以奇妙的爱待我。

22我曾惊恐地说:

“你丢弃了我!”

其实你听了我的呼求。

23耶和华忠心的子民啊,

你们要爱祂。

祂保护忠心的人,

严惩骄傲的人。

24凡仰望耶和华的人啊,

要刚强壮胆!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.