箴言 2 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

箴言 2:1-22

智慧的益处

1孩子啊,

你若接受我的教诲,

珍爱我的诫命,

2侧耳聆听智慧,

倾心渴慕悟性;

3你若呼求洞见,

竭力追求悟性,

4寻它如寻银子,

找它如找宝藏,

5你就会懂得敬畏耶和华,

认识上帝。

6因为耶和华赐人智慧,

知识和悟性出自祂的口。

7祂使正直人充满智慧,

是行为纯全者的盾牌。

8祂看守正义之路,

护卫虔诚人的道。

9这样,你就明白何为仁义、

公平和正直,

懂得一切美善之道。

10因为智慧必进入你心,

知识必令你的灵欢快。

11明辨力必护佑你,

悟性必看顾你。

12智慧必救你远离恶道,

脱离言语荒谬的人。

13他们舍弃正道,走上黑路,

14以行恶为乐,喜爱恶人的邪僻;

15他们的道路歪邪,行径扭曲。

16智慧要救你脱离淫妇,

脱离花言巧语的妓女。

17她撇弃了年轻时的丈夫,

忘了在上帝面前立的约。

18她的家通向死亡,

她的路直达阴间。

19到她那里的人都有去无回,

找不到生命之道。

20所以你要行善人的路,

守义人的道。

21因为在地上,

正直人必安居,

纯全无过的人必长存,

22恶人必遭灭绝,

奸徒必被铲除。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 2:1-22

Ubwino Wanzeru

1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga

ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,

2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru

ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;

3ngati upempha kuti uzindikire zinthu

inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,

4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva

ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,

5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;

ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.

6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,

ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.

7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.

Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,

8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.

Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,

kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.

10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,

kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.

11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;

kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,

kwa anthu amabodza,

13amene amasiya njira zolungama

namayenda mʼnjira zamdima,

14amene amakondwera pochita zoyipa

namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.

15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,

ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;

kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,

17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake

ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.

18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;

njira zake zimamufikitsa ku manda.

19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera

kapena kupezanso njira zamoyo.

20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,

uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.

21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko

ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;

22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,

ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.