申命记 8 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

申命记 8:1-20

不可忘记耶和华

1“你们要谨遵我今日吩咐你们的一切诫命,以便能够存活,生养众多,并且得到耶和华起誓要赐给你们祖先的土地。 2要记住这四十年来你们的上帝耶和华怎样在旷野引领你们,祂磨炼你们、考验你们,好知道你们的心意如何、肯不肯遵守祂的诫命。 3祂让你们忍饥挨饿,然后赐给你们祖祖辈辈从未见过的吗哪吃,为了使你们明白人活着不是单靠食物,乃是靠祂口中的每一句话。 4这四十年来,你们的衣服没有穿破,双脚也没有走肿。 5你们心里要明白,你们的上帝耶和华管教你们,如同父亲管教儿子。

6“所以,你们要遵守你们的上帝耶和华的诫命,行祂的道,敬畏祂, 7因为祂要带你们到一个佳美之地。那里的谷中和山间流淌着条条溪流、股股清泉; 8那里盛产大麦、小麦、葡萄、无花果、石榴、橄榄油和蜂蜜; 9那里食物充足,一无所缺;那里矿产资源丰富,石头就是铁,山中可以采铜。 10你们吃饱喝足后,要赞美你们的上帝耶和华,因为祂赐给你们那佳美之地。

11“你们要谨慎,免得忘记你们的上帝耶和华,不遵守我今天吩咐你们的诫命、典章和律例。 12当你们丰衣足食、居室华美、 13牛羊众多、金银日增的时候, 14切勿心骄气傲,忘记你们的上帝耶和华。祂把你们从受奴役之地——埃及救出来, 15带领你们走过干旱、可怕、毒蛇和蝎子出没的大旷野。祂使坚硬的磐石流出水来给你们喝, 16在旷野中把你们祖先从未见过的吗哪赐给你们吃,为要磨炼你们、考验你们,使你们最终得到益处。 17你们切勿以为是凭自己的双手和能力致富的。 18要记住,是你们的上帝耶和华赐给你们致富的能力,为要坚立祂给你们祖先的誓约,正如今日的情形。

19“我今天警告你们,如果你们忘记你们的上帝耶和华,去追随、供奉、祭拜其他神明,你们必灭亡。 20如果你们不听从你们的上帝耶和华,你们必灭亡,正如祂使列国在你们面前灭亡一样。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 8:1-20

Musayiwale Yehova

1Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu. 2Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi. 3Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova. 4Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe. 5Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.

6Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye. 7Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri, 8dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi; 9dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.

10Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani. 11Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, 12kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo, 13ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka, 14mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo. 15Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma. 16Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino. 17Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.” 18Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.

19Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu. 20Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.