申命记 25 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

申命记 25:1-19

1“如果发生纠纷,双方告上法庭,审判官要判明是非。 2如果有罪的一方被判受鞭打,审判官要命令他当场伏在地上,按罪行轻重受刑。 3最多可以鞭打他四十下。如果超过四十下,你们就是在公开羞辱自己的同胞。

4“牛在踩谷时,不可笼住它的嘴。

为死亡的兄弟传宗接代

5“如果兄弟们住在一起,其中一个没有儿子便死了,死者的妻子不可改嫁给外人。死者的兄弟要尽兄弟的责任娶她为妻。 6她生的第一个儿子要算为死者的儿子,免得死者在以色列绝后。 7如果死者的兄弟不愿娶那寡妇,她要到城门口见长老们,告诉他们,‘我丈夫的兄弟不肯尽兄弟的责任娶我,不肯为我丈夫留后。’ 8长老们要把死者的兄弟召来,与他商谈。如果他执意不肯, 9那寡妇要当着众长老的面,上前脱下他的鞋,吐唾沫在他脸上,说,‘这就是不肯为兄弟留后之人的下场。’ 10从此以后,他的家在以色列要被称为‘被脱鞋者之家’。

其他条例

11“如果两个男人打架,其中一人的妻子为帮助丈夫而伸手抓住另外一人的下体, 12就要砍掉她的手,不可怜悯她。

13“你们做买卖时,口袋里不可有一大一小两种砝码, 14家里也不可用一大一小两种量器。 15你们必须诚实无欺,使用同样的砝码和量器,以便在你们的上帝耶和华要赐给你们的土地上得享长寿。 16因为你们的上帝耶和华憎恶行事诡诈的人。

灭绝亚玛力人的命令

17“你们要记住,你们从埃及出来的路上,亚玛力人是怎样对待你们的。 18他们趁你们疲惫不堪时,袭击你们当中掉队的人,毫不敬畏上帝。 19所以,当你们的上帝耶和华赐给你们那片土地作产业、使你们四境安宁时,要灭绝亚玛力人,抹去世人对他们的记忆。你们要切记!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 25:1-19

1Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa. 2Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake, 3koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.

4Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.

5Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo. 6Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.

7Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.” 8Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,” 9mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.” 10Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.

11Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo, 12muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.

13Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka. 14Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono. 15Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. 16Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.

17Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto. 18Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu. 19Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!